< Josua 1 >

1 Efter at HERRENs Tjener Moses var død, sagde HERREN til Moses's Medhjælper Josua, Nuns Søn:
Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
2 "Min Tjener Moses er død; bryd nu op tillige med hele dette Folk og gå over Jordan derhenne til det Land, jeg vil give dem, Israeliterne.
“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
3 Ethvert Sted, eders Fod betræder, giver jeg eder, som jeg lovede Moses.
Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
4 Fra Ørkenen og Libanon til den store Flod, Eufratfloden, hele Hetiternes Land, og til det store Hav i Vest skal eders Landemærker nå.
Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
5 Så længe du lever, skal det ikke være muligt for nogen at holde Stand imod dig; som jeg var med Moses, vil jeg være med dig; jeg vil ikke slippe dig og ikke forlade dig.
Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
6 Vær frimodig og stærk, thi du skal skaffe dette Folk det Land i Eje, som jeg tilsvor deres Fædre at ville give dem.
“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
7 Vær kun helt frimodig og stærk. så du omhyggeligt handler efter hele den Lov, min Tjener Moses pålagde dig, vig ikke derfra til højre eller venstre, for at du må have Lykken med dig i alt, hvad du tager dig for.
Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
8 Denne Lovbog skal ikke vige fra din Mund, og du skal grunde over den Dag og Nat, for at du omhyggeligt kan handle efter alt, hvad der står skrevet i den; thi da vil det gå dig vel i al din Færd, og Lykken vil følge dig.
Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
9 Har jeg ikke budt dig: Vær frimodig og stærk; vær ikke bange og bliv ikke forfærdet, thi HERREN din Gud er med dig i alt, hvad du tager dig for!"
Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
10 Josua bød derpå Folkets Tilsynsmænd:
Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
11 "Gå omkring i Lejren og byd Folket: Sørg for Rejsetæring, thi om tre Dage skal I gå over Jordan derhenne for at drage ind og tage det Land i Besiddelse, som HERREN eders Gud vil give eder i Eje!"
“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
12 Men til Rubeniterne, Gaditerne og Manasses halve Stamme sagde Josua:
Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
13 "Husk på, hvad HERRENs Tjener Moses bød eder, da han sagde: HERREN eders Gud bringer eder nu til Hvile og giver eder Landet her!
“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
14 Eders Kvinder og Børn og Kvæg skal blive i det Land, Moses gav eder hinsides Jordan; men I selv, alle våbenføre, skal væbnet drage over i Spidsen for eders Brødre og hjælpe dem,
Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
15 indtil HERREN har bragt eders Brødre til Hvile ligesom eder, når også de har taget det Land i Besiddelse, som HERREN eders Gud vil give dem. Så kan I vende tilbage til eders eget Land og tage det i Besiddelse, det, som HERRENs Tjener Moses gav eder østpå hinsides Jordan!"
Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
16 Da svarede de Josua: "Alt, hvad du har pålagt os, vil vi gøre, og vi vil gå overalt, hvor du sender os;
Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
17 som vi har adlydt Moses i alt, vil vi adlyde dig. Måtte kun HERREN din Gud være med dig, som han var med Moses!
Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
18 Enhver, som sætter sig op imod dine Befalinger og ikke adlyder dine Ord i alt, hvad du pålægger ham, skal dø. Vær kun modig og uforsagt!"
Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”

< Josua 1 >