< 4 Mosebog 6 >

1 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Tal til Israeliterne og sig til dem: Når en Mand eller Kvinde vil aflægge et Nasiræerløfte for således at indvie sig til HERREN,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mwamuna kapena mkazi afuna kuchita lonjezo lapadera, lonjezo lodzipatula yekha kwa Yehova ngati Mnaziri,
3 skal han afholde sig fra Vin og stærk Drik; Vineddike og stærk Drik må han ikke drikke, ej heller nogen som helst drik af Druer; han må hverken spise friske eller tørrede Druer;
sayenera kumwa vinyo kapena zakumwa zosasa ndipo asamamwe chakumwa chilichonse cha mphesa. Asamamwe madzi a mphesa kapena kudya mphesa zaziwisi kapena zowuma.
4 så længe hans Indvielse varer, må han intet som helst nyde, der kommer af Vinstokken, hverken umodne Druer eller friske Skud.
Pa nthawi yonse imene ali Mnaziri, asamadye chilichonse chopangidwa kuchokera ku mphesa ngakhale mbewu zake kapena makungu ake.’
5 Så længe hans Indvielsesløfte gælder, må ingen Ragekniv komme på hans Hoved; indtil Udløbet af den Tid han indvier sig til HERREN, skal han være hellig og lade sit Hovedhår vokse frit.
“‘Pa nthawi yonse ya lonjezo lodzipatula yekhalo, asamete kumutu kwake ndi lumo. Akhale wopatulika mpaka nthawi yake yonse ya kudzipatula yekha kwa Yehova itatha. Alileke tsitsi la pamutu pake kuti likule.’
6 Hele den Tid han har indviet sig til HERREN, må han ikke komme Lig nær;
Pa nthawi yonse imene munthuyo wadzipatula yekha kwa Yehova asayandikire mtembo.
7 selv når hans Fader eller Moder, hans Broder eller Søster dør, må han ikke pådrage sig Urenhed ved dem, thi han bærer sin Guds indvielse på sit Hoved.
Ngakhale abambo ake kapena amayi ake kapena mchimwene wake kaya mchemwali wake atamwalira, asadzidetse pokhudza mitembo yawo chifukwa kulumbira kwake kwa kudzipatula yekha kwa Yehova kuli pamutu pake.
8 Så længe hans Indvielse varer, er han helliget HERREN.
Munthuyo ndi wopatulika masiku onse odzipereka kwake kwa Yehova.
9 Men når nogen uventet og pludselig dør i hans Nærhed, og han således bringer Urenhed over sit indviede Hoved, skal han rage sit Hoved, den Dag han atter bliver ren; den syvende Dag skal han rage det;
“Ngati munthu wina afa mwadzidzidzi pafupi naye ndi kudetsa tsitsi lake loperekedwalo, amete mutu wake pa tsiku lodziyeretsa, tsiku lachisanu ndi chiwiri.
10 og den ottende Dag skal han bringe to Turtelduer eller Dueunger til Præsten ved Åbenbaringsteltets Indgang.
Tsono pa tsiku lachisanu ndi chitatu abweretse nkhunda ziwiri kapena mawunda awiri anjiwa kwa wansembe pa khomo lolowera ku tenti ya msonkhano.
11 Og Præsten skal ofre den ene som Syndoffer og den anden som Brændoffer og skaffe ham Soning, fordi han har syndet ved at røre ved Lig. Derpå skal han samme Dag atter hellige sit Hoved
Wansembe apereke imodzi kuti ikhale nsembe yauchimo ndi ina nsembe yopsereza yotetezera tchimo chifukwa anachimwa popezeka pafupi ndi mtembo. Ndipo tsiku lomwelo apatulenso tsitsi la pamutu pake.
12 og atter indvie sig til HERREN for lige så lang Tid, som han før havde indviet sig, og bringe et årgammelt Lam som Skyldoffer; den forløbne Tid regnes ikke med, da han har bragt Urenhed over sit indviede Hoved.
Adzipereke kwa Yehova pa nthawi yodzipatula ndipo abweretse nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi ngati nsembe yopepesera. Masiku akale sawerengedwanso chifukwa anadzidetsa pa nthawi yodzipatulira kwake.
