< Josua 9 >
1 Da alle Kongerne på den anden Side af Jordan, i Bjergene og i Lavlandet og langs hele det store Havs Kyst hen imod Libanon, Hetiterne, Amoriterne, Kana'anæerne, Perizziterne, Hivviterne og Jebusiterne, hørte, hvad der var sket,
Mafumu onse okhala kumadzulo kwa Yorodani atamva zimenezi pamodzi ndi mafumu okhala ku mayiko a ku mapiri, mu zigwa, mʼmbali mwa Nyanja yayikulu mpaka ku Lebanoni (mafumu a Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi, ndi Ayebusi),
2 samlede de sig for i Fællesskab at kæmpe mod Josua og Israel.
anapangana kuti achite nkhondo ndi Yoswa ndi Israeli.
3 Men da Indbyggerne i Gibeon hørte, hvad Josua havde gjort ved Jeriko og Aj,
Koma Ahivi ena a ku Gibiyoni atamva zomwe Yoswa anachitira mizinda ya Yeriko ndi Ai,
4 greb også de til en List; de gik hen og forsynede sig med Rejsetæring, læssede nogle slidte Sække og nogle slidte, sprukne, stoppede Vinsække på deres Æsler
anaganiza zochita zachinyengo. Anapita nasenzetsa abulu awo chakudya mʼmatumba akalekale ndiponso matumba a vinyo achikopa ongʼambikangʼambika.
5 og tog slidte, lappede Sko på Fødderne og slidte Klæder på Kroppen, og alt deres Rejsebrød var tørt og mullent.
Anthuwa anavala nsapato zakutha ndi zazigamba ndiponso anavala sanza. Buledi wawo yense anali wowuma ndi wowola.
6 Så gik de til Josua i Lejren ved Gilgal og sagde til ham og Israels Mænd: "Vi kommer fra et fjernt Land; slut derfor Pagt med os!"
Ndipo anapita kwa Yoswa ku msasa ku Giligala ndikumuwuza kuti, pamodzi ndi Aisraeli onse, “Ife tachokera ku dziko lakutali, ndipo tikufuna kuti muchite mgwirizano ndi ife.”
7 Israels Mænd svarede Hivviterne: "Det kunde være, at I bor her midt iblandt os, hvorledes kan vi da slutte Pagt med eder?"
Koma Aisraeli anayankha Ahiviwo kuti, “Mwinatu inu mukukhala pafupi ndi ife. Tsono ife tingachite bwanji mgwirizano ndi inu?”
8 De sagde til Josua: "Vi er dine Trælle!" Josua spurgte dem så: "Hvem er I, og hvorfra kommer I?"
Iwo anati kwa Yoswa, “Ife ndife akapolo anu.” Tsono Yoswa anawafunsa kuti, “Inu ndinu yani ndipo mukuchokera kuti?”
9 Og de svarede ham: "Fra et såre fjernt Land er dine Trælle kommet for HERREN din Guds Navns Skyld; thi vi har hørt hans Ry og alt, hvad han gjorde i Ægypten,
Iwo anayankha kuti, “Akapolo anufe tachokera ku dziko lakutali chifukwa tamva za Yehova Mulungu wanu. Tamva mbiri yonse ya zimene Iye anachita ku Igupto,
10 og alt, hvad han gjorde mod de to Amoriterkonger hinsides Jordan, Kong Sihon af Hesjbon og Kong Og af Basan, som boede i Asjtarot.
ndi zonse zimene anachita kwa mafumu awiri a Aamori kummawa kwa Yorodani, mfumu Sihoni ya Hesiboni ndi Ogi mfumu ya Basani amene amalamulira ku Asiteroti.
11 og vore Ældste og alle Indbyggerne i vort Land sagde til os: Tag Rejse tæring med eder, drag dem i Møde og sig til dem: Vi er eders Trælle; slut derfor nu Pagt med os!
Tsono akuluakulu athu ndi onse amene akukhala mʼdziko lathu anati kwa ife. Tengani chakudya cha pa ulendo wanu. Pitani mukakumane nawo ndipo mukati kwa iwo, ‘Ife ndife akapolo anu, ndipo tikufuna kuti mugwirizane nafe za mtendere.’”
12 Vort Brød her var endnu varmt, da vi tog det med hjemmefra, dengang vi begav os af Sted for at drage til eder; men se, nu er det tørt og mullent;
Buledi wathuyu anali wotentha pamene timanyamuka ku mudzi kubwera kwa inu. Koma tsopano taonani ali gwaa ndiponso wawola.
13 og vore Vinsække her var nye, da vi fyldte dem; se, nu er de sprukne; og vore Klæder og Sko her er slidte, fordi Vejen var så lang!"
Zikopa zimene tinathiramo vinyozi zinali zatsopano, koma taonani zathetheka. Zovala zathu ndi nsapato zathu zatha chifukwa cha kutalika kwa ulendo.
14 Så tog Mændene af deres Rejsetæring; men HERREN rådspurgte de ikke.
Aisraeli anatengako chakudya chawo koma sanafunse kwa Yehova.
