< Johannes 8 >

1 Men Jesus gik til Oliebjerget.
Koma Yesu anapita ku phiri la Olivi.
2 og årle om Morgenen kom han igen i Helligdommen, og hele Folket kom til ham; og han satte sig og lærte dem.
Mmamawa Iye anaonekeranso ku Nyumba ya Mulungu kumene anthu onse anamuzungulira ndipo Iye anakhala pansi nawaphunzitsa.
3 Men de skriftkloge og Farisæerne føre en Kvinde til ham, greben i Hor, og stille hende frem i Midten.
Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi anabweretsa mkazi amene anagwidwa akuchita chigololo. Iwo anamuyimiritsa patsogolo pa anthu ndipo
4 Og de sige til ham: "Mester! denne Kvinde er greben i Hor på fersk Gerning.
anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, mkazi uyu tinamugwira akuchita chigololo.
5 Men Moses bød os i Loven, at sådanne skulle stenes; hvad siger nu du?"
Mʼmalamulo a Mose anatilamulira kuti akazi otere tiwagende ndi miyala. Tsopano Inu mukuti chiyani?”
6 Men dette sagde de for at friste ham, for at de kunde have noget at anklage ham for. Men Jesus bøjede sig ned og skrev med Fingeren på Jorden.
Iwo anagwiritsa ntchito funsoli ngati msampha, ndi cholinga choti apeze chifukwa cha kumuneneza Iye. Koma Yesu anawerama pansi ndi kuyamba kulemba pa dothi ndi chala chake.
7 Men da de bleve ved at spørge ham, rettede han sig op og sagde til dem: "Den iblandt eder, som er uden Synd, kaste først Stenen på hende!"
Pamene iwo anapitirira kumufunsa, Iye anaweramuka ndipo anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu alipo wopanda tchimo, ayambe iyeyo kumugenda ndi miyala mkaziyu.”
8 Og han bøjede sig atter ned og skrev på Jorden.
Iye anaweramanso pansi ndi kulemba pa dothi.
9 Men da de hørte det, gik de bort, den ene efter den anden, fra de ældste til de yngste, og Jesus blev alene tilbage med Kvinden, som stod der i Midten.
Iwo atamva izi anayamba kuchoka mmodzimmodzi, akuluakulu poyamba, mpaka Yesu anatsala yekha ndi mkaziyo atayimirira pomwepo.
10 Men da Jesus rettede sig op og ingen så uden Kvinden, sagde han til hende: "Kvinde! hvor ere de henne? Var der ingen, som fordømte dig?,"
Yesu anaweramuka ndipo anamufunsa iye kuti, “Akuluakulu aja ali kuti? Kodi palibe amene wakutsutsa?”
11 Men hun sagde: "Herre! ingen." Da sagde Jesus: "Heller ikke jeg fordømmer dig; gå bort, og synd ikke mere!"
Iye anati, “Ambuye, palibe ndi mmodzi yemwe.” “Inenso sindikukutsutsa iwe. Pita kuyambira tsopano usakachimwenso.”
12 Jesus talte da atter til dem og sagde: "Jeg er Verdens Lys; den, som følger mig, skal ikke vandre i Mørket, men have Livets Lys."
Yesu atayankhulanso kwa anthu, anati, “Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi. Aliyense amene anditsata Ine sadzayenda mu mdima, koma adzakhala ndi kuwala kotsogolera anthu ku moyo.”
13 Da sagde Farisæerne til ham: "Du vidner om dig selv; dit Vidnesbyrd er ikke sandt."
Afarisi anamutsutsa Iye nati, “Iwe ukudzichitira umboni wa Iwe mwini, umboni wako siwoona.”
14 Jesus svarede og sagde til dem: "Om jeg end vidner om mig selv. er mit Vidnesbyrd sandt; thi jeg ved, hvorfra jeg kom, og hvor jeg går hen; men I vide ikke, hvorfra jeg kommer, og hvor jeg går hen.
Yesu anayankha kuti, “Ngakhale Ine ndidzichitire umboni, umboni wangawu ndi woona, pakuti Ine ndikudziwa kumene ndinachokera ndi kumene ndikupita. Koma inu simukudziwa ndi pangʼono pomwe kumene ndinachokera kapena kumene ndikupita.
15 I dømme efter Kødet; jeg dømmer ingen.
Inu mumaweruza potsata maganizo a anthu chabe. Ine sindiweruza munthu wina aliyense.
