< 4 Mosebog 3 >
1 Følgende var Arons og Moses's Efterkommere, på den Tid HERREN talede på Sinaj Bjerg.
Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.
2 Navnene på Arons Sønner var følgende: Nadab, den førstefødte, Abihu, Eleazar og Itamar;
Mayina a ana aamuna a Aaroni anali Nadabu, woyamba kubadwa, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
3 det var Navnene på Arons Sønner, de salvede Præster, som indsattes til Præstetjeneste.
Amenewa ndi mayina a ana aamuna a Aaroni, ansembe odzozedwa omwe anapatulidwa kuti azitumikira ngati ansembe.
4 Men Nadab og Abihu døde for HERRENs Åsyn, da de frembar fremmed Ild for HERRENs Åsyn i Sinaj Ørken, og de havde ingen Sønner. Således kom Eleazar og Itamar til at gøre Præstetjenest: for deres Fader Arons Åsyn.
Koma Nadabu ndi Abihu, anagwa nafa pamaso pa Yehova pamene ankapereka nsembe ndi moto wachilendo pamaso pa Yehova mʼchipululu cha Sinai. Iwowo analibe ana aamuna. Choncho Eliezara ndi Itamara ndiwo amene ankatumikira ngati ansembe nthawi imene Aaroni abambo awo anali moyo.
5 HERREN talede til Moses og sagde:
Yehova anati kwa Mose,
6 Lad Levis Stamme træde frem og stil dem frem for Præsten Aron, for at de kan gå ham til Hånde.
“Bweretsa fuko la Levi ndipo ulipereke kwa Aaroni wansembe kuti lizimutumikira.
7 De skal tage Vare på, hvad han og hele Menigheden har at varetage foran Åbenbaringsteltet, og således udføre Arbejdet ved Boligen,
Azigwira ntchito yothandiza iyeyo ndi gulu lonse ku tenti ya msonkhano pogwira ntchito ya ku Chihema.
8 og de skal tage Vare på alle Åbenbaringsteltets Redskaber og på, hvad Israeliterne har at varetage, og således udføre Arbejdet ved Boligen.
Azisamalira zipangizo zonse za mu tenti ya msonkhano, ndipo azigwirira ntchito Aisraeli potumikira mu tenti.
9 Altså skal du overgive Aron og hans Sønner Leviterne; de er ham overgivet som Gave fra Israeliterne.
Pereka Alevi kwa Aaroni ndi kwa ana ake aamuna. Amenewa ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwa iye kwathunthu.
10 Men Aron og hans Sønner skal du sætte til at tage Vare på deres Præstetjeneste; enhver Lægmand, som trænger sig ind deri, skal lide Døden.
Usankhe Aaroni ndi ana ake aamuna kuti azitumikira pa ntchito ya unsembe. Koma wina aliyense woyandikira malo opatulika aphedwe.”
11 HERREN talede til Moses og sagde:
Yehova anawuzanso Mose kuti,
12 Se, jeg har selv udtaget Leviterne af Israelitternes Midte i Stedet for alt det førstefødte, der åbner Moders Liv hos Israeliterne, og Leviterne er blevet min Ejendom;
“Pakati pa Aisraeli onse ndatenga Alevi kulowa mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa kwa amayi a Chiisraeli. Alevi ndi anga,
13 thi mig tilhører alt det førstefødte. Dengang jeg dræbte alt det førstefødte i Ægypten, helligede jeg mig alt det førstefødte i Israel, både af Mennesker og Dyr; mig HERREN skal de tilhøre.
pakuti ana onse oyamba kubadwa ndi anga. Nditakantha ana onse oyamba kubadwa mu Igupto, ndinadzipatulira ndekha mwana aliyense woyamba kubadwa mu Israeli, wa munthu ndi nyama. Azikhala anga. Ine ndine Yehova.”
14 HERREN talede til Moses i Sinaj Ørken og sagde:
Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti,
15 Du skal mønstre Levis Sønner efter deres Fædrenehuse, efter deres Slægter; alle af Mandkøn fra en Måned og opefter skal du mønstre.
“Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.”
16 Da mønstrede Moses dem på HERRENs Bud, som der var ham pålagt.
Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.
17 Følgende var Levis Sønner efter deres Navne: Gerson, Kehat og Merari.
Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
18 Følgende var Navnene på Gersons Sønner efter deres Slægter: Libni og Sjimi;
Mayina a ana a Geresoni potsata mabanja awo ndi awa: Libini ndi Simei.