15 Og Josua tilsagde dem Fred og sluttede Overenskomst med dem og lovede at lade dem leve, og Menighedens Øverster tilsvor dem det.
Choncho Yoswa anapangana nawo za mtendere kuti sadzawapha, ndipo atsogoleri a gulu anavomereza pochita lumbiro.
16 Men tre Dage efter at de havde sluttet Pagt med dem, hørte de, at de var fra den nærmeste Omegn og boede midt iblandt dem.
Patatha masiku atatu atachita mgwirizano wa mtendere ndi Agibiyoni, Aisraeli anamva kuti anali anansi awo, anthu amene amakhala nawo pafupi.
17 Og Israeliterne brød op og kom den tredje Dag til deres Byer, det var Gibeon, Kefira, Beerot og Kirjat Jearim.
Tsono Aisraeli ananyamuka ulendo ndipo tsiku lachitatu anafika ku mizinda ya Gibiyoni, Kefira, Beeroti ndi Kiriati-Yearimu.
18 Men Israeliterne dræbte dem ikke, fordi Menighedens Øverster havde, tilsvoret dem Fred ved HERREN, Israels Gud. Da knurrede hele Menigheden mod Øversterne;
Koma Aisraeli sanawaphe anthuwo chifukwa atsogoleri awo anali atalonjeza mʼdzina la Yehova Mulungu wa Israeli za Agibiyoniwo. Koma anthu onse anatsutsana ndi atsogoleriwo.
19 men alle Øversterne sagde til hele Menigheden: "Vi har tilsvoret dem Fred ved HERREN, Israels Gud, derfor kan vi ikke gøre dem noget ondt.
Koma atsogoleriwo anayankha kuti, “Ife tinawalonjeza mʼdzina la Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo tsopano sitingawaphe.
20 Men dette vil vi gøre med dem, når vi skåner deres Liv, at der ikke skal komme Vrede over os for den Ed, vi svor dem:
Chimene tidzachita nawo ndi ichi: Tidzawasiya akhale ndi moyo kuti mkwiyo wa Yehova usatigwere chifukwa chophwanya lonjezo limene tinawalonjeza.”
21 De skal blive i Live, men være Brændehuggere og Vandbærere for hele Menigheden." Og hele Menigheden gjorde, som Øverstene havde sagt.
Anapitiriza kunena kuti “Asiyeni akhale ndi moyo, komabe akhale otidulira mitengo ndi kutitungira madzi ogwiritsa ntchito pa chipembedzo.” Lonjezo la atsogoleriwo linasungidwa.
22 Og Josua lod dem kalde og talte således til dem: "Hvorfor førte I os bag Lyset og sagde, at I havde hjemme langt borte fra os, skønt I bor her midt iblandt os?
Kenaka Yoswa anayitanitsa Agibiyoni aja nawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani inu munatinyenga ponena kuti mumachokera kutali pamene zoona zake nʼzoti mumakhala pafupi pomwe pano?
23 Derfor skal I nu være forbandede, og ingen af eder skal nogen Sinde ophøre at være Træl; Brændehuggere og Vandbærere skal I være ved min Gus Hus!"
Tsopano popeza mwachita izi, Mulungu wakutembererani ndipo palibe wina mwa inu amene akhale mfulu. Nthawi zonse inu muzidzatidulira nkhuni ndi kutitungira madzi ku Nyumba ya Yehova.”
24 De svarede Josua og sagde:"Det var blevet dine Trælle sagt, at HERREN din Gud pålagde sin Tjener Moses, at når han gav eder hele Landet, skulde I udrydde alle Landets Indbyggere foran eder. Da påkom der os stor Frygt for, at I skulde tage vort Liv; derfor handlede vi således.
Iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife akapolo anufe tinachita zimenezi chifukwa tinamva bwino lomwe kuti Yehova Mulungu wanu analamula Mose mtumiki wake kuti adzakupatsani dziko lonseli ndi kuti anthu onse okhalamo adzaphedwe. Tsono ife tinachita mantha aakulu ndipo tinachita zimenezi pofuna kupulumutsa miyoyo yathu.
25 Men se, nu er vi i din Hånd; gør med os, som det tykkes dig godt og ret!"
Tsopanotu ife tili mʼmanja mwanu, ndipo inu chitani nafe monga kukukomerani.”
26 Da handlede han således med dem; han friede dem fra Israeliternes Hånd, så de ikke dræbte dem;
Tsono Yoswa anawapulumutsa mʼmanja mwa Aisraeli ndipo sanawaphe.
27 men Josua gjorde dem den Dag til Brændehuggere og Vandbærere for Menigheden og for HERRENs Alter på det Sted, han vilde udvælge. Og det er de den Dag i Dag.
Kuyambira tsiku limenelo Agibiyoni aja anasanduka odula nkhuni zaguwa lansembe la Yehova ndiponso otunga madzi. Mpaka lero lino iwo akuchitabe zimenezi kulikonse kumene Yehova anasankha.