< 3 Mosebog 14 >
1 HERREN talede fremdeles til Moses og sagde:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Dette er Loven om, hvorledes man skal forholde sig med Renselsen af en spedalsk: Han skal fremstilles for Præsten,
“Malamulo a munthu wakhate pa tsiku la kuyeretsedwa kwake ndi awa: Abwere naye kwa wansembe.
3 og Præsten skal gå uden for Lejren og syne ham, og viser det sig da, at Spedalskheden er helbredt hos den spedalske,
Wansembe atuluke kunja kwa msasa ndipo amuonetsetse wodwalayo. Ngati munthu wakhateyo wachira,
4 skal Præsten give Ordre til at tage to levende, rene Fugle, Cedertræ, karmoisinrødt Garn og en Ysopkvist til den, der skal renses.
wansembe alamule anthu kuti amutengere wodwala woti ayeretsedweyo, mbalame zamoyo ziwiri zomwe Ayuda amaloledwa kudya, nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope.
5 Og Præsten skal give Ordre til at slagte den ene Fugl over et Lerkar med rindende Vand.
Wansembe alamule anthuwo kuti mbalame imodzi ayiphere mu mʼphika wa dothi pamwamba pa madzi abwino.
6 Så skal han tage den levende Fugl, Cedertræet, det kamoisinrøde Garn og Ysopkvisten og dyppe dem tillige med den levende Fugl i Blodet af den Fugl, der er slagtet over det rindende Vand,
Kenaka wansembe atenge mbalame yamoyo ija ndi kuyinyika pamodzi ndi nthambi yamkungudza, kansalu kofiirira ndi kanthambi ka hisope kaja mʼmagazi ambalame imene anayiphera pamwamba pa madzi abwino.
7 og syv Gange foretage Bestænkning på den, der skal renses for Spedalskhed, og således rense ham; derpå skal han lade den levende Fugl flyve ud over Marken.
Wansembe awaze magazi kasanu ndi kawiri pa munthu woti amuyeretse khateyo ndipo alengeze kuti munthuyo ndi woyeretsedwa. Kenaka wansembe awulutsire ku thengo mbalame yamoyoyo.
8 Men den, der skal renses, skal tvætte sine Klæder, afrage alt sit Hår og bade sig i Vand; så er han ren. Derefter må han gå ind i Lejren, men han skal syv Dage opholde sig uden for sit Telt.
“Munthu amene wayeretsedwa uja achape zovala zake, amete tsitsi lake lonse, ndipo asambe mʼmadzi. Akatero adzakhala woyeretsedwa. Atatha zimenezi munthuyo apite ku msasa wake koma akhale kunja kwa msasawo kwa masiku asanu ndi awiri.
9 På den syvende Dag skal han afrage alt sit Hår, sit Hovedhår, sit Skæg, sine Øjenbryn, alt sit Hår skal han afrage, og han skal tvætte sine Klæder og bade sit Legeme i Vand; så er han ren.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri amete tsitsi lake lonse: amete kumutu, ndevu zake, nsidze zake pamodzi ndi tsitsi lina lonse. Kenaka achape zovala zake ndi kusamba mʼmadzi, ndipo adzakhala woyeretsedwa.
10 Men den ottende dag skal han tage to lydefri Væderlam og et lydefrit, årgammelt Hunlam, desuden tre Tiendedele Efa fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer og en Log Olie.
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu munthuyo atenge ana ankhosa aamuna awiri ndi mwana wankhosa wamkazi wa chaka chimodzi. Zonsezi zikhale zopanda chilema. Atengenso chopereka chachakudya cha ufa wosalala wa makilogalamu atatu wosakaniza ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita.
11 Så skal den Præst, der foretager Renselsen, stille den, der skal renses, tillige med disse Offergaver frem for HERRENs Åsyn ved Åbenbaringsteltets Indgang.
