< Job 20 >

1 Så tog Na'amatiten Zofar til Orde og sagde
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 "Derfor bruser Tankerne i mig, og derfor stormer det i mig;
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 til min Skam må jeg høre på Tugt, får tankeløst Mundsvejr til Svar!
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 Ved du da ikke fra Arilds Tid, fra Tiden, da Mennesket sattes på Jorden,
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 at gudløses Jubel er kort og vanhelliges Glæde stakket?
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 Steg end hans Hovmod til Himlen, raged hans Hoved i Sky,
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 som sit Skarn forgår han for evigt, de, der så ham, siger: "Hvor er han?"
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 Han flyr som en Drøm, man finder ham ikke, som et Nattesyn jages han bort;
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 Øjet, der så ham, ser ham ej mer, hans Sted får ham aldrig at se igen.
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 Hans Sønner bejler til ringes Yndest, hans Hænder må give hans Gods tilbage.
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 Hans Ben var fulde af Ungdomskraft, men den lægger sig med ham i Støvet.
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 Er det onde end sødt i hans Mund, når han gemmer det under sin Tunge,
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 sparer på det og slipper det ikke, holder det fast til sin Gane,
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 så bliver dog Maden i hans Indre til Slangegift inden i ham;
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 Godset, han slugte, må han spy ud, Gud driver det ud af hans Bug,
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 han indsuger Slangernes Gift, og Øgleungen slår ham ihjel;
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 han skuer ej Strømme af Olie, Bække af Honning og Fløde;
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 han må af med sin Vinding, svælger den ej, får ingen Glæde af tilbyttet Gods.
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 Thi han knuste de ringe og lod dem ligge, ranede Huse, han ej havde bygget.
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 Thi han har ingen Hjælp af sin Rigdom, trods sine Skatte reddes han ikke;
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 ingen gik fri for hans Glubskhed, derfor varer hans Lykke ikke;
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 midt i sin Overflod har han det trangt, al Slags Nød kommer over ham.
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 For at fylde hans Bug sender Gud sin Vredes Glød imod ham, lader sin Harme regne på ham.
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 Flyr han for Brynje af Jern, så gennemborer ham Kobberbuen;
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 en Kni kommer ud af hans Ryg, et lynende Stål af hans Galde; over ham falder Rædsler,
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 idel Mørke er opsparet til ham; Ild, der ej blæses op, fortærer ham, æder Levningen i hans Telt.
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 Himlen bringer hans Brøde for Lyset, og Jorden rejser sig mod ham.
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 Hans Huses Vinding må bort, rives bort på Guds Vredes Dag.
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 Slig er den gudløses Lod fra Gud og Lønnen fra Gud for hans Brøde!
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

< Job 20 >