19 Hehats Sønner efter deres Slægter var: Amram, Jizhar, Hebron og Uzziel;
Ana a Kohati potsata mabanja awo ndi awa: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli.
20 Meraris Sønner efter deres Slægter var: Mali og Musji. Det var Leviternes Slægter efter deres Fædrenehuse.
Ana a Merari potsata mabanja awo ndi awa: Mali ndi Musi. Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi monga mwa makolo awo.
21 Fra Gerson nedstammede Libniternes og Sjimiternes Slægter; det var Gersoniternes Slægter.
Kwa Geresoni kunali banja la Alibini, banja la Asimei. Amenewa ndiwo anali mabanja a Ageresoni.
22 De, som mønstredes af dem, da alle af Mandkøn fra en Måned og opefter blev optalt, de, som mønstredes af dem, udgjorde 7500.
Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500.
23 Gersoniternes Slægter havde deres Lejrplads bag ved Boligen mod Vest.
Mabanja a Ageresoni azimanga misasa yawo kumadzulo, kumbuyo kwa Chihema.
24 Øverste for Gersoniternes Fædrenehus var Eljasar, Laels Søn.
Mtsogoleri wa mabanja a Ageresoni anali Eliyasafu mwana wa Laeli.
25 Gersoniterne havde ved Åbenbaringsteltet at tage Vare på selve Boligen og Teltdækket, dets Dække, Forhænget for Åbenbaringsteltets Indgang,
Ntchito imene Ageresoni anapatsidwa ku tenti ya msonkhano inali yosamalira Chihema ndi tenti, pamodzi ndi zophimbira zake, katani ya pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
26 Forgårdens Omhæng, Forhænget for Indgangen til Forgården, der omgav Boligen og Alteret, og dens Teltreb, alt Arbejdet dermed.
ndi makatani wotchinga bwalo, katani ya pa chipata cholowera ku bwalo lozungulira Chihema ndi guwa lansembe, zingwe ndi zonse zokhudzana ndi ntchito yawo.
27 Fra Kehat nedstammede Amramiternes, Jizhariternes, Hebroniternes og Uzzieliternes Slægter; det var Kehatiternes Slægter.
Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati.
28 De, der mønstredes af dem, da alle af Mandkøn fra en Måned og opefter blev optalt, udgjorde 8600, som tog Vare på, hvad der var at varetage ved Helligdommen.
Chiwerengero cha amuna onse a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 8,600. Akohati ankagwira ntchito yosamalira malo wopatulika.
29 Kehatiternes Slægter havde deres Lejrplads ved Boligens Sydside.
Mabanja a ana a Kohati ankamanga misasa yawo kummwera kwa Chihema.
30 Øverste for Kehatiternes Slægters Fædrenehus var Elizafan, Uzziels Søn.
Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Kohati anali Elizafani mwana wa Uzieli.
31 De havde at tage Vare på Arken, Bordet, Lysestagen, Altrene, Helligdommens Redskaber, som brugtes ved Tjenesten, og Forhænget med dertil hørende Arbejde.
Iwo ankagwira ntchito yosamalira Bokosi la Chipangano, tebulo, choyikapo nyale, maguwa, zipangizo za kumalo wopatulika zimene ansembe ankagwiritsa ntchito, katani, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito.
32 Øverste over Leviternes Øverster var Eleazar, Præsten Arons Søn, som havde Tilsyn med dem, der tog Vare på, hvad der var at varetage ved Helligdommen.
Mtsogoleri wamkulu wa Alevi anali Eliezara mwana wa Aaroni wansembe. Iye anasankhidwa kukhala woyangʼanira omwe ankasamalira malo wopatulika.
33 Fra Merari nedstammede Maliternes og Musjiternes Slægter; det var Meraris Slægter.
Kwa Merari kunali banja la Mali ndi banja la Musi. Amenewa ndiye anali mabanja a Amerari.
34 De, som mønstredes af dem, da alle af Mandkøn fra en Måned og opefter blev optalt, udgjorde 6200.
Chiwerengero cha amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 6,200.
35 Øverste for Meraris Slægters Fædrenehus var Zuriel, Abibajils Søn. De havde deres Lejrplads ved Boligens Nordside.
Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Amerari anali Zuriyeli mwana wa Abihaili. Iwo ankamanga misasa yawo kumpoto kwa Chihema.