Wansembe amene ati ayeretse munthu wodwalayo amuyimitse munthuyo ali ndi zopereka zake zonse pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
12 Og Præsten skal tage det ene Væderlam og frembære det som Skyldoffer tillige med den Log Olie, som hører dertil, og udføre Svingningen dermed for HERRENs Åsyn.
“Ndipo wansembe atenge mwana wankhosa wamwamuna mmodzi ndi kumupereka kuti akhale nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta wokwana limodzi mwa magawo atatu a lita. Wansembe aziweyule zonsezi pamaso pa Yehova kuti zikhale chopereka choweyula.
13 Og han skal slagte Lammet der, hvor Syndofferet og Brændofferet slagtes, på det hellige Sted, thi ligesom Syndofferet tilfalder Skyldofferet Præsten; det er højhelligt.
Mwana wankhosayo amuphere pa malo amene amaphera nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yopsereza, kutanthauza malo opatulika. Monga zimakhalira ndi chopereka chopepesera machimo, chopereka ichi ndi chake cha wansembe ndipo ndi chopereka choyera kopambana.
14 Derpå skal Præsten tage noget af Skyldofferets Blod, og Præsten skal stryge det på højre Øreflip af den, der skal renses, og på hans højre Tomme1finger og højre Tommeltå;
Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera kupalamula ndi kuwapaka pa msonga pa khutu lakumanja la munthu woti ayeretsedweyo. Apakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndi chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
15 og Præsten skal tage noget af den Log Olie, som hører dertil, og hælde det i sin venstre Hånd,
Wansembe atengeko mafuta pangʼono, nʼkuwathira mʼdzanja lake lamanzere,
16 og Præsten skal dyppe sin højre Pegefinger i den Olie, han har i sin venstre Hånd, og med sin Finger stænke Olien syv Gange foran HERRENs Åsyn.
aviyike chala chake cha ku dzanja lamanja mʼmafuta amene ali mʼdzanja lamanzerewo, ndi kuwaza mafutawo ndi chala chakecho kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
17 Og af den Olie, han har tilbage i sin Hånd, skal Præsten stryge noget på højre Øreflip af den, der skal renses, og på hans højre Tommelfinger og højre Tommeltå oven på Skyldofferets Blod.
Wansembe apake mafuta otsala mʼdzanja lake pa khutu lakumanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Awapakenso pa chala chake chachikulu cha ku dzanja lamanja ndiponso pa chala chake chachikulu cha ku phazi lakumanja, pamalo pamene anali atapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula paja.
18 Og Præsten skal hælde det, der er tilbage af Olien i hans Hånd, på Hovedet af den, der skal renses, og således skal Præsten skaffe ham Soning for HERRENs Åsyn.
Mafuta onse otsala mʼdzanja la wansembe awathire pamutu pa munthu woti ayeretsedwe uja, ndipo potero adzachita mwambo womupepesera pamaso pa Yehova.
19 Derpå skal Præsten ofre Syndofferet og skaffe den, der skal renses, Soning for hans Urenhed.
“Kenaka wansembe apereke nsembe yopepesera machimo kuti achite mwambo womupepesera munthu woti ayeretsedwe khate lake uja. Atatha kuchita zimenezi, wansembe aphe nyama ya nsembe yopsereza
20 Og Præsten skal ofre Brændofferet og Afgrødeofferet på Alteret og således skaffe ham Soning; så er han ren.
ndi kuyipereka pa guwa, pamodzi ndi nsembe yachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera munthu wodzayeretsedwayo, ndipo adzakhala woyera.
21 Men hvis han er fattig og ikke evner at give så meget, skal han tage et enkelt Lam til Skyldoffer. til at udføre Svingningen med, for at der kan skaffes ham Soning. desuden en Tiendedel Efa fint Hvedemel, rørt i Olie, til Afgrødeoffer og en Log Olie
“Ngati munthu woti ayeretsedweyo ndi wosauka ndipo sangathe kupeza zinthu zimenezi, apereke mwana wankhosa wamwamuna monga nsembe yopepesera kupalamula ndipo ayiweyule pochita mwambo womupepesera. Aperekenso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala osakaniza ndi mafuta kuti ikhale nsembe yachakudya, pamodzi ndi mafuta wokwanira limodzi mwa magawo atatu a lita.
