< Salme 37 >
1 (Af David.) Græm dig ikke over Ugerningsmænd, misund ikke dem, der gør Uret!
Salimo la Davide. Usamavutike chifukwa cha anthu oyipa kapena kuchitira nsanje amene akuchita cholakwa;
2 Thi hastigt svides de af som Græsset, visner som det friske Grønne.
pakuti monga udzu iwo adzafota msanga, ngati mbewu zobiriwira adzanyala msanga.
3 Stol på HERREN og gør det gode, bo i Landet og læg Vind på Troskab,
Khulupirira Yehova ndipo uzichita zabwino; khazikika mʼdziko ndi kutsata zokhulupirika.
4 da skal du have din Fryd i HERREN, og han skal give dig, hvad dit Hjerte attrår.
Udzikondweretse wekha mwa Yehova ndipo Iye adzakupatsa zokhumba za mtima wako.
5 Vælt din Vej på HERREN, stol på ham, så griber han ind
Pereka njira yako kwa Yehova; dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 og fører din Retfærdighed frem som Lyset, din Ret som den klare Dag.
Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha, chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 Vær stille for HERREN og bi på ham, græm dig ej over den, der har Held, over den, der farer med Rænker.
Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa; usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo, pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Tæm din Harme, lad Vreden fare, græm dig ikke, det volder kun Harm.
Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali, usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 Thi Ugerningsmænd skal ryddes ud, men de, der bier på HERREN, skal arve Landet.
Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa, koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
10 En liden Stund, og den gudløse er ikke mere; ser du hen til hans Sted, så er han der ikke.
Kwa kanthawi oyipa sadzapezekanso; ngakhale muwafunefune, sadzapezekanso.
11 Men de sagtmodige skal arve Landet, de fryder sig ved megen Fred.
Koma ofatsa adzalandira dziko ndipo adzasangalala ndi mtendere waukulu.
12 Den gudløse vil den retfærdige ilde og skærer Tænder imod ham;
Oyipa amakonza chiwembu kutsutsana ndi olungama ndipo amawakukutira mano;
13 men Herren, han ler ad ham, thi han ser hans Time komme.
koma Ambuye amaseka oyipa pakuti Iye amadziwa kuti tsiku lawo likubwera.
14 De gudløse drager Sværdet og spænder Buen for at fælde arm og fattig, for at nedslagte dem, der vandrer ret;
Oyipa amasolola lupanga ndi kupinda uta kugwetsa osauka ndi osowa, kupha iwo amene njira zawo ndi zolungama.
15 men Sværdet rammer dem selv i Hjertet, og Buerne brydes sønder og sammen.
Koma malupanga awo analasa mitima yawo yomwe, ndipo mauta awo anathyoka.
16 Det lidt, en retfærdig har, er bedre end mange gudløses Rigdom;
Zabwino zochepa zimene olungama ali nazo ziposa chuma cha anthu oyipa ambiri;
17 thi de gudløses Arme skal brydes, men HERREN støtter de retfærdige;
pakuti mphamvu ya oyipa idzasweka, koma Yehova amasunga olungama.
18 HERREN kender de uskyldiges Dage, deres Arvelod bliver evindelig;
Masiku a anthu osalakwa amadziwika ndi Yehova, ndipo cholowa chawo chidzakhala mpaka muyaya.
19 de beskæmmes ikke i onde Tider, de mættes i Hungerens Dage.
Pa nthawi ya mavuto iwo sadzafota; mʼmasiku a njala adzakhala ndi zinthu zambiri.
20 Thi de gudløse går til Grunde, som Engenes Pragt er HERRENs Fjender, de svinder, de svinder som Røg.
Koma oyipa adzawonongeka; adani a Yehova adzakhala ngati kukongola kwa kuthengo, iwo adzazimirira ngati utsi.
21 Den gudløse låner og bliver i Gælden, den retfærdige ynkes og giver;
Oyipa amabwereka ndipo sabweza koma olungama amapereka mowolowamanja.
22 de, han velsigner, skal arve Landet, de, han forbander, udryddes.
Iwo amene Yehova amawadalitsa adzalandira dziko, koma amene Iye amawatemberera adzachotsedwa.