36 Merariterne var sat til at tage Vare på Boligens Brædder, Tværstænger, Piller og Fodstykker, alle dens Redskaber og alt det dertil hørende Arbejde,
Amerari anapatsidwa ntchito yosamalira mitengo ya chihema, nsichi zake, mizati yake, matsinde ake, ndi zida zake zonse, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito,
37 Pillerne til Forgården, som var rundt om den, med Fodstykker, Pæle og Reb.
pamodzi ndi mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema ndi zingwe zake.
38 Foran Boligen, på Åbenbaringsteltets Forside mod Øst, havde Moses, Aron og hans Sønner deres Lejrpladser, og de tog Vare på alt det, Israeliterne havde at varetage ved Boligen. Enhver Lægmand, der trængte sig ind i det, måtte lide Døden.
Mose ndi Aaroni ndi ana ake aamuna ankamanga misasa yawo kummawa kwa chihema, kuyangʼana kotulukira dzuwa, kutsogolo kwa tenti ya msonkhano. Anali ndi ntchito yosamalira malo wopatulika mʼmalo mwa Aisraeli. Aliyense woyandikira malo wopatulika ankayenera kuphedwa.
39 De mønstrede af Leviterne, de, som Moses og Aron mønstrede på HERRENs Bud efter deres Slægter, alle af Mandkøn fra en Måned og opefter, udgjorde i alt 22 000.
Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.
40 HERREN sagde til Moses: Du skal mønstre alle førstefødte af Mandkøn blandt Israeliterne fra en Måned og opefter og optage Tallet på deres Navne.
Yehova anawuza Mose kuti, “Werenga ana onse aamuna oyamba kubadwa mu Israeli, omwe ali ndi mwezi umodzi kapena kupitirirapo ndipo ulembe mndandanda wa mayina awo.
41 Så skal du udtage Leviterne til mig HERREN i Stedet for alle Israelitternes førstefødte og ligeledes Leviternes Kvæg i Stedet for alt det førstefødte af Israelitternes Kvæg.
Unditengere Alevi onse mʼmalo mwa ana oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso ziweto zazimuna za Alevi mʼmalo mwa ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa za Aisraeli. Ine ndine Yehova.”
42 Og Moses mønstrede, som HERREN havde pålagt ham, alle Israelitternes førstefødte;
Choncho Mose anawerenga ana aamuna onse oyamba kubadwa a Aisraeli monga momwe Yehova anamulamulira.
43 og da Navnene på dem fra en Måned og opefter optaltes, udgjorde de førstefødte af Mandkøn, alle de, som mønstredes i alt 22 273.
Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273.
44 Derpå talede HERREN til Moses og sagde:
Ndipo Yehova anawuzanso Mose kuti,
45 Tag Leviterne i Stedet for alle Israelitternes førstefødte og ligeledes Leviternes Kvæg i Stedet for deres Kvæg, så at Leviterne kommer til at tilhøre mig HERREN.
“Tenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso zoweta zonse za Alevi mʼmalo mwa zoweta za Aisraeli. Alevi ndi anga. Ine ndine Yehova.
46 Men til Udløsning af de 273, hvormed Antallet af Israelitternes førstefødte overstiger Leviternes Antal,
Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi,
47 skal du tage fem Sekel for hvert Hoved, efter hellig Vægt skal du tage dem, tyve Gera på en Sekel;
utenge masekeli asanu pa munthu aliyense. Masekeliwo akhale ofanana ndi masekeli a ku malo wopatulika, kumene sekeli imodzi imakwanira magera makumi awiri.
48 og Pengene skal du give Aron og hans Sønner som Udløsning for de overskydende.
Ndalama zimenezi uzipereke kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kuti ukhale mtengo woombolera Aisraeli woonjezerawo.”
49 Da tog Moses Løsepengene af de overskydende, dem, der ikke var udløst ved Leviterne;
Choncho Mose anatenga ndalama zowombolera zija kuchokera kwa Aisraeli amene chiwerengero chawo chinaposa chiwerengero cha omwe anawomboledwa ndi Alevi.
50 af Israelitternes førstefødte tog han Pengene, 1365 Sekel efter hellig Vægt.
Anatenga masekeli a siliva okwana 1,365 molingana ndi masekeli a ku malo opatulika, kuchokera kwa ana aamuna oyamba kubadwa a Aisraeli.
51 Og Moses gav Aron og hans Sønner Løsepengene efter HERRENs Bud, som HERREN havde pålagt Moses.
Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.