< Jeremias 34 >
1 Det Ord, som kom til Jeremias fra Herren, da kong Nebukadnezar af Babel og hele hans Hær og alle Riger på Jorden, der stod under hans Herredømme, og alle Folkeslag angreb Jerusalem og alle dets Byer; det lød:
Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi gulu lake lonse lankhondo, pamodzi ndi maufumu onse a pa dziko lapansi amene ankawalamulira ndiponso anthu a mitundu yonse ankathira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda yonse yozungulira Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Så siger HERREN, Israels Gud: Gå hen og sig til Kong Zedekias af Juda: Så siger HERREN: Se, jeg giver denne By i Babels Konges Hånd, og han skal afbrænde den.
“Yehova, Mulungu wa Israeli akuti: Pita kwa Zedekiya mfumu ya Yuda ndipo ukamuwuze kuti Yehova akuti mzinda uno ndidzawupereka mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni ndipo adzawutentha ndi moto.
3 Og du skal ikke undslippe hans Hånd, men gribes og overgives i hans Hånd og se Babels Konge Øje til Øje, og han skal tale med dig Mund til Mund, og du skal komme til Babel.
Iweyo sudzapulumuka mʼmanja mwake koma udzagwidwa ndithu ndipo adzakupereka mʼmanja mwake. Udzayiona mfumu ya ku Babuloni maso ndi maso ako ndipo udzayankhula nayo pakamwa ndi pakamwa. Ndipo udzapita ku Babuloni.
4 Hør dog HERRENs Ord, Kong Zedekias af Juda: Så siger HERREN om dig: Du skal ikke falde for Sværdet,
“Koma iwe Zedekiya mfumu ya Yuda, imva lonjezo ili la Yehova. Izi ndi zimene Yehova akunena za iwe: Sudzaphedwa pa nkhondo;
5 men dø i Fred, og ligesom man brændte til Ære for dine Fædre, kongerne før dig, således skal man brænde til Ære for dig og klage over dig: "Ve, Herre!" så sandt jeg har talet, lyder det fra HERREN.
udzafera pa mtendere. Monga anthu ankafukiza lubani poyika maliro a makolo ako akale, amene anali mafumu iwe usanalowe ufumu, choncho nawenso podzayika maliro ako adzafukiza lubani ndipo polira azidzati, ‘Kalanga, mbuye wanga!’ Ine mwini ndalonjeza zimenezi, akutero Yehova.”
6 Og Profeten Jeremias talte alle disse Ord til kong Zedekias af Juda i Jerusalem,
Ndipo mneneri Yeremiya anawuza zonsezi Zedekiya mfumu ya Yuda, mu Yerusalemu.
7 medens Babels Konges Hær angreb Jerusalem og begge de Byer i Juda, der var tilbage, Lakisj og Azeka; thi disse faste Stæder var tilbage af Judas Byer.
Nthawi imeneyi nʼkuti gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni likuthira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda ina yotsala ya Yuda, Lakisi ndi Azeka. Imeneyi yokha ndiye inali mizinda yotetezedwa yotsala ya ku Yuda.
8 Det Ord, som kom til Jeremias fra HERREN, efter at kong Zedekias havde sluttet en Pagt med alt Folket i Jerusalem og udråbt Frigivelse,
Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya. Nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Zedekiya atachita pangano ndi anthu onse a mu Yerusalemu kuti alengeze zakuti akapolo awo adzawamasule.
9 således at enhver skulde lade sin Træl og Trælkvinde gå bort i Frihed, såfremt de var Hebræere, og ikke mere lade en judæisk Broder trælle.
Aliyense amene anali ndi akapolo a Chihebri, aamuna kapena aakazi awamasule; palibe amene ayenera kusunga mu ukapolo Myuda mnzake.
10 Og alle Fyrsterne og alt Folket, som havde indgået Pagten om, at enhver skulde lade sin Træl og Trælkvinde gå bort i Frihed og ikke mere lade dem trælle, adlød; de adlød og lod dem gå.
Choncho akuluakulu pamodzi ndi anthu onse amene anachita pangano ili anagwirizana kuti amasule akapolo awo aamuna ndi aakazi ndi kuti asawasungenso mu ukapolo. Iwo anachitadi zimenezi ndipo anawamasuladi.
11 Men siden skiftede de Sind og tog Trællene og Trælkvinderne, som de havde ladet gå bort i Frihed, tilbage og tvang dem til at være Trælle og Trælkvinder.
Koma pambuyo pake anasintha maganizo awo ndi kuwatenganso amuna ndi akazi amene anawamasula aja ndipo anawasandutsanso akapolo.
