< Job 7 >

1 Har Mennesket på Jord ej Krigerkår? Som en Daglejers er hans Dage.
“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
2 Som Trællen, der higer efter Skygge som Daglejeren, der venter på Løn,
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
3 så fik jeg Skuffelses Måneder i Arv kvalfulde Nætter til Del.
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
4 Når jeg lægger mig, siger jeg: "Hvornår er det Dag, af jeg kan stå op?" og når jeg står op: "Hvornår er det Kvæld?" Jeg mættes af Uro, til Dagen gryr.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
5 Mit Legeme er klædt med Orme og Skorpe, min Hud skrumper ind og væsker.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
6 Raskere end Skyttelen flyver mine Dage, de svinder bort uden Håb.
“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
7 Kom i Hu, at mit Liv er et Pust, ej mer får mit Øje Lykke at skue!
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
8 Vennens Øje skal ikke se mig, dit Øje søger mig - jeg er ikke mere.
Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
9 Som Skyen svinder og trækker bort, bliver den, der synker i Døden, borte, (Sheol h7585)
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol h7585)
10 han vender ej atter hjem til sit Hus, hans Sted får ham aldrig at se igen.
Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
11 Så vil jeg da ej lægge Bånd på min Mund, men tale i Åndens Kvide, sukke i bitter Sjælenød.
“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Er jeg et Hav, eller er jeg en Drage, siden du sætter Vagt ved mig?
Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
13 Når jeg tænker, mit Leje skal lindre mig, Sengen lette mit Suk,
Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 da ængster du mig med Drømme, skræmmer mig op ved Syner,
ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 så min Sjæl vil hellere kvæles. hellere dø end lide.
kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 Nu nok! Jeg lever ej evigt, slip mig, mit Liv er et Pust!
Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
17 Hvad er et Menneske, at du regner ham og lægger Mærke til ham,
“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
18 hjemsøger ham hver Morgen, ransager ham hvert Øjeblik?
kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 Når vender du dog dit Øje fra mig, slipper mig, til jeg har sunket mit Spyt?
Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 Har jeg syndet, hvad skader det dig, du, som er Menneskets Vogter? Hvi gjorde du mig til Skive, hvorfor blev jeg dig til Byrde?
Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 Hvorfor tilgiver du ikke min Synd og lader min Brøde uænset? Snart ligger jeg jo under Mulde, du søger mig - og jeg er ikke mere!
Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

< Job 7 >