< Salme 20 >
1 (Til sangmesteren. En salme af David.) På trængselens dag bønhøre Herren dig, værne dig Jakobs Guds Navn!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Yehova akuyankhe pamene uli pa msautso; dzina la Mulungu wa Yakobo likuteteze.
2 Han sende dig Hjælp fra Helligdommen, fra Zion styrke han dig;
Iye atumize thandizo kuchokera ku malo ake opatulika; akugwirizize kuchokera ku Ziyoni.
3 han komme alle dine Afgrødeofre i Hu og tage dit Brændoffer gyldigt! (Sela)
Iye akumbukire nsembe zako zonse ndipo alandire nsembe zako zopsereza. (Sela)
4 Han give dig efter dit Hjertes Attrå, han fuldbyrde alt dit Råd,
Akupatse chokhumba cha mtima wako ndipo akuthandize kuti zonse wakonza zichitike.
5 at vi må juble over din Frelse, løfte Banner i vor Guds Navn! HERREN opfylde alle dine Bønner!
Ife tidzafuwula ndi chimwemwe pamene iwe wapambana ndipo tidzanyamula mbendera zathu mʼdzina la Mulungu wathu, Yehova ayankhe zopempha zako zonse.
6 Nu ved jeg, at HERREN frelser sin Salvede og svarer ham fra sin hellige Himmel med sin højres frelsende Vælde.
Tsopano ndadziwa kuti Yehova amapulumutsa wodzozedwa wake; Iye amamuyankha kuchokera kumwamba ku malo ake opatulika ndi mphamvu yopulumutsa ya dzanja lake lamanja.
7 Nogle stoler på Heste, andre på Vogne, vi sejrer ved HERREN vor Guds Navn.
Ena amadalira magaleta ndipo ena akavalo koma ife tidzadalira dzina la Yehova Mulungu wathu.
8 De synker i Knæ og falder, vi rejser os og kommer atter på Fode.
Iwo amagonjetsedwa ndi kugwa, koma ife timadzuka ndi kuyima chilili.
9 HERRE, frels dog Kongen og svar os, den Dag vi kalder!
Inu Yehova, pulumutsani mfumu! Tiyankheni pamene tikuyitanani!