< 3 Mosebog 5 >
1 Hvis nogen, når han hører en Forbandelse udtale, synder ved at undlade at vidne, skønt han var Øjenvidne eller på anden Måde kender Sagen, og således pådrager sig Skyld,
“‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.
2 eller hvis nogen, uden at det er ham vitterligt, rører ved noget urent, hvad enten det nu er et Ådsel af et urent vildt Dyr eller af urent Kvæg eller urent Kryb, og han opdager det og bliver sig sin Skyld bevidst,
“‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.
3 eller når han, uden at det er ham vitterligt, rører ved Urenhed hos et Menneske, Urenhed af en hvilken som helst Art, hvorved man bliver uren, og han opdager det og bliver sig sin Skyld bevidst,
“‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
4 eller når nogen, uden at det er ham vitterligt, med sine Læber aflægger en uoverlagt Ed på at ville gøre noget, godt eller ondt, hvad nu et Menneske kan aflægge en uoverlagt Ed på, og han opdager det og bliver sig sin Skyld bevidst i et af disse Tilfælde,
“‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
5 så skal han, når han bliver sig sin Skyld bevidst i et af disse Tilfælde, bekende det, han har forsyndet sig med,
“‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo.
6 og til Bod for den Synd, han har begået, bringe HERREN et Hundyr af Småkvæget, et Får eller en Ged, som Syndoffer; da skal Præsten skaffe ham Soning for hans Synd.
Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.
7 Men hvis han ikke evner at give et Stykke Småkvæg, skal han til Bod for sin Synd bringe HERREN to Turtelduer eller Dueunger, en som Syndoffer og en som Brændoffer.
“‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza.
8 Han skal bringe dem til Præsten, og Præsten skal først frembære den, der skal bruges til Syndoffer; han skal knække Halsen på den ved Nakken uden at rive Hovedet helt af
Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu,
9 og stænke noget af Syndofferets Blod på Alterets Side, medens Resten af Blodet skal udpresses ved Alterets Fod. Det er et Syndoffer.
kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
10 Men den anden skal han ofre som Brændoffer på den foreskrevne Måde; da skal Præsten skaffe ham Soning for den Synd, han har begået, så han finder Tilgivelse.
Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.
11 Men hvis han ej heller evner at give to Turtelduer eller Dueunger, skal han som Offergave for sin Synd bringe en Tiendedel Efa fint Hvedemel til Syndoffer, men han må ikke hælde Olie derover eller komme Røgelse derpå, thi det er et Syndoffer.
“‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo.
12 Han skal bringe det til Præsten, og Præsten skal tage en Håndfuld deraf, det, som skal ofres deraf, og bringe det som Røgoffer på Alteret oven på HERRENs Ildofre. Det er et Syndoffer.
Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
13 Da skal Præsten skaffe ham Soning for den Synd, han har begået på en af de nævnte Måder, så han finder Tilgivelse. Resten skal tilfalde Præsten på samme Måde som Afgrødeofferet.
Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’”
14 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anawuza Mose kuti,
15 Når nogen gør sig skyldig i Svig og af Vanvare forsynder sig mod HERRENs Helliggaver, skal han til Bod derfor som Skyldoffer bringe HERREN en lydefri Væder af Småkvæget, der er vurderet til mindst to Sølvsekel efter hellig Vægt;
“Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula.
16 og han skal give Erstatning for, hvad han har forsyndet sig med over for det hellige, med Tillæg af en Femtedel af Værdien. Han skal give Præsten det, og Præsten skal skaffe ham Soning ved Skyldoffervæderen, så han finder Tilgivelse.
Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.
17 Når nogen, uden at det er ham vitterligt, synder ved at overtræde et af HERRENs Forbud, så han bliver skyldig og pådrager sig Skyld,
“Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa.
18 da skal han af Småkvæget bringe en lydefri Væder, der er taget god, som Skyldoffer til Præsten, og Præsten skal skaffe ham Soning for den uforsætlige Synd, han har begået, uden at den var ham vitterlig, så han finder Tilgivelse.
Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.
19 Det er et Skyldoffer; han har pådraget sig Skyld over for HERREN.
Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”