< Josua 20 >
1 Og HERREN talede til Josua og sagde
Pambuyo pake Yehova anati kwa Yoswa:
2 "Tal til Israeliterne og sig: Afgiv de Tilflugtsbyer, jeg talede til eder om ved Moses,
“Uza Aisraeli kuti apatule mizinda yopulumukiramo, monga ine ndinakulangizira kudzera mwa Mose,
3 for at en Manddraber, der uforsætligt og af Vanvare slår en ihjel, kan ty til dem, så at de kan være eder Tilflugtssteder mod Blodhævneren.
kuti aliyense amene wapha munthu mosazindikira osati mwadala azithawirako. Motero adzatetezedwa kwa wolipsira.
4 Når han tyr hen til en af disse Byer og stiller sig i Byportens Indgang og forebringer sin Sag for Byens Ældste, skal de optage ham i Byen hos sig og anvise ham et Sted, hvor han kan bo bos dem;
Ngati munthu wathawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi, akafike pa malo oweruzira milandu amene ali pa chipata cha mzindawo ndipo akafotokoze mlandu wake pamaso pa akuluakulu a mzindawo. Kenaka iwo adzamulola kulowa mu mzinda wawo ndi kumupatsa malo woti akhale nawo.
5 og når Blodhævneren forfølger ham, må de ikke udlevere Manddraberen til ham, thi han har slået sin Næste ihjel af Vanvare uden i Forvejen at have båret Nag til ham;
Ngati munthu wolipsirayo amutsatira komweko atsogoleriwo asapereke munthu wakuphayo chifukwa anapha Mwisraeli mnzakeyo mosazindikira, osati mwachiwembu.
6 han skal blive boende i denne By, indtil han har været stillet for Menighedens Domstol, eller den Mand, som på den Tid er Ypperstepræst, dør; derefter kan Manddraberen vende tilbage til sin By og sit Hjem, den By, han er flygtet fra."
Munthu wakuphayo adzakhalabe mu mzindawo mpaka atayimbidwa mlandu pamaso pa gulu lonse, ndiponso mpaka atamwalira mkulu wa ansembe amene akutumikira pa nthawiyo. Pamenepo munthuyo atha kubwereranso ku mudzi kwawo kumene anachoka mothawa kuja.”
7 Da helligede de Kedesj i Galilæa i Naftalis Bjerge, Sikem i Efrims Bjerge og Kirjat-Arba, det er Hebron, i Judas Bjerge.
Choncho iwo anapatula Kedesi mʼdera la Galileya ku mapiri a Nafutali, Sekemu ku mapiri a Efereimu, ndi Kiriati Ariba (ndiye Hebroni) ku mapiri a Yuda.
8 Og østen for Jordan afgav de Bezer i Ørkenen, på Højsletten, af Rubens Stamme, Ramot i Gilead at Gads Stamme og Golan i Basan af Manasses Stamme.
Kummawa kwa Yorodani, mʼmapiri a chipululu a kummawa kwa Yeriko, anapatula Bezeri pakati pa dera la fuko la Rubeni. Anapatulanso Ramoti ku Giliyadi mʼdera la fuko la Gadi, ndiponso Golani ku Basani mʼdera la fuko la Manase.
9 Det var de Byer, som fastsattes for alle Israeliterne og de fremmede, som bor iblandt dem, i det Øjemed at enhver, der uforsætligt slår en ihjel, kan ty derhen og undgå Døden for Blodhævnerens Hånd, før han har været stillet for Menighedens Domstol.
Imeneyi ndiyo inali mizinda yopulumukiramo ya Aisraeli onse ngakhalenso mlendo wokhala pakati pawo. Munthu aliyense wopha mnzake mwangozi ankathawira ku mizinda imeneyi. Munthu wolipsira sankaloledwa kuti aphe munthu wothawayo ngati mlandu wake sunazengedwe pamaso pa gulu lonse.