< Job 32 >

1 Da nu hine tre Mænd ikke mere svarede Job, fordi han var retfærdig i sine egne Øjne,
Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama.
2 blussede Vreden op i Buziten Elihu, Barak'els Søn, af Rams Slægt. På Job vrededes han, fordi han gjorde sig retfærdigere end Gud,
Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga.
3 og på hans tre Venner, fordi de ikke fandt noget Svar og dog dømte Job skyldig.
Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa.
4 Elihu havde ventet, så længe de talte med Job, fordi de var ældre end han;
Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo.
5 men da han så, at de tre Mænd intet havde at svare, blussede hans Vrede op;
Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.
6 og Buziten Elihu, Barak'els Søn, tog til Orde og sagde: Ung af Dage er jeg, og I er gamle Mænd, derfor holdt jeg mig tilbage, angst for at meddele eder min Viden;
Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati: “Ine ndine wamngʼono, inuyo ndinu akuluakulu, nʼchifukwa chake ndimaopa, ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
7 jeg tænkte: "Lad Alderen tale og Årenes Mængde kundgøre Visdom!"
Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula; anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
8 Dog Ånden, den er i Mennesket, og den Almægtiges Ånde giver dem Indsigt;
Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu, mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
9 de gamle er ikke altid de kloge, Oldinge ved ej altid, hvad Ret er;
Si okalamba amene ali ndi nzeru, si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.
10 derfor siger jeg: Hør mig, lad også mig komme frem med min Viden!
“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni; inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
11 Jeg biede på, at I skulde tale, lyttede efter forstandige Ord, at I skulde finde de rette Ord;
Ndadikira nthawi yonseyi, ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula, pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
12 jeg agtede nøje på eder; men ingen af eder gendrev Job og gav Svar på hans Ord.
ineyo ndinakumvetseranidi. Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu; palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
13 Sig nu ikke: "Vi stødte på Visdom, Gud må fælde ham, ikke et Menneske!"
Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru; Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
14 Mod mig har han ikke rettet sin Tale, og med eders Ord vil jeg ikke svare ham.
Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine, ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.
15 De blev bange, svarer ej mer, for dem slap Ordene op.
“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso; mawu awathera.
16 Skal jeg tøve, fordi de tier og står der uden at svare et Ord?
Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano, pakuti angoyima phee wopanda yankho?
17 Også jeg vil svare min Del, også jeg vil frem med min Viden!
Inenso ndiyankhulapo tsopano; nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
18 Thi jeg er fuld af Ord, Ånden i mit Bryst trænger på;
Pakuti ndili nawo mawu ambiri, ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
19 som tilbundet Vin er mit Bryst, som nyfyldte Vinsække nær ved at sprænges;
mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo, ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
20 tale vil jeg for at få Luft, åbne mine Læber og svare.
Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike; ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
21 Forskel gør jeg ikke og smigrer ikke for nogen;
Sindidzakondera munthu wina aliyense, kapena kuyankhula zoshashalika,
22 thi at smigre bruger jeg ikke, snart rev min Skaber mig ellers bort!
pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika, Mlengi wanga akanandilanga msanga.”

< Job 32 >