23 Af HERREN stadfæstes Mandens Skridt, når han har Behag i hans Vej;
Ngati Yehova akondwera ndi njira ya munthu, amakhazikitsa mayendedwe ake;
24 om end han snubler, falder han ikke, thi HERREN støtter hans Hånd.
ngakhale atapunthwa sadzagwa, pakuti Yehova amamutchinjiriza ndi dzanja lake.
25 Ung har jeg været, og nu er jeg gammel, men aldrig så jeg en retfærdig forladt eller hans Afkom tigge sit Brød;
Ine ndinali wamngʼono ndipo tsopano ndakalamba koma sindinaonepo olungama akusiyidwa kapena ana awo akupempha chakudya.
26 han ynkes altid og låner ud, og hans Afkom er til Velsignelse.
Iwo ndi owolowamanja nthawi zonse ndipo amabwereketsa mwaufulu; ana awo adzadalitsika.
27 Vig fra ondt og øv godt, så bliver du boende evindelig;
Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino; pamenepo udzakhazikika mʼdziko kwamuyaya.
28 thi HERREN elsker Ret og svigter ej sine fromme. De onde udslettes for evigt, de gudløses Afkom udryddes;
Pakuti Yehova amakonda wolungama ndipo sadzasiya okhulupirika ake. Iwo adzatetezedwa kwamuyaya, koma zidzukulu za oyipa zidzachotsedwa;
29 de retfærdige arver Landet og skal bo der til evig Tid.
olungama adzalandira dziko ndipo adzakhazikikamo kwamuyaya.
30 Den retfærdiges Mund taler Visdom; hans Tunge siger, hvad ret er;
Pakamwa pa munthu wolungama pamayankhula za nzeru, ndipo lilime lake limayankhula zolungama.
31 sin Guds Lov har han i Hjertet, ikke vakler hans Skridt.
Lamulo la Mulungu wake lili mu mtima mwake; mapazi ake saterereka.
32 Den gudløse lurer på den retfærdige og står ham efter Livet,
Oyipa amabisala kudikira olungama; kufunafuna miyoyo yawoyo;
33 men, HERREN giver ham ej i hans Hånd og lader ham ikke dømmes for Retten.
koma Yehova sadzawasiya pansi pa mphamvu yawo kapena kuti atsutsidwe pamene abweretsedwa pa milandu.
34 Bi på HERREN og bliv på hans Vej, så skal han ophøje dig til at arve Landet; du skal skue de gudløses Undergang.
Khulupirira Yehova, ndipo sunga njira yake; Iye adzakukweza ndipo udzalandira dziko kuti likhale lako; udzaona anthu oyipa akuwonongeka.
35 Jeg har set en gudløs trodse, bryste sig som en Libanons Ceder
Ine ndinaona munthu woyipa ndi munthu wopanda chifundo akupeza bwino ngati mtengo wobiriwira pa nthaka ya makolo ake.
36 men se, da jeg gik der forbi, var han borte; da jeg søgte ham, fandtes han ikke.
Koma sanachedwe kumwalira ndipo sanaonekenso; ngakhale ndinamuyangʼanayangʼana, sanapezekenso.
37 Vogt på Uskyld, læg Vind på Oprigtighed, thi Fredens Mand har en Fremtid;
Ganizira za munthu wosalakwa, yangʼanitsitsa munthu wolungama; udzaona kuti ali ndi tsogolo labwino ndipo ali ndi zidzukulu zambiri.
38 men Overtræderne udryddes til Hobe, de gudløses Fremtid går tabt.
Koma anthu ochimwa adzawonongeka; iwowo pamodzi ndi zidzukulu zawo zomwe.
39 De retfærdiges Frelse kommer fra HERREN, deres Tilflugt i Nødens Stund;
Chipulumutso cha olungama chimachokera kwa Yehova; Iye ndiye linga lawo pa nthawi ya masautso.
40 HERREN hjælper og frier dem, fra de gudløse frier og frelser han dem; thi hos ham har de søgt deres Tilflugt.
Yehova amawathandiza ndi kuwalanditsa; Iye amawalanditsa kwa oyipa ndi kuwapulumutsa, pakuti amathawira kwa Iye.