22 og to Turtelduer eller Dueunger, hvad han nu evner at give, den ene skal være til Syndoffer, den anden til Brændoffer.
Aperekenso njiwa ziwiri kapena mawunda awiri zomwe iye angathe kuzipeza. Imodzi ikhale nsembe yopepesera machimo, ndi inayo ikhale ya nsembe yopsereza.
23 Dem skal han den ottende Dag efter sin Renselse bringe til Præsten ved Åbenbaringsteltets Indgang for HERRENs Åsyn.
“Pa tsiku lachisanu ndi chitatu zonsezo abwere nazo kwa wansembe, pa khomo pa tenti ya msonkhano, pamaso pa Yehova kuti munthuyo ayeretsedwe.
24 Så skal Præsten tage Skyldofferlammet med den Log Olie, som hører dertil, og Præsten skal udføre Svingningen dermed for HERRENs Åsyn.
Wansembe atenge mwana wankhosa wopereka nsembe yopepesera kupalamula, pamodzi ndi mafuta aja, ndipo aziweyule kuti zikhale nsembe yoweyula pamaso pa Yehova.
25 Og han skal slagte Skyldofferlammet, og Præsten skal tage noget af Skyldofferets Blod og stryge det på højre Øreflip af den, der skal renses, og på hans højre Tommelfinger og højre Tommeltå.
Wansembe aphe nkhosa yopereka nsembe yopepesera kupalamula ndipo atenge magazi ake ndi kuwapaka pa msonga ya khutu lakumanja la munthu amene ayeretsedweyo. Awapakenso pa chala chachikulu cha ku dzanja lamanja, ndiponso pa chala chachikulu cha ku phazi lakumanja.
26 Og af Olien skal Præsten hælde noget i sin venstre Hånd,
Kenaka wansembe athire mafuta mʼdzanja lake lamanzere,
27 og Præsten skal med sin højre Pegefinger syv Gangestænke noget af Olien, som er i hans venstre Hånd, for HERRENs Åsyn.
ndipo ndi chala chake cha ku dzanja lamanja awaze mafutawo kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova.
28 Og af Olien, som er i hans Hånd, skal Præsten stryge noget på højre Øreflip af den, der skal renses, og på hans højre Tommelfinger og højre Tommeltå oven på Skyldofferets Blod.
Apakenso mafuta omwewo amene ali mʼdzanja lake lamanja pa msonga ya khutu la kudzanja lamanja la munthu amene akuyeretsedwayo. Apakenso pa chala chachikulu cha phazi lakumanja, pamalo pamene anapakapo magazi a nsembe yopepesera kupalamula.
29 Og Resten af Olien, som er i hans Hånd, skal Præsten hælde på Hovedet af den, der skal renses, for at skaffe ham Soning for HERRENs Åsyn.
Mafuta onse otsala amene ali mʼdzanja la wansembe awapake pamutu pa munthu amene ayeretsedweyo kuti amuchitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.
30 Derpå skal han ofre den ene Turteldue eller Dueunge, hvad han nu har evnet at give,
Ndipo munthuyo apereke njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri, molingana ndi mmene anapezeramo,
31 den ene som Syndoffer, den anden som Brændoffet, sammen med Afgrødeofferet; og Præsten skal skaffe den, der skal renses, Soning for HERRENs Åsyn.
imodzi ikhale ya nsembe yopepesera machimo ndipo inayo ikhale ya nsembe yopsereza, pamodzi ndi chopereka chachakudya. Akatero ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera machimo a munthu woti ayeretsedwe.