12 Da kom HERRENs Ord til Jeremias således:
Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti:
13 Så siger HERREN, Israels Gud: Jeg sluttede en Pagt med eders Fædre, dengang jeg førte dem ud af Ægypten, af Trællehuset, idet jeg sagde:
“Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Ine ndinachita pangano ndi makolo anu pamene ndinawatulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo. Ine ndinati,
14 "Når der er gået syv År, skal enhver af eder lade sin hebraiske Landsmand, som har solgt sig til dig og tjent dig i seks År, gå bort; du skal lade ham gå af din Tjeneste i Frihed!" Men eders Fædre hørte mig ikke og lånte mig ikke Øre.
‘Chaka chachisanu ndi chiwiri chilichonse aliyense wa inu ayenera kumasula mʼbale wake wa Chihebri amene anadzigulitsa yekha kwa inuyo. Iyeyo amasulidwe akagwira ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, mumulole apite mwaufulu.’ Komatu makolo anu sanandimvere kapena kusamala konse.
15 Nys omvendte I eder og gjorde, hvad der er ret i mine Øjne, idet I udråbte Frigivelse, hver for sin Broder, og I sluttede en Pagt for mit Åsyn i det Hus, mit Navn er nævnet over,
Posachedwa pomwepa inu munalapa ndi kuchita zinthu zabwino pamaso panga: Aliyense wa inu anamasula mʼbale wake. Ndipo munachita pangano pamaso panga mʼNyumba imene imadziwika ndi dzina langa kuti mudzachitadi zimenezi.
16 men siden skiftede I Sind og vanhelligede mit Navn, idet enhver af eder tog sin Træl eller Trælkvinde tilbage, som I havde ladet gå bort i Frihed, om de ønskede det, og tvang dem til at være eders Trælle og Trælkvinder.
Koma tsopano mwasintha maganizo anu ndipo mwayipitsa dzina langa. Mwatenganso ukapolo aamuna ndi aakazi amene munawamasula aja kuti apite kumene akufuna. Mwawakakamiza kuti akhalebe akapolo anu.
17 Derfor, så siger HERREN: Da I ikke hørte mig og udråbte Frigivelse, hver for sin Broder og hver for sin Næste, vil jeg nu udråbe Frigivelse for eder, lyder det fra HERREN, så I hjemfalder til Sværd, Pest og Hunger, og jeg vil gøre eder til Rædsel for alle Jordens Riger.
“Nʼchifukwa chake Yehova akuti: Inu simunandimvere Ine; simunalengeze kuti abale anu amasulidwe. Chabwino! Ine ndidzakupatsani ufulu; ufulu wake ukhala wophedwa ndi nkhondo, mliri ndi njala. Ndidzakusandutsani chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
18 Og jeg giver de Mænd, som har overtrådt min Pagt og ikke holdt den Pagts Ord, som de sluttede for mit Åsyn, da de slagtede Kalven og skar den i to Stykker, mellem hvilke de gik,
Inu simunasunge pangano limene munachita ndi Ine. Simunasamale lonjezo limene munachita pamaso panga. Choncho ndidzakusandutsani ngati mwana wangʼombe uja amene ankamudula pawiri napita pakati pa zigawozo.
19 Judas og Jerusalems Fyrster, Hofmændene og Præsterne og hele Landets Befolkning, som gik mellem Stykkerne af Kalven
Amene ankadutsa pakati pa zigawozo anali atsogoleri a Yuda ndi Yerusalemu, akuluakulu a bwalo, ansembe ndi anthu onse a mʼdzikomo.
20 dem giver jeg i deres Fjenders Hånd og i deres Hånd, som står dem efter Livet, og deres Lig skal blive Himmelens Fugle og Jordens Dyr til Æde.
Onsewa ndidzawapereka kwa adani awo amene akufuna kuwapha. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo za dziko lapansi.
21 Og Kong Zedekias af Juda og hans Fyrster giver jeg i deres Fjenders Hånd og i deres Hånd, som står dem efter Livet. Og Babels Konges Hær, som drog bort fra eder,
“Ndidzapereka Zedekiya mfumu ya Yuda ndi nduna zake kwa adani awo amene akufuna kuwapha, kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni limene nthawi ino layamba kubwerera mʼmbuyo.
22 se, den bydet jeg, lyder det fra HERREN, at vende tilbage til denne By, og de skal angribe den og indfage og afbrænde den; og Judas Byer lægger jeg øde, så ingen bor der!
Taonani, Ine ndidzawalamula, akutero Yehova, ndipo ndidzawabweretsanso ku mzinda uno. Adzathira nkhondo mzindawu, kuwulanda ndi kuwutentha. Ndipo Ine ndidzasandutsa chipululu mizinda ya Yuda kotero kuti palibe amene adzakhalemo.”