< Jeremias 52 >
1 Zedekias var enogtyve år gammel da han blev konge, og han herskede elleve År i Jerusalem. Hans Moder hed Hamital og var en Datter af Jirmeja fra Libna.
Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
2 Han gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne, ganske som Jojakim.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
3 Thi for HERRENs Vredes Skyld kom dette over Jerusalem og Juda, og til sidst stødte han dem bort fra sit Åsyn. Og Zedekias faldt fra Babels konge.
Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
4 I hans niende Regeringsår på den tiende Dag i den tiende Måned drog Kong Nebukadrezar af Babel da med hele sin Hær mod Jerusalem, og de belejrede det og byggede Belejringstårne imod det rundt omkring;
Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
5 og Belejringen varede til Kong Zedekiass ellevte Regeringsår.
Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
6 På den niende Dag i den fjerde Måned blev Hungersnøden hård i Byen, og Folket fra Landet havde ikke Brød. Da blev Byens Mur gennembrudt.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
7 Alle krigsfolkene flygtede om Natten ud af Byen gennem Porten mellem de to Mure ved Kongens Have, medens Kaldæerne holdt Byen omringet, og de tog Vejen ad Arabalavningen til.
Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
8 Men Kaldæernes Hær satte efter Kongen og indhentede ham på Jerikosletten, efter at hele hans Hær var blevet splittet til alle Sider.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
9 Så greb de Kongen og bragte ham op til Ribla i Hamats Land til Babels Konge, der fældede Dommen over ham.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
10 Hans Sønner lod han henrette i hans Påsyn, ligeledes lod han alle Judas Øverster henrette i Ribla;
Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
11 og på Zedekias selv lod Babels Konge Øjnene stikke ud; derpå lod han ham lægge i Kobberlænker, og således førte han ham til Babel; og han lod ham kaste i Fængsel, hvor han blev til sin Dødedag.
Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
12 På den tiende Dag i den femte Måned, det var Babels Konge Nebukadrezars nittende Regeringsår, kom Nebuzaradan, Øversten for Livvagten, Babels konges Tjener, til Jerusalem.
Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
13 Han satte Ild på HERRENs Hus og Kongens Palads og alle Husene i Jerusalem; på alle Stormændenes Huse satte han Ild;
Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
14 og Murene om Jerusalem nedbrød hele kaldæernes Hær, som Øversten for Livvagten havde med sig.
Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
15 De sidste Folk, som var tilbage i Byen, og Overløberne, der var gået over til Babels Konge, og de sidste Håndværkere førte Nebuzaradan, Øversten for Livvagten, bort.
Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
16 Men nogle af de fattigste af Folket fra Landet lod Nebuzaradan, Øversten for Livvagten, blive tilbage som Vingårdsmænd og Agerdyrkere,
Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
17 Kobbersøjlerne i HERRENs Hus, Stellene og Kobberhavet i HERRENs Hus slog Kaldæerne i Stykker og førte Kobberet til Babel.
Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
18 Karrene, Skovlene, knivene og Kanderne og alle Kobbersagerne, som brugtes ved Tjenesten, røvede de;
Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
19 også Fadene, Panderne, Skålene, Karrene, Lysestagerne, Kanderne og Offerskålene, der helt var af Guld eller Sølv, røvede Øversten for Livvagten.
Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
20 De to Søjler, Havet med de tolv Kobberokser under og Stellene, som Salomo havde ladet lave til HERRENs Hus Kobberet i alle disse Ting var ikke til at veje.
Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
21 Atten Alen høj var hver Søjle, og en Snor på tolv Alen kunde nå om den, og den var hul, og Kobberet var fire Fingre tykt.
Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
22 Og der var et Søjlehoved af Kobber oven på den, fem Alen højt, og rundt om Søjlehovedet var der Fletværk og Granatæbler, alt af Kobber; og på samme Måde var det med den anden Søjle.
Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
23 Og der var seks og halvfemsindstyve Granatæbler, som hang frit; der var i alt hundrede Granatæbler rundt om Fletværket.
Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
24 Øversten for Livvagten tog Ypperstepræsten Seraja, Anden præsten Zefanja og de tre Dørvogtere;
Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
25 og fra Byen tog han en Hofmand, der havde Opsyn med krigsfolket, og syv Mænd, der hørte til Kongens nærmeste Omgivelser, og som endnu fandtes i Byen, desuden Hærførerens Skriver, der udskrev Folket fra Landet til Krigstjeneste, og dertil tresindstyve Mænd at Folket fra Landet, der fandtes i Byen
Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
26 dem tog Øversten for Livvagten Nebuzaradan og førte til Babels Konge i Ribla
Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
27 og Babels Konge lod dem dræbe i Ribla i Hamats Land. Så førtes Juda i Landflygtighed fra sit Land.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
28 Følgende er Tallet på de Folk, Nebukadrezar bortførte i Fangenskab: I hans syvende År 3023 Judæere,
Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
29 i Nebukadrezars attende År 832 fra Jerusalem;
mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
30 i Nebukadrezars tre og tyvende År bortførte Nebuzaradan, Øversten for Livvagten, 745 af Judæerne; tilsammen 4600.
mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
31 I det syv og tredivte År efter Kong Jojakin af Judas Bortførelse på den fem og tyvende Dag i den tolvte Måned tog Babels Konge Evil-Merodak, der i det År kom på Tronen, Kong Jojakin af Juda til Nåde og førte ham ud af Fængselet.
Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
32 Han talte ham venligt til og gav ham Sæde oven for de Konger, som var hos ham i Babel.
Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
33 Jojakin aflagde sin Fangedragt og spiste daglig hos ham, så længe han levede.
Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
34 Han fik sit daglige Underhold af Babels Konge, hver Dag hvad han behøvede for den Dag, indtil sin Dødedag, så længe han levede.
Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.