32 Det er Loven om den, der har været angrebet af Spedalskhed og ikke evner at bringe det almindelige Offer ved sin Renselse.
“Amenewa ndi malamulo a munthu wakhate amene alibe zinthu zoti apereke pamene akuyeretsedwa.
33 Og HERREN talede til Moses og Aron og sagde:
“Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
34 Når I kommer til Kanåns Land, som jeg vil give eder i Eje, og jeg lader Spedalskhed komme frem på et Hus i eders Ejendomsland,
Mukakalowa mʼdziko la Kanaani limene ndikukupatsani kuti likhale lanu, ndipo Ine ndikakabweretsa ndere zoyanga mʼnyumba mʼdziko limenelo,
35 så skal Husets Ejer gå hen og melde det til Præsten og sige: "Der har i mit Hus vist sig noget, der ligner Spedalskhed!"
mwini wake nyumbayo adzapite kwa wansembe ndi kukamuwuza kuti, ‘Ndaona chinthu chooneka ngati ndere mʼnyumba mwanga.’
36 Da skal Præsten give Ordre til at flytte alt ud af Huset, inden han kommer for at syne Pletten, for at ikke noget af, hvad der er i Huset, skal blive urent; derpå skal Præsten komme for at syne Huset.
Tsono wansembe alamule kuti anthu atulutse zinthu zonse mʼnyumbamo iye asanalowemo ndi kukaonetsetsa ndereyo kuti mʼnyumbamo musapezeke chinthu choti achitchule chodetsedwa. Izi zitachitika, wansembe alowe mʼnyumbamo ndi kukaonamo.
37 Viser det sig da, når han syner Pletten, at Pletten på Husets Vægge frembyder grønlige eller rødlige Fordybninger, der ser ud til at ligge dybere end Væggen udenom,
Iye aonetsetse nderezo. Tsono akapeza kuti nderezo zili mʼkhoma la nyumba, ndipo ngati zili ndi mawanga obiriwira kapena ofiirira, komanso zikuoneka kuti zalowerera mpaka mʼkati mwa khoma,
38 skal Præsten gå ud af Huset til Husets Dør og holde Huset lukket i syv Dage.
wansembe atuluke mʼnyumbamo ndi kupita pa khomo, ndipo ayitseke nyumbayo masiku asanu ndi awiri.
39 På den syvende Dag skal Præsten komme igen og syne det, og hvis det da viser sig, at Pletten har bredt sig på Husets Vægge,
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri wansembe abwerenso kudzayangʼana mʼnyumbamo. Ngati ndere yafalikira mʼmakoma a nyumbayo,
40 skal Præsten give Ordre til at udtage de angrebne Sten og kaste dem hen på et urent Sted uden for Byen
wansembe alamule kuti anthu agumule miyala imene muli nderezo ndipo akayitaye kudzala la kunja kwa mzinda.
41 og til at skrabe Lerpudset af Husets indvendige Vægge og hælde det fjernede Puds ud på et urent Sted uden for Byen.
Wansembe awuze anthu kuti apale makoma onse a mʼkati mwa nyumbayo, ndipo zopalidwazo akazitaye ku malo odetsedwa a kunja kwa mudzi.
42 Derefter skal man tage andre Sten og sætte dem ind i Stedet for de gamle og ligeledes tage nyt Puds og pudse Huset dermed.
Tsono anthuwo atenge miyala ina ndi kuyilowetsa mʼmalo mwa miyala imene anagumula ija ndipo atenge dothi latsopano ndi kumata nyumbayo.
43 Hvis Pletten så atter bryder frem i Huset, efter at Stenene er taget ud, Pudset skrabet af og Huset pudset på ny,
“Ngati ndere iwonekanso mʼnyumbamo atagumula kale miyala ndiponso atayipala kale ndi kuyimatanso,
44 skal Præsten komme og syne Huset, og viser det sig da, at Pletten har bredt sig på Huset, så er det ondartet Spedalskhed, der er på Huset; det er urent.
wansembe apite kukayionetsetsenso ndipo ngati nderezo zafalikira mʼnyumbamo, ndiye kuti ndere zimenezo ndi zoopsa. Nyumba imeneyo ndi yodetsedwa.
