< Ordsprogene 28 >

1 Den gudløse flyr, skønt ingen er efter ham; tryg som en Løve er den retfærdige.
Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
2 Ved Voldsmands Brøde opstår Strid, den kvæles af Mand med Forstand.
Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
3 En fattig Tyran, der kuer de ringe, er Regn, der hærger og ej giver Brød.
Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
4 Hvo Loven sviger, roser de gudløse, hvo Loven holder, er på Krigsfod med dem.
Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
5 Ildesindede fatter ej Ret; alt fatter de, som søger HERREN.
Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
6 Hellere en fattig med lydefri Færd end en, som går Krogveje, er han end rig.
Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
7 Forstandig Søn tager Vare på Loven, men Drankeres Fælle gør sin Fader Skam.
Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
8 Hvo Velstand øger ved Åger og Opgæld, samler til en, som er mild mod de ringe.
Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
9 Den, der vender sit Øre fra Loven, endog hans Bøn er en Gru.
Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
10 Leder man retsindige vild på onde Veje, falder man selv i sin Grav; men de lydefri arver Lykke.
Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
11 Rigmand tykkes sig viis, forstandig Småmand gennemskuer ham.
Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
12 Når retfærdige jubler, er Herligheden stor, vinder gudløse frem, skal man lede efter Folk.
Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
13 At dølge sin Synd fører ikke til Held, men bekendes og slippes den, finder man Nåde.
Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
14 Saligt det Menneske, som altid ængstes, men forhærder man sit Hjerte, falder man i Ulykke.
Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
15 En brølende Løve, en grådig Bjørn er en gudløs, som styrer et ringe Folk.
Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
16 Uforstandig Fyrste øver megen Vold, langt Liv får den, der hader Rov.
Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
17 Et Menneske, der tynges af Blodskyld, er på Flugt til sin Grav; man hjælpe ham ikke.
Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
18 Den, som vandrer lydefrit, frelses, men den, som går Krogveje, falder i Graven.
Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
19 Den mættes med brød, som dyrker sin Jord, med Fattigdom den, der jager efter Tomhed.
Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
20 Ærlig Mand velsignes rigt, men Jag efter Rigdom undgår ej Straf.
Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
21 At være partisk er ikke godt, en Mand kan forse sig for en Bid Brød.
Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
22 Misundelig Mand vil i Hast vinde Gods; at Trang kommer over ham, ved han ikke.
Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
23 Den, der revser, får Tak til sidst fremfor den, hvis Tunge er slesk.
Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
24 Stjæle fra Forældre og nægte, at det, er Synd, er at være Fælle med hærgende Mand.
Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
25 Den vindesyge vækker Splid, men den, der stoler på HERREN, kvæges.
Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
26 Den, der stoler på sit Vid, er en Tåbe, men den, der vandrer i Visdom, reddes.
Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
27 Hvo Fattigmand giver, skal intet fattes, men mangefold bandes, hvo Øjnene lukker.
Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
28 Vinder gudløse frem, kryber Folk i Skjul; når de omkommer, bliver de retfærdige mange.
Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

< Ordsprogene 28 >