< 3 Mosebog 8 >
1 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 "Tag Aron og hans Sønner sammen med ham, Klæderne, Salveolien, Syndoffertyren, de to Vædre og Kurven med de usyrede Brød
“Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti,
3 og kald hele Menigheden sammen ved indgangen til Åbenbaringsteltet!"
ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.”
4 Moses gjorde som HERREN bød ham, og Menigheden forsamlede sig ved Indgangen til Åbenbaringsteltet.
Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.
5 Og Moses sagde til Menigheden: "Dette har HERREN påbudt at gøre."
Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.”
6 Da lod Moses Aron og hans Sønner træde frem og tvættede dem med Vand.
Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi.
7 Og han gav ham Kjortelen på, omgjordede ham med Bæltet, iførte ham Kåben, gav ham Efoden på, omgjordede ham med Efodens Bælte og bandt dermed Efoden fast på ham;
Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo.
8 så anbragte han Brystskjoldet på ham, lagde Urim og Tummim i Brystskjoldet,
Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu.
9 lagde Hovedklædet om hans Hoved og fæstede Guldpladen, det hellige Diadem, på Forsiden af Hovedklædet, som HERREN havde pålagt Moses.
Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.
10 Derpå tog Moses Salveolien og salvede Boligen og alle Tingene deri og helligede dem;
Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula.
11 så bestænkede han Alteret syv Gange dermed og salvede Alteret og alt dets Tilbehør og Vandkummen med dens Fodstykke for at hellige dem;
Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula.
12 derpå udgød han. noget af Salveolien over Arons Hoved og salvede ham for at hellige ham.
Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula.
13 Derefter lod Moses Arons Sønner træde frem, iførte dem Kjortler, omgjordede dem med Bælter og bandt Huer på deres Hoveder, som HERREN havde pålagt Moses.
Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.
14 Så førte han Syndoffertyren frem, og Aron og hans Sønner lagde deres Hænder lå Syndoffertyrens Hoved.
Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo.
15 Derefter slagtede Moses den, tog Blodet og strøg med sin Finger noget deraf rundt om på Alterets Horn og rensede Alteret for Synd; men Resten af Blodet udgød han ved Alterets Fod; således helligede han det ved at skaffe Soning for det.
Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo.
16 Så tog Moses alt Fedtet på Indvoldene, Leverlappen og begge Nyrerne med Fedtet på dem og bragte det som Røgoffer på Alteret.
Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo.
17 Men Tyren, dens Hud, Kød og Skarn, brændte han uden for Lejren, som HERREN havde pålagt Moses.
Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
18 Derpå førte han Brændoffervæderen frem, og Aron og hans Sønner lagde deres Hænder på Væderens Hoved.
Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
19 Så slagtede Moses den og sprængte Blodet rundt om på Alteret;
Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo.
20 og Moses skar Væderen i Stykker og bragte Hovedet, Stykkerne og Fedtet som Røgoffer,
Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta.
21 men Indvoldene og Skinnebenene tvættede han med Vand; og så bragte Moses hele Væderen som Røgoffer på Alteret. Det var et Brændoffer til en liflig Duft, et Ildoffer for HERREN, som HERREN havde pålagt Moses.
Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.
22 Derpå førte han den anden Væder, Indsættelsesvæderen, frem, og Aron og hans Sønner lagde deres Hænder på Væderens Hoved.
Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake.
23 Så slagtede Moses den, tog noget af dens Blod og strøg det på Arons højre Øreflip og på hans højre Tommelfinger og højre Tommeltå.
Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja.
24 Derpå lod Moses Arons Sønner træde frem og strøg noget af Blodet på deres højre Øreflip og på deres højre Tommelfinger og højre Tommeltå, Men Resten af Blodet sprængte han rundt om på Alteret.
Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo.
25 Derpå tog han Fedtet, Fedthalen, alt Fedtet på Indvoldene, Leverlappen og begge Nyrerne med Fedtet på dem og den højre Kølle:
Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja.
26 Og af Kurven med de usyrede Brød, som stod for HERRENs Åsyn, tog han en usyret Kage, en Oliebrødkage og et Fladbrød og lagde dem oven på Fedtstykkerne og den højre Kølle,
Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija.
27 lagde det så alt sammen på Arons og hans Sønners Hænder og lod dem udføre Svingningen dermed for HERRENs Åsyn.
Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula.
28 Derpå tog Moses det igen fra dem og bragte det som Røgoffer på Alteret oven på Brændofferet. Det var et Indsættelsesoffer til en liflig Duft, et Ildoffer for HERREN.
Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova.
29 Så tog Moses Brystet og udførte Svingningen dermed for HERRENs Åsyn; det tilfaldt Moses som hans Del af Indsættelsesvæderen, som HERREN havde pålagt Moses.
Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.
30 Derefter tog Moses noget af Salveolien og af Blodet på Alteret og stænkede det på Aron og hans Klæder, ligeledes på hans Sønner og deres Klæder, og helligede således Aron og hans Klæder og ligeledes hans Sønner og deres Klæder.
Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.
31 Og Moses sagde til Aron og hans Sønner: "Kog Kødet ved indgangen til Åbenbaringsteltet og spis det der tillige med Brødet, som er i Indsættelseskurven, således som Budet lød til mig: Aron og hans Sønner skal spise det!
Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’
32 Men hvad der levnes af Kødet og Brødet skal I opbrænde.
Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche.
33 I syv bage må I ikke vige fra Indgangen til Åbenbaringsteltet, indtil eders Indsættelsesdage er omme; thi syv Dage varer eders Indsættelse.
Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri.
34 Ligesom i Dag har HERREN påbudt eder at gøre også de følgende Dage for at skaffe eder Soning.
Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu.
35 Ved Indgangen til Åbenbaringsteltet skal I opholde eder Dag og Nat i syv Dage og holde eder HERRENs Forskrift efterrettelig, for at I ikke skal dø; thi således lød hans Bud til mig!"
Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.”
36 Og Aron og hans Sønner gjorde alt, hvad HERREN havde påbudt ved Moses.
Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.