16 Men om jeg også dømmer, er min Dom sand; thi det er ikke mig alene, men mig og Faderen, han, som sendte mig.
Koma Ine ndikati ndiweruze, ndimaweruza molondola, chifukwa Ine sindili ndekha koma ndili ndi Atate amene anandituma.
17 Men også i eders Lov er der skrevet, at to Menneskers Vidnesbyrd er sandt.
Mʼmalamulo anu munalembedwa kuti umboni wa anthu awiri ndi wovomerezeka.
18 Jeg er den, der vidner om mig selv, og Faderen, som sendte mig, vidner om mig."
Ine ndikudzichitira ndekha umboni; ndipo mboni inanso ndi Atate amene anandituma.”
19 Derfor sagde de til ham: "Hvor er din Fader?" Jesus svarede: "I kende hverken mig eller min Fader; dersom I kendte mig, kendte I også min Fader."
Kenaka iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi Atate anuwo ali kuti?” Yesu anayankha kuti, “Inu simundidziwa Ine. Atate anganso simuwadziwa. Mukanandidziwa Ine, mukanawadziwanso Atate anga.”
20 Disse Ord talte Jesus ved Tempelblokken, da han lærte i Helligdommen; og ingen greb ham, fordi hans Time endnu ikke var kommen.
Iye anayankhula mawu awa pamene amaphunzitsa Nyumba ya Mulungu pafupi ndi malo amene amaponyapo zopereka. Komabe palibe amene anamugwira Iye, chifukwa nthawi yake inali isanakwane.
21 Da sagde han atter til dem: "Jeg går bort, og I skulle lede efter mig, og I skulle dø i eders Synd; hvor jeg går hen, kunne I ikke komme."
Kenakanso Yesu anawawuza kuti, “Ine ndikupita, ndipo mudzandifunafuna, koma mudzafa muli mʼmachimo anu. Kumene ndikupita, inu simungabwereko.”
22 Da sagde Jøderne: "Mon han vil slå sig selv ihjel, siden han siger: Hvor jeg går hen, kunne I ikke komme?"
Izi zinachititsa Ayuda kufunsa kuti, “Kodi adzadzipha yekha? Kodi ndicho chifukwa chake akuti, ‘Kumene ndikupita, inu simungabwereko?’”
23 Og han sagde til dem: "I ere nedenfra, jeg er ovenfra; I ere af denne Verden, jeg er ikke af denne Verden.
Koma Iye anapitiriza kuti, “Inu ndi ochokera pansi pano. Ine ndine wochokera kumwamba. Inu ndinu anthu a dziko la pansi. Ine sindine wa dziko lapansi lino.
24 Derfor har jeg sagt eder, at I skulle dø i eders Synder; thi dersom I ikke tro, at det er mig, skulle I dø i eders Synder."
Ine ndinakuwuzani kuti mudzafera mʼmachimo anu ngati simukhulupirira kuti Ine Ndine. Ndithu inu mudzafera mʼmachimo anu.”
25 De sagde da til ham: "Hvem er du?" Og Jesus sagde til dem: "Just det, som jeg siger eder.
Iwo anafunsa kuti, “Ndinu ndani?” Yesu anayankha kuti, “Monga Ine ndakhala ndikunena nthawi yonseyi,
26 Jeg har meget at tale og dømme om eder; men den, som sendte mig, er sanddru, og hvad jeg har hørt af ham, det taler jeg til Verden."
ndili ndi zambiri zoti ndinene zoweruza inu. Koma Iye amene anandituma ndi woona, ndipo chimene Ine ndamva kuchokera kwa Iye, ndi chimene ndimaliwuza dziko lapansi.”
27 De forstode ikke, at han talte til dem om Faderen.
Iwo sanazindikire kuti Iye amawawuza za Atate ake.
28 Da sagde Jesus til dem: "Når I få ophøjet Menneskesønnen, da skulle I kende, at det er mig, og at jeg gør intet af mig selv; men som min Fader har lært mig, således taler jeg.
Choncho Yesu anati, “Inu mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziwa kuti Ine Ndine. Mudzadziwa kuti sindichita kalikonse pa Ine ndekha koma ndimayankhula zokhazo zimene Atate anandiphunzitsa.
29 Og han, som sendte mig, er med mig; han har ikke ladet mig alene, fordi jeg; gør altid det, som er ham til Behag."
Iye amene anandituma Ine ali nane pamodzi. Iye sanandisiye ndekha popeza nthawi zonse ndimachita zomwe zimamukondweretsa Iye.”
