< Salme 47 >
1 (Til sangmesteren. Af Koras sønner. En salme.) Alle Folkeslag, klap i Hænderne, bryd ud i jublende Lovsang for Gud!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2 Thi HERREN, den Højeste, er frygtelig, en Konge stor over hele Jorden.
Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3 Han bøjede Folkefærd under os og Folkeslag under vor Fod;
Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4 han udvalgte os vor Arvelod, Jakob hans elskedes Stolthed. (Sela)
Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
5 Gud steg op under Jubel, HERREN under Homets Klang.
Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6 Syng, ja syng for Gud, syng, ja syng for vor Konge;
Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7 thi han er al Jordens Konge, syng en Sang for Gud.
Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
8 Gud har vist, han er Folkenes Konge, på sin hellige Trone har Gud taget Sæde.
Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9 Folkenes Stormænd samles med Folket, der tilhører Abrahams Gud; thi Guds er Jordens Skjolde, højt ophøjet er han!
Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.