< Ordsprogene 13 >

1 Viis Søn elsker tugt, spotter hører ikke på skænd.
Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake, koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.
2 Af sin Munds Frugt nyder en Mand kun godt, til Vold står troløses Hu.
Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake, koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.
3 Vogter man Munden, bevarer man Sjælen, den åbenmundede falder i Våde.
Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake, koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.
4 Den lade attrår uden at få, men flittiges Sjæl bliver mæt.
Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu, koma munthu wakhama adzalemera.
5 Den retfærdige hader Løgnetale, den gudløse spreder Skam og Skændsel.
Munthu wolungama amadana ndi zabodza, koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.
6 Retfærd skærmer, hvo lydefrit vandrer, Synden fælder de gudløse.
Chilungamo chimateteza munthu wangwiro, koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.
7 Mangen lader rig og ejer dog intet, mangen lader fattig og ejer dog meget.
Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse; munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.
8 Mands Rigdom er Løsepenge for hans Liv, Fattigmand får ingen Trusel at høre.
Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake, koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.
9 Retfærdiges Lys bryder frem, gudløses Lampe går ud.
Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa, koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.
10 Ved Hovmod vækkes kun Splid, hos dem, der lader sig råde, er Visdom.
Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano, koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.
11 Rigdom, vundet i Hast, smuldrer hen, hvad der samles Håndfuld for Håndfuld, øges.
Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.
12 At bie længe gør Hjertet sygt, opfyldt Ønske er et Livets Træ.
Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima, koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.
13 Den, der lader hånt om Ordet, slås ned, den, der frygter Budet, får Løn.
Amene amanyoza malangizo adzawonongeka, koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.
14 Vismands Lære er en Livsens Kilde, derved undgås Dødens Snarer.
Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo; amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.
15 God Forstand vinder Yndest, troløses Vej er deres Undergang.
Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu, koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.
16 Hver, som er klog, går til Værks med Kundskab, Tåben udfolder Dårskab.
Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru, koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.
17 Gudløs Budbringer går det galt, troværdigt Bud bringer Lægedom.
Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto, koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.
18 Afvises Tugt, får man Armod og Skam; agtes på Revselse, bliver man æret.
Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa, koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.
19 Opfyldt Ønske er sødt for Sjælen, at vige fra ondt er Tåber en Gru.
Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima, koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.
20 Omgås Vismænd, så bliver du viis, ilde faren er Tåbers Ven.
Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru; koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.
21 Vanheld følger Syndere, Lykken når de retfærdige.
Choyipa chitsata mwini, koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.
22 Den gode efterlader Børnebrn Arv, til retfærdige gemmes Synderens Gods.
Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa, koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.
23 På Fattigfolks Nyjord er rigelig Føde, mens mangen rives bort ved Uret.
Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri, koma anthu opanda chilungamo amachilanda.
24 Hvo Riset sparer, hader sin Søn, den, der elsker ham, tugter i Tide.
Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda, koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.
25 Den retfærdige spiser, til Sulten er stillet, gudløses Bug er tom.
Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta, koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

< Ordsprogene 13 >