30 Da han talte dette, troede mange på ham.
Pamene Iye ankayankhula zimenezi, ambiri anamukhulupirira.
31 Jesus sagde da til de Jøder, som vare komne til Tro på ham: "Dersom I blive i mit Ord, ere I sandelig mine Disciple,
Kwa Ayuda amene anamukhulupirira, Yesu anati, “Ngati inu mutsatira chiphunzitso changa, ndithu ndinu ophunzira anga.
32 og I skulle erkende Sandheden, og Sandheden skal frigøre eder."
Tsono mudzadziwa choonadi, ndipo choonadicho chidzakumasulani.”
33 De svarede ham: "Vi ere Abrahams Sæd og have aldrig været nogens Trælle; hvorledes siger du da: I skulle vorde frie?"
Iwo anamuyankha Iye kuti, “Ife ndife zidzukulu za Abrahamu ndipo sitinakhalepo akapolo a wina aliyense. Kodi mukunena bwanji kuti, ‘Ife tidzamasulidwa?’”
34 Jesus svarede dem: "Sandelig, sandelig, siger jeg eder, hver den, som gør Synden, er Syndens Træl.
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wochita tchimo ndi kapolo wa tchimolo.
35 Men Trællen bliver ikke i Huset til evig Tid, Sønnen bliver der til evig Tid. (aiōn g165)
Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. (aiōn g165)
36 Dersom da Sønnen får frigjort eder, skulle I være virkelig frie.
Nʼchifukwa chake ngati Mwana adzakumasulani, mudzakhala mfulu ndithu.
37 Jeg ved, at I ere Abrahams Sæd; men I søge at slå mig ihjel, fordi min Tale ikke finder Rum hos eder.
Ine ndikudziwa kuti inu ndinu zidzukulu za Abrahamu. Chonsecho inu mwakonzeka kundipha Ine, chifukwa mawu anga alibe malo mwa inu.
38 Jeg taler det, som jeg har set hos min Fader; så gøre også I det, som I have hørt af eders Fader."
Ine ndikukuwuzani zimene ndaziona pamaso pa Atate, ndipo inu mukuchita zimene mwazimva kwa abambo anu.”
39 De svarede og sagde til ham: "Vor Fader er Abraham." Jesus sagde til dem: "Dersom I vare Abrahams Børn, gjorde I Abrahams Gerninger.
Iwo anayankha kuti, “Ife abambo athu ndi Abrahamu.” Yesu anati, “Inu mukanakhala ana a Abrahamu, bwenzi mukuchita zinthu zimene Abrahamuyo ankachita.
40 Men nu søge I at slå mig ihjel, et Menneske, der har sagt eder Sandheden, som jeg har hørt af Gud; dette gjorde Abraham ikke.
Koma mmene zililimu, inu mwatsimikiza kundipha Ine, munthu amene ndinakuwuzani choonadi chimene Ine ndinachimva kuchokera kwa Mulungu. Abrahamu sanachite zinthu zoterezi.
41 I gøre eders Faders Gerninger." De sagde til ham: "Vi ere ikke avlede i Hor; vi have een Fader, Gud."
Inu mukuchita zinthu zimene abambo anu amachita.” Iwo anatsutsa kuti, “Ife si ana amʼchigololo, Atate amene tili nawo ndi Mulungu yekha.”
42 Jesus sagde til dem: "Dersom Gud var eders Fader, da elskede I mig; thi jeg er udgået og kommen fra Gud; thi jeg er heller ikke kommen af mig selv, men han har udsendt mig.
Yesu anawawuza kuti, “Mulungu akanakhala Atate anu, inu mukanandikonda Ine, pakuti Ine ndinachokera kwa Mulungu ndipo tsopano ndili pano. Ine sindinabwere mwa Ine ndekha.
43 Hvorfor forstå I ikke min Tale? fordi I ikke kunne høre mit Ord.
Nʼchifukwa chiyani simukumvetsetsa mawu anga? Chifukwa chake nʼchakuti simungathe kumva zoyankhula zanga.
44 I ere af den Fader Djævelen, og eders Faders Begæringer ville I gøre. Han var en Manddraber fra Begyndelsen af, og han står ikke i Sandheden; thi Sandhed er ikke i ham. Når han taler Løgn, taler han af sit eget; thi han er en Løgner og Løgnens Fader.
