< Job 18 >

1 Så tog Sjuhiten Bildad til Orde og sagde:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 "Så gør dog en Ende på dine Ord, kom til Fornuft og lad os tale!
“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
3 Hvi skal vi regnes for Kvæg og stå som umælende i dine Øjne?
Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
4 Du, som i Vrede sønderslider din Sjæl, skal for din Skyld Jorden blive øde og Klippen flyttes fra sit Sted?
Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
5 Nej, den gudløses Lys bliver slukt, hans Ildslue giver ej Lys;
“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
6 Lyset i hans Telt går ud, og hans Lampe slukkes for ham;
Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
7 hans kraftige Skridt bliver korte, han falder for eget Råd;
Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
8 thi hans Fod drives ind i Nettet, på Fletværk vandrer han frem,
Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
9 Fælden griber om Hælen, Garnet holder ham fast;
Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 Snaren er skjult i Jorden for ham og Saksen på hans Sti;
Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
11 Rædsler skræmmer ham alle Vegne og kyser ham Skridt for Skridt:
Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 Ulykken hungrer efter ham, Undergang lurer på hans Fald:
Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
13 Dødens førstefødte æder hans Lemmer, æder hans Legemes Lemmer;
Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 han rives bort fra sit Telt, sin Fortrøstning; den styrer hans Skridt til Rædslernes Konge;
Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 i hans Telt har Undergang hjemme, Svovl strøs ud på hans Bolig;
Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 nedentil tørrer hans Rødder, oventil visner hans Grene;
Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
17 hans Minde svinder fra Jord, på Gaden nævnes ikke hans Navn;
Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 man støder ham ud fra Lys i Mørket og driver ham bort fra Jorderig;
Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 i sit Folk har han ikke Afkom og Æt, i hans Hjem er der ingen tilbage;
Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 de i Vester stivner ved hans Skæbnedag, de i Øst bliver slagne af Rædsel.
Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Ja, således går det den lovløses Bolig, dens Hjem, der ej kender Gud!
Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

< Job 18 >