45 Da skal man rive Huset ned, Sten, Træværk og alt Pudset på Huset, og bringe det til et urent Sted uden for Byen.
Agwetse nyumbayo, ndipo miyala yake, matabwa pamodzi ndi dothi lake lonse, zonse akazitaye kudzala lodetsedwa, kunja kwa mzinda.
46 Den, som går ind i Huset, så længe det er lukket, skal være uren til Aften;
“Aliyense amene alowa mʼnyumbamo itatsekedwa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
47 den, der sover deri skal tvætte sine Klæder, og den der spiser deri, skal tvætte sine Klæder.
Munthu amene wagona mʼnyumbamo kapena kudyeramo ayenera kuchapa zovala zake.
48 Men hvis det, når Præsten kommer og syner Huset, viser sig, at Pletten ikke har bredt sig på det, efter at det er pudset på ny, skal Præsten erklære Huset for rent, thi Pletten er helbredt.
“Koma ngati pambuyo pa kuyimata, wansembe abwera kudzaonetsetsa mʼnyumbamo napeza kuti ndereyo sinafalikire, iye alengeze kuti nyumbayo ndi yoyeretsedwa, chifukwa ndereyo yatha.
49 Da skal han for at rense Huset for Synd tage to Fugle, Cedertræ, karmoisinrødt Garn og en Ysopkvist.
Kuti nyumbayo iyeretsedwe, mwini wake atenge mbalame ziwiri, kanthambi kamkungudza, kansalu kofiirira ndi kachitsamba ka hisope.
50 Den ene Fugl skal han slagte over et Lerkar med rindende Vand,
Wansembe aphe mbalame imodzi pamwamba pa madzi abwino mu mʼphika wa dothi.
51 og han skal tage Cedertræet, Ysopkvisten, det karmoisinrøde Garn og den levende Fugl og dyppe dem i Blodet af den slagtede Fugl og det rindende Vand og syv Gange foretage Bestænkning på Huset
Kenaka atenge kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope, kansalu kofiirira pamodzi ndi mbalame yamoyo ija, zonsezi aziviyike mʼmagazi a mbalame yophedwa ija, ndiponso mʼmadzi abwino aja, ndipo awaze nyumbayo kasanu ndi kawiri
52 og således rense det for Synd med Fuglens Blod, det rindende Vand, den levende Fugl, Cedertræet, Ysopkvisten og det karmoisinrøde Garn.
Akatero ndiye kuti wayeretsa nyumbayo ndi magazi a mbalame, madzi abwino, mbalame yamoyo, kanthambi kamkungudza, kachitsamba ka hisope ndi kansalu kofiirira.
53 Og den levende Fugl skal han lade flyve ud af Byen hen over Marken og således skaffe Huset Soning; så er det rent.
Kenaka ayiwulutsire mbalame yamoyo ija kuthengo, kunja kwa mzinda. Pamenepo ndiye kuti wansembe wachita mwambo wopepesera nyumbayo, ndipo idzakhala yoyeretsedwa.”
54 Det er Loven om al Slags Spedalskhed og Skurv,
Amenewa ndiwo malamulo a nthenda ya khate, bala lonyerenyetsa,
55 om Spedalskhed på Klæder og Huse
nguwi za pa zovala, ndere za mʼnyumba,
56 og om Hævelser, Udslæt og lyse Pletter,
khate la chithupsa, khate la mʼbuko ndi khate la banga
57 til Belæring om, når noget er urent, og når det er rent. Det er Loven om Spedalskhed.
kuti mudziwe ngati chinthucho ndi choyeretsedwa kapena chodetsedwa. Amenewa ndiwo malamulo a nthenda zonse za khate.