Inu ndinu ana a mdierekezi. Iye ndiye abambo anu ndipo mukufuna kuchita zimene abambo anuwo amakhumba. Iye anali wakupha kuyambira pachiyambi, sanasunge choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene Iye anena bodza, amayankhula chiyankhulo chobadwa nacho, popeza ndi wabodza ndipo ndi bambo wa mabodza.
45 Men mig tro I ikke, fordi jeg siger Sandheden.
Koma chifukwa ndikuwuzani choonadi, inu simukundikhulupirira Ine!
46 Hvem af eder kan overbevise mig om nogen Synd? Siger jeg Sandhed, hvorfor tro I mig da ikke?
Ndani mwa inu angatsimikize kuti ndine wochimwa? Ngati Ine ndikunena choonadi, nʼchifukwa chiyani simukundikhulupirira?
47 Den, som er af Gud, hører Guds Ord; derfor høre I ikke, fordi I ere ikke af Gud."
Munthu wochokera kwa Mulungu amamva zimene Mulungu amanena. Chifukwa chimene simumvera nʼchakuti, inuyo sindinu ochokera kwa Mulungu.”
48 Jøderne svarede og sagde til ham: "Sige vi ikke med Rette, at du er en Samaritan og er besat?"
Ayuda anamuyankha Iye kuti, “Kodi ife sitikulondola ponena kuti Inu ndi Msamariya ndi wogwidwa ndi chiwanda?”
49 Jesus svarede: "Jeg er ikke besat, men jeg ærer min Fader, og I vanære mig.
Yesu anati, “Ine sindinagwidwe ndi chiwanda, koma ndimalemekeza Atate anga, koma inu mukundinyoza.
50 Men jeg søger ikke min Ære; der er den, som søger den og dømmer.
Ine sindidzifunira ndekha ulemu; koma alipo wina amene amandifunira, ndipo Iyeyo ndiye woweruza.
51 Sandelig, sandelig, siger jeg eder, dersom nogen holder mit Ord, skal han i al Evighed ikke se Døden." (aiōn g165)
Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.” (aiōn g165)
52 Jøderne sagde til ham: "Nu vide vi, at du et besat; Abraham døde og Profeterne, og du siger: Dersom nogen holder mit Ord, han skal i al Evighed ikke smage Døden. (aiōn g165)
Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ (aiōn g165)
53 Mon du er større end vor Fader Abraham, som jo døde? også Profeterne døde; hvem gør du dig selv til?"
Kodi ndinu wa mkulu kuposa abambo athu Abrahamu? Iye anafa, ndiponso aneneri onse. Inu mukuganiza kuti ndinu yani?”
54 Jesus svarede: "Dersom jeg ærer mig selv, er min Ære intet; det er min Fader, som ærer mig, han, om hvem I sige, at han er eders Gud.
Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndidzilemekeza ndekha, ulemu wangawo ndi wosatanthauza kanthu. Atate anga amene inu mukuti ndi Mulungu wanu, ndiye amene amandilemekeza Ine.
55 Og I have ikke kendt ham, men jeg kender ham. Og dersom jeg siger: "Jeg kender ham ikke," da bliver jeg en Løgner ligesom I; men jeg kender ham og holder hans Ord.
Ngakhale kuti inuyo simukumudziwa, Ineyo ndikumudziwa. Ngati Ine nditanena kuti sindikumudziwa, Ineyo nditha kukhala wabodza ngati inuyo, koma Ine ndimamudziwa ndipo ndimasunga mawu ake.
56 Abraham, eders Fader, frydede sig til at se min Dag, og han så den og glædede sig."
Abambo anu Abrahamu anakondwera poyembekezera kubwera kwanga. Iwo anandiona ndipo anasangalala.”
57 Da sagde Jøderne til ham: "Du er endnu ikke halvtredsindstyve År gammel, og du har set Abraham?"
Ayuda anati kwa Iye, “Inu sumunafike nʼkomwe zaka makumi asanu, ndipo mukuti munamuona Abrahamu!”
58 Jesus sagde til dem: "Sandelig, sandelig, siger jeg eder, førend Abraham blev til, har jeg været."
Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani choonadi, Abrahamu asanabadwe, Ine Ndine!”
59 Så toge de Sten for at kaste på ham; men Jesus skjulte sig og gik ud af Helligdommen.
Pamenepo iwo anatola miyala kuti amugende, koma Yesu anabisala, nachoka mozemba mʼNyumba ya Mulungu.

< Johannes 8 >