< Klagesangene 3 >

1 Jeg er den, der så nød ved hans vredes ris,
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 mig har han ført og ledt i det tykkeste Mulm,
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 ja, Hånden vender han mod mig Dagen lang.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 Mit Bød og min Hud har han opslidt, brudt mine Ben,
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 han mured mig inde, omgav mig med Galde og Møje,
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 lod mig bo i Mørke som de, der for længst er døde.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 Han har spærret mig inde og lagt mig i tunge Lænker.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 Om jeg end råber og skriger, min Bøn er stængt ude.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 Han spærred mine Veje med Kvader, gjorde Stierne kroge.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 Han blev mig en lurende Bjørn, en Løve i Baghold;
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 han ledte mig vild, rev mig sønder og lagde mig øde;
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 han spændte sin Bue; lod mig være Skive for Pilen.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 Han sendte sit Koggers Sønner i Nyrerne på mig;
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 hvert Folk lo mig ud og smæded mig Dagen lang,
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 med bittert mætted han mig, gav mig Malurt at drikke.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 Mine Tænder lod han bide i Flint, han trådte mig i Støvet;
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 han skilte min Sjæl fra Freden, jeg glemte Lykken
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 og sagde: "Min Livskraft, mit Håb til HERREN er ude."
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 At mindes min Vånde og Flakken er Malurt og Galde;
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 min Sjæl, den mindes det grant den grubler betynget.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 Det lægger jeg mig på Sinde, derfor vil jeg håbe:
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 HERRENs Miskundhed er ikke til Ende, ikke brugt op,
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 hans Nåde er ny hver Morgen, hans Trofasthed stor.
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 Min Del er HERREN, (siger min Sjæl, ) derfor håber jeg på ham.
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 Dem, der bier på HERREN, er han god, den Sjæl, der ham søger;
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 det er godt at håbe i Stilhed på HERRENs Frelse,
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 godt for en Mand, at han bærer Åg i sin Ungdom.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 Han sidde ensom og tavs, når han lægger det på ham;
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 han trykke sin Mund mod Støvet, måske er der Håb.
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Række Kind til den, der slår ham, mættes med Hån.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 Thi Herren bortstøder ikke for evigt,
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 har han voldt Kvide, så ynkes han, stor er hans Nåde;
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 ej af Hjertet plager og piner han Menneskens Børn.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 Når Landets Fanger til Hobe trædes under Fod,
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 når Mandens Ret for den Højestes Åsyn bøjes,
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 når en Mand lider Uret i sin Sag mon Herren ej ser det?
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 Hvo taler vel, så det sker, om ej Herren byder?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 Kommer ikke både ondt og godt fra den Højestes Mund?
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Over hvad skal den levende sukke? Hver over sin Synd!
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 Lad os ransage, granske vore Veje og vende os til HERREN,
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 løfte Hænder og Hjerte til Gud i Himlen;
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 vi syndede og stod imod, du tilgav ikke,
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 men hylled dig i Vrede, forfulgte os, dræbte uden Skånsel,
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 hylled dig i Skyer, så Bønnen ej nåed frem;
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 til Skarn og til Udskud har du gjort os midt iblandt Folkene.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 De opspærred Munden imod os, alle vore Fjender.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 Vor Lod blev Gru og Grav og Sammenbruds Øde;
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Vandstrømme græder mit Øje, mit Folk brød sammen.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 Hvileløst strømmer mit Øje, det kender ej Ro,
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 før HERREN skuer ned fra Himlen, før han ser til.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Synet af Byens Døtre piner min Sjæl.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 Jeg joges som en Fugl af Fjender, hvis Had var grundløst,
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 de spærred mig inde i en Grube, de stenede mig;
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 Vand strømmed over mit Hoved, jeg tænkte: "Fortabt!"
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 Dit Navn påkaldte jeg, HERRE, fra Grubens Dyb;
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 du hørte min Røst: "O, gør dig ej døv for mit Skrig!"
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Nær var du den Dag jeg kaldte, du sagde: "Frygt ikke!"
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 Du førte min Sag, o Herre, genløste mit Liv;
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 HERRE, du ser, jeg lider Uret. skaf mig min Ret!
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 Al deres Hævnlyst ser du, alle deres Rænker,
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 du hører deres Smædeord HERRE, deres Rænker imod mig,
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 mine Fjenders Tale og Tanker imod mig bestandig.
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Se dem, når de sidder eller står, deres Nidvise er jeg.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 Dem vil du gengælde, HERRE, deres Hænders Gerning,
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 gør deres Hjerte forhærdet din Forbandelse over dem!
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 forfølg dem i Vrede, udryd dem under din Himmel.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.

< Klagesangene 3 >