< Ordsprogene 27 >

1 Ros dig ikke af Dagen i Morgen, du ved jo ikke, hvad Dag kan bringe.
Usamanyadire za mawa, pakuti sudziwa zimene zidzachitike pa tsikulo.
2 Lad en anden rose dig, ikke din Mund, en fremmed, ikke dine egne Læber.
Munthu wina akutamande, koma osati wekha; mlendo akakutamanda, ndiponi koma osati ndi pakamwa pako.
3 Sten er tung, og Sand vejer til, men tung fremfor begge er Dårers Galde.
Mwala ndi wolemera ndipo mchenganso ndi wolemera kwambiri, koma makani a chitsiru ndi oposa zonsezo kulemera kwake.
4 Vrede er grum, og Harme skummer, men Skinsyge, hvo kan stå for den?
Mkwiyo umadzetsa nkhanza ndipo kupsa mtima kumachititsa zoopsa. Koma nsanje imachita zoopsa zopambana.
5 Hellere åbenlys Revselse end Kærlighed, der skjules.
Kudzudzula munthu poyera nʼkwabwino kuposa chikondi chobisika.
6 Vennehånds Hug er ærligt mente, Avindsmands Kys er mange.
Munthu amene amakukonda ngakhale akupweteke zili bwino, koma mdani wako amakupsompsona mwachinyengo.
7 Den mætte vrager Honning, alt beskt er sødt for den sultne.
Iye amene wakhuta amayipidwa ndi chisa cha uchi, koma kwa munthu wanjala ngakhale chimene chili chowawa chimamukomera.
8 Som Fugl, der må fly fra sin Rede, er Mand, der må fly fra sit Hjem:
Munthu amene wasochera ku nyumba kwake, ali monga mbalame imene yasochera pa chisa chake.
9 Olie og Røgelse fryder Sindet, men Sjælen sønderslides af Kummer.
Mafuta ndi zonunkhira zimasangalatsa mtima, ndipo kukoma mtima kwa bwenzi kwagona pa malangizo ake.
10 Slip ikke din Ven og din Faders Ven, gå ej til din Broders Hus på din Ulykkes Dag. Bedre er Nabo ved Hånden end Broder i det fjerne.
Usasiye bwenzi lako ndiponso bwenzi la abambo ako, ndipo usapite ku nyumba ya mʼbale wako pamene wakumana ndi mavuto; mnzako wokhala naye pafupi amaposa mʼbale wako wokhala kutali.
11 Vær viis, min Søn, og glæd mit Hjerte, at jeg kan svare den, der smæder mig.
Mwana wanga, khala wanzeru, ndipo ukondweretse mtima wanga; pamenepo ine ndidzatha kuyankha aliyense amene amandinyoza.
12 Den kloge ser Faren og søger i Skjul, tankeløse går videre og bøder,
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amakumana ndi mavuto.
13 Tag hans Klæder, han borged for en anden, pant ham for fremmedes Skyld!
Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole; ngati chigwiriro chifukwa waperekera chikole mlendo wosadziwika.
14 Den, som årle højlydt velsigner sin Næste, han får det regnet for Banden.
Ngati munthu apatsa mnzake moni mofuwula mmamawa kwambiri, anthu adzamuyesa kuti akutemberera.
15 Ustandseligt Tagdryp en Regnvejrsdag og trættekær Kvinde ligner hinanden;
Mkazi wolongolola ali ngati mvula yamvumbi.
16 den, som vil skjule hende, skjuler Vind, og hans højre griber i Olie.
Kumuletsa mkazi wotereyu zimenezi zili ngati kuletsa mphepo kapena kufumbata mafuta mʼdzanja.
17 Jern skærpes med Jern, det ene Menneske skærper det andet.
Chitsulo chimanoledwa ndi chitsulo chinzake, chomwechonso munthu amanoledwa ndi munthu mnzake.
18 Røgter man et Figentræ, spiser man dets Frugt; den, der vogter sin Herre, æres.
Amene amasamalira mtengo wamkuyu adzadya zipatso zake, ndipo iye amene amasamalira mbuye wake adzalandira ulemu.
19 Som i Vandspejlet Ansigt møder Ansigt, slår Menneskehjerte Menneske i Møde.
Monga momwe nkhope imaonekera mʼmadzi, chomwechonso mtima wa munthu umadziwika ndi ntchito zake.
20 Dødsrige og Afgrund kan ikke mættes, ej heller kan Menneskens Øjne mættes. (Sheol h7585)
Manda sakhuta, nawonso maso a munthu sakhuta. (Sheol h7585)
21 Digel til Sølv og Ovn til Guld, efter sit Ry bedømmes en Mand.
Siliva amasungunulira mu uvuni ndipo golide mʼngʼanjo, chomwechonso munthu amadziwika ndi zomwe akudzitamandira nazo.
22 Om du knuste en Dåre i Morter med Støder midt imellem Gryn, hans Dårskab veg dog ej fra ham.
Ngakhale utakonola chitsiru mu mtondo ndi musi ngati chimanga, uchitsiru wakewo sudzachoka.
23 Mærk dig, hvorledes dit Småkvæg ser ud, hav Omhu for dine Hjorde;
Uzidziwe bwino nkhosa zako momwe zilili. Kodi usamalire bwino ziweto zako?
24 thi Velstand varer ej evigt, Rigdom ikke fra Slægt til Slægt;
Paja chuma sichikhala mpaka muyaya, ndipo ufumu sukhala mpaka mibado yonse.
25 er Sommergræsset svundet, Grønt spiret frem, og sankes Bjergenes Urter,
Pamene udzu watha, msipu nʼkumera; ndipo atatuta udzu wa ku mapiri,
26 da har du Lam til at give dig Klæder og Bukke til at købe en Mark,
ana ankhosa adzakupatsani chovala ndipo pogulitsa mbuzi mudzapeza ndalama yogulira munda.
27 Gedemælk til Mad for dig og dit Hus, til Livets Ophold for dine Piger.
Mudzakhala ndi mkaka wambuzi wambiri kuti muzidya inuyo ndi banja lanu ndi kudyetsa antchito anu aakazi.

< Ordsprogene 27 >