13 Dette er Loven om Nasiræeren: Når hans indvielsestid er til Ende, skal han begive sig til Åbenbaringsteltets Indgang
“Tsono ili ndi lamulo la Mnaziri pamene nthawi yodzipatula kwake yatha: Abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
14 og som Offergave bringe HERREN et årgammelt, lydefrit Væderlam til Brændoffer, et årgammelt, lydefrit Hunlam til Syndoffer og en lydefri Væder til Takoffer,
Pamenepo apereke chopereka chake kwa Yehova: Nkhosa yayimuna ya chaka chimodzi yopanda chilema kuti ikhale nsembe yopsereza, mwana wankhosa wamkazi mmodzi wopanda chilema kuti ikhale nsembe yauchimo, ndi nkhosa imodzi yayikulu yayimuna kuti ikhale nsembe yachiyanjano,
15 en Kurv med usyret Bagværk, Kager af fint Hvedemel, rørte i Olie, og usyrede Fladbrød, smurte med Olie, desuden det tilhørende Afgrødeoffer og de tilhørende Drikofre.
ndipo abwere pamodzi ndi nsembe yachakudya ndi nsembe yachakumwa ndi dengu la buledi wopanda yisiti, makeke opangidwa ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ndi timitanda ta buledi topakidwa mafuta.
16 Så skal Præsten bringe det for HERRENs Åsyn og ofre hans Syndoffer og Brændoffer,
“Wansembe apereke zimenezi pamaso pa Yehova ndi kuchita nsembe ya uchimo ndi nsembe yopsereza.
17 og Væderen skal han ofre som Takoffer til HERREN tillige med de usyrede Brød i Kurven; derpå skal Præsten ofre hans Afgrødeoffer og Drikofer.
Apereke dengu la buledi wopanda yisiti ndiponso nsembe yachiyanjano kwa Yehova ya nkhosa yayimuna, pamodzi ndi chopereka cha chakudya ndi chopereka cha chakumwa.
18 Så skal Nasiræeren ved Indgangen til Åbenbaringsteltet rage sit indviede Hoved og tage sit indviede Hovedhår og kaste det i Ilden under Takofferet.
“Mnaziriyo amete tsitsi limene analipereka lija pa khomo la tenti ya msonkhano. Atenge tsitsilo ndi kuliyika pa moto umene uli pansi pa nsembe yachiyanjano.
19 Og Præsten skal tage den kogte Bov af Væderen og een usyret Kage og eet usyret Fladbrød af Kurven og lægge dem på Nasiræerens Hænder, efter at han har afraget sit indviede Hovedhår.
“Mnaziriyo atatha kumeta tsitsi analiperekalo, wansembe ayike mʼmanja mwake mwendo wa mmwamba wankhosa yayimuna umene waphikidwa ndipo atengenso keke ndi kamtanda ka buledi, zonse zopanda yisiti zomwe zili mʼdengu lija.
20 Og Præsten skal udføre Svingningen dermed for HERRENs Åsyn; det tilfalder Præsten som Helliggave foruden Svingningsbrystet og Offerydelseskøllen. Derefter må Nasiræeren atter drikke Vin.
Wansembe aziweyule pamaso pa Yehova ngati nsembe yoweyula. Zimenezi ndi zopatulika ndipo ndi za wansembe pamodzi ndi chidale chimene anachiweyula ndi ntchafu yomwe anayipereka ija. Zitatha izi, Mnaziri akhoza kumwa vinyo.
21 Det er Loven om Nasiræeren, der aflægger Løfte, om hans Offergave til HERREN i Anledning af Indvielsen, foruden hvad han ellers evner at give; overensstemmende med Løftet, han aflægger, skal han forholde sig efter den for hans Indvielse gældende Lov.
“Ili ndi lamulo la Mnaziri yemwe walonjeza kudzipereka kwa Yehova podzipatula yekha kuphatikiza pa zomwe angathe kukwaniritsa. Ayenera kukwaniritsa lonjezo lomwe wachitalo potsata lamulo la Mnaziri.”
22 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anawuza Mose kuti,
23 Tal til Aron og hans Sønner og sig: Når I velsigner Israeliterne, skal I sige til dem:
“Uza Aaroni ndi ana ake aamuna kuti, ‘Umu ndi mmene muzidalitsira Aisraeli. Muzinena kuti,
24 HERREN velsigne dig og bevare dig,
“‘Yehova akudalitse ndi kukusunga;
25 HERREN lade sit Ansigt lyse over dig og være dig nådig,
Yehova awalitse nkhope yake pa iwe, nakuchitira chisomo;
26 HERREN løfte sit Åsyn på dig og give dig Fred!
Yehova akweze nkhope yake pa iwe, nakupatse mtendere.’”
27 Således skal de lægge mit Navn på Israeliterne, og jeg vil velsigne dem.
Choncho akadzatchula dzina langa podalitsa Aisraeli, Ine ndidzawadalitsadi.

< 4 Mosebog 6 >