< Jeremias 26 >
1 I Joasias's søns, kong Jojakim af Judas, første regeringstid kom dette ord fra HERREN:
Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Så siger HERREN: Stå frem i Forgården til HERRENs Hus og tal til hele Juda, som kommer for at tilbede i HERRENs Hus, alle de Ord, jeg har pålagt dig at tale til dem; udelad ikke et Ord!
“Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
3 Måske hører de og omvender sig, hver fra sin onde Vej, så jeg kan angre det onde, jeg har i Sinde at gøre dem for deres onde Gerningers Skyld.
Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
4 Sig til dem: Så siger HERREN: Hvis I ikke hører mig og følger den Lov, jeg har forelagt eder,
Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
5 så I hører mine Tjenere Profeternes Ord, som jeg årle og silde sendte eder, skønt I ikke vilde høre,
ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
6 så gør jeg med dette Hus som med Silo og giver alle Jordens Folk denne By at forbande ved.
ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
7 Præsterne, Profeterne og alt Folket hørte nu Jeremias tale disse Ord i HERRENs Hus;
Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
8 og da Jeremias havde sagt alt, hvad HERREN havde pålagt ham at sige til alt Folket, greb Præsterne og Profeterