< Matthæus 9 >

1 Og han gik om Bord i et Skib og for over og kom til sin egen By.
Yesu analowa mʼbwato nawoloka, ndipo anabwera ku mudzi wa kwawo.
2 Og se, de bare til ham en værkbruden, som lå på en Seng; og da Jesus så deres Tro, sagde han til den værkbrudne: "Søn! vær frimodig, dine Synder forlades dig."
Amuna ena anabwera ndi munthu wakufa ziwalo kwa Iye atamugoneka pa mphasa. Yesu ataona chikhulupiriro chawo anati kwa wakufa ziwaloyo, “Limba mtima mwana wanga, machimo ako akhululukidwa.”
3 Og se, nogle af de skriftkloge sagde ved sig selv: "Denne taler bespotteligt."
Pamenepo aphunzitsi ena amalamulo anaganiza mu mtima mwawo kuti, “Munthu uyu akuchitira Mulungu mwano.”
4 Og da Jesus så deres Tanker, sagde han: "Hvorfor tænke I ondt i eders Hjerter?
Ndipo podziwa maganizo awo Yesu anati, “Bwanji mukuganiza zoyipa mʼmitima mwanu?
5 Thi hvilket er lettest at sige: Dine Synder forlades dig, eller at sige: Stå op og gå?
Chapafupi ndi chiti kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa’ kapena kunena kuti, ‘Imirira ndipo yenda?’
6 Men for at I skulle vide, at Menneskesønnen har Magt på Jorden til at forlade Synder," da siger han til den værkbrudne: "Stå op, og tag din Seng, og gå til dit Hus!"
Tsono kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko wokhululuka machimo, pamenepo anati kwa wakufa ziwaloyo, ‘Imirira, tenga mphasa yako kazipita kwanu.’”
7 Og han stod op og gik bort til sit Hus.
Ndipo munthuyo anayimirira napita kwawo.
8 Men da Skarerne så det, frygtede de og priste Gud, som havde givet Menneskene en sådan Magt.
Gulu la anthu litaona izi, linadzazidwa ndi mantha ndipo linalemekeza Mulungu amene anapereka ulamuliro kwa anthu.
9 Og da Jesus gik videre derfra, så han en Mand, som hed Matthæus, sidde ved Toldboden; og han siger til ham: "Følg mig!" Og han stod op og fulgte ham.
Ndipo Yesu atachoka kumeneko, anaona munthu wina dzina lake Mateyu, atakhala mʼnyumba ya msonkho. Anati kwa iye, “Nditsate Ine.” Ndipo iye ananyamuka namutsata.
10 Og det skete, da han sad til Bords i Huset, se, da kom der mange Toldere og Syndere og sade til Bords med Jesus og hans Disciple.
Ndipo pamene Iye ankadya mʼnyumba, onani, amisonkho ndi ochimwa ambiri anabwera nakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ake.
11 Og da Farisæerne så det, sagde de til hans Disciple: "Hvorfor spiser eders Mester med Toldere og Syndere?"
Ndipo Afarisi poona izi, anati kwa ophunzira ake, “Nʼchifukwa chiyani Aphunzitsi anu akudya pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
12 Men da Jesus hørte det, sagde han: "De raske trænge ikke til Læge, men de syge.
Yesu atamva, anati, “Munthu wamoyo safuna singʼanga ayi, koma wodwala.
13 Men går hen og lærer, hvad det vil sige: Jeg har Lyst til Barmhjertighed og ikke til Offer; thi jeg er ikke kommen for at kalde retfærdige, men Syndere,"
Koma pitani kaphunzireni tanthauzo la mawu awa: ‘Ndimafuna chifundo osati nsembe ayi.’ Pakuti sindinabwere kudzayitana olungama koma ochimwa.”
14 Da komme Johannes's Disciple til ham og sige: "Hvorfor faste vi og Farisæerne meget, men dine Disciple faste ikke?"
Ndipo ophunzira a Yohane anabwera namufunsa Iye kuti, “Bwanji ife ndi Afarisi timasala kudya koma ophunzira anu sasala kudya?”
15 Og Jesus sagde til dem: "Kunne Brudesvendene sørge, så længe Brudgommen er hos dem? Men der skal komme Dage, da Brudgommen bliver tagen fra dem, og da skulle de faste.
Yesu anayankha kuti, “Kodi oyitanidwa ku ukwati angamalire bwanji pamene mkwati ali naye pamodzi? Nthawi idzafika pamene mkwatiyo adzachotsedwa ndi pamene adzasala kudya.”
16 Men ingen sætter en Lap af uvalket Klæde på et gammelt Klædebon; thi Lappen river Klædebonnet itu, og der bliver et værre Hul.
Ndipo palibe munthu amasokerera chigamba chatsopano pa chovala chakale chifukwa chigambacho chidzachoka ndipo chibowocho chidzakula kuposa kale.
17 Man kommer heller ikke ung Vin på gamle Læderflasker, ellers sprænges Læderflaskerne, og Vinen spildes, og Læderflaskerne ødelægges; men man kommer ung Vin på nye Læderflasker, så blive begge Dele bevarede."
Kapena sathira vinyo watsopano mʼmatumba akale; akatero, matumba akalewo adzaphulika ndipo vinyoyo adzatayika, matumbawo adzawonongeka; satero ayi. Amathira vinyo watsopano mʼmatumba atsopanonso ndipo zonse zimasungika.
18 Medens han talte dette til dem, se, da kom der en Forstander og faldt ned for ham og sagde: "Min Datter er lige nu død; men kom og læg din Hånd på hende, så bliver hun levende."
Pamene ankanena zimenezi, mkulu wa sunagoge anabwera namugwadira Iye nati, “Mwana wanga wamkazi wamwalira posachedwapa koma tiyeni mukasanjike dzanja lanu pa iye ndipo adzakhala ndi moyo.”
19 Og Jesus stod op og fulgte ham med sine Disciple.
Yesu ndi ophunzira ake ananyamuka napita naye pamodzi.
20 Og se, en Kvinde, som havde haft Blodflod i tolv År, trådte hen bagfra og rørte ved Fligen af hans Klædebon;
Panali mayi wina amene ankadwala nthenda yotaya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri ndipo anadza mʼmbuyo mwake nakhudza mkanjo wake.
21 thi hun sagde ved sig selv: "Dersom jeg blot rører ved hans Klædebon, bliver jeg frelst."
Iyeyo anati mwa iye yekha, “Nditangokhudza kasonga ka mkanjo wake, ine ndidzachiritsidwa.”
22 Men Jesus vendte sig om, og da han så hende, sagde han: "Datter! vær frimodig, din Tro har frelst dig." Og Kvinden blev frelst fra den samme Time.
Ndipo Yesu anatembenuka namuona mayiyo nati, “Limbani mtima mayi iwe, chikhulupiriro chako chakuchiritsa.” Nthawi yomweyo mayiyo anachiritsidwa.
23 Og da Jesus kom til Forstanderens Hus og så Fløjtespillerne og Hoben, som larmede, sagde han:
Yesu atalowa mʼnyumba ya mkulu wa sunagoge ndi kuona oyimba zitoliro ndi gulu la anthu ochita phokoso,
24 "Gå bort, thi Pigen er ikke død, men hun sover." Og de lo ad ham.
anati, “Tulukani, mtsikanayu sanafe koma ali mtulo.” Koma anamuseka Iye.
25 Men da Hoben var dreven ud, gik han ind og tog hende ved Hånden; og Pigen stod op.
Atangowatulutsa anthuwo, analowa mʼnyumba ndipo anagwira dzanja la mtsikanayo ndipo anauka.
26 Og Rygtet herom kom ud i hele den Egn.
Mbiriyi inamveka mʼdera lonse.
27 Og da Jesus gik bort derfra, fulgte der ham to blinde, som råbte og sagde: "Forbarm dig over os, du Davids Søn!"
Yesu atapitirira ulendo wake, amuna awiri osaona anamutsatira Iye, akufuwula kuti, “Tichitireni chifundo, Mwana wa Davide!”
28 Men da han kom ind i Huset, gik de blinde til ham; og Jesus siger til dem: "Tro I, at jeg kan gøre dette?"De siger til ham:"Ja, Herre!"
Atalowa mʼnyumba, amuna awiri osaonawo anabwera kwa Iye ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukhulupirira kuti ndikhoza kukuchiritsani?” Iwo anayankha kuti, “Inde Ambuye.”
29 Da rørte han ved deres Øjne og sagde: "Det ske eder efter eders Tro!"
Pomwepo anakhudza maso awo nati, “Zichitike kwa inu monga mwachikhulupiriro chanu.”
30 Og deres Øjne bleve åbnede. Og Jesus bød dem strengt og sagde: "Ser til, lad ingen få det at vide."
Ndipo anayamba kuona. Yesu anawachenjeza kwambiri nati, “Onani, wina aliyense asadziwe za zimenezi.”
31 Men de gik ud og udbredte Rygtet om ham i hele den Egn.
Koma iwo anatuluka mʼnyumbamo nafalitsa za Iye mʼchigawo chonse.
32 Men da disse gik ud, se, da førte de til ham et stumt Menneske, som var besat.
Pamene iwo ankatuluka kunja, anthu anabwera kwa Iye ndi munthu wogwidwa ndi mzimu wosayankhula.
33 Og da den onde Ånd var uddreven, talte den stumme. Og Skarerne forundrede sig og sagde: "Aldrig er sådant set i Israel."
Ndipo atatulutsa mzimuwo, munthuyo anayankhula. Gulu la anthuwo linadabwa ndipo linati, “Zinthu zotere sizinaonekepo mu Israeli.”
34 Men Farisæerne sagde: "Ved de onde Ånders Fyrste uddriver han de onde Ånder."
Koma Afarisi anati, “Akutulutsa mizimu yoyipa ndi mphamvu ya mkulu wa ziwanda.”
35 Og Jesus gik omkring i alle Byerne og Landsbyerne, lærte i deres Synagoger og prædikede Rigets Evangelium og helbredte enhver Sygdom og enhver Skrøbelighed.
Yesu anayendayenda mʼmizinda yonse ndi mʼmidzi, kuphunzitsa mʼmasunagoge awo, nalalikira Uthenga Wabwino wa ufumu ndi kuchiritsa nthenda zawo zonse ndi zofowoka za mʼmatupi mwawo.
36 Men da han så Skarerne, ynkedes han inderligt over dem; thi de vare vanrøgtede og forkomne som Får, der ikke have Hyrde.
Ataona maguluwo, anagwidwa ndi chisoni chifukwa anali ozunzika ndi osowa chithandizo ngati nkhosa zopanda mʼbusa.
37 Da siger han til sine Disciple: "Høsten er stor, men Arbejderne ere få;
Pamenepo anati kwa ophunzira ake, “Zokolola ndi zambiri koma antchito ndi ochepa.
38 beder derfor Høstens Herre om, at han vil sende Arbejdere ud til sin Høst."
Nʼchifukwa chake, pemphani Ambuye mwini zokolola kuti atumize antchito ku munda wake.”

< Matthæus 9 >