< Job 28 >

1 Sølvet har jo sit Leje, som renses, sit sted
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
2 Jern hentes op af Jorden, og Sten smeltes om til Kobber.
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
3 På Mørket gør man en Ende og ransager indtil de dybeste Kroge Mørkets og Mulmets Sten;
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
4 man bryder en Skakt under Foden, og glemte, foruden Fodfæste, hænger de svævende fjernt fra Mennesker.
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
5 Af Jorden fremvokser Brød, imedens dens Indre omvæltes som af Ild;
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
6 i Stenen der sidder Safiren, og der er Guldstøv i den.
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
7 Stien derhen er Rovfuglen ukendt, Falkens Øje udspejder den ikke;
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
8 den trædes ikke af stolte Vilddyr, Løven skrider ej frem ad den.
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
9 På Flinten lægger man Hånd og omvælter Bjerge fra Roden;
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
10 i Klipperne hugger man Gange, alskens Klenodier skuer Øjet;
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
11 man tilstopper Strømmenes Kilder og bringer det skjulte for Lyset.
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
12 Men Visdommen - hvor mon den findes, og hvor er Indsigtens Sted?
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
13 Mennesket kender ikke dens Vej, den findes ej i de levendes Land;
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
14 Dybet siger: "I mig er den ikke!" Havet: "Ej heller hos mig!"
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
15 Man får den ej for det fineste Guld, for Sølv kan den ikke købes,
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
16 den opvejes ikke med Ofirguld, med kostelig Sjoham eller Safir;
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
17 Guld og Glar kan ej måle sig med den, den fås ej i Bytte for gyldne Kar,
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
18 Krystal og Koraller ikke at nævne. At eje Visdom er mere end Perler,
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
19 Ætiopiens Topas kan ej måle sig med den, den opvejes ej med det rene Guld.
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
20 Men Visdommen - hvor mon den kommer fra, og hvor er Indsigtens Sted?
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
21 Den er dulgt for alt levendes Øje og skjult for Himmelens Fugle;
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
22 Afgrund og Død må sige: "Vi hørte kun tale derom."
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
23 Gud er kendt med dens Vej, han ved, hvor den har sit Sted;
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
24 thi han skuer til Jordens Ender, alt under Himmelen ser han.
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
25 Dengang han fastsatte Vindens Vægt og målte Vandet med Mål,
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
26 da han satte en Lov for Regnen, afmærked Tordenskyen dens Vej,
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
27 da skued og mønstred han den, han stilled den op og ransaged den.
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
28 Men til Mennesket sagde han: "Se, HERRENs Frygt, det er Visdom, at sky det onde er Indsigt."
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”

< Job 28 >