< Salme 121 >

1 (Sang til Festrejserne.) Jeg løfter mine Øjne til Bjergene: Hvorfra kommer min Hjælp?
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Fra HERREN kommer min Hjælp, fra Himlens og Jordens Skaber.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 Din fod vil han ej lade vakle, ej blunder han, som bevarer dig;
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 nej, han blunder og sover ikke, han, som bevarer Israel.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 HERREN er den, som bevarer dig, HERREN er din Skygge ved din højre;
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 Solen stikker dig ikke om Dagen, og Månen ikke om Natten;
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 HERREN bevarer dig mod alt ondt, han bevarer din Sjæl;
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 HERREN bevarer din Udgang og Indgang fra nu og til evig Tid!
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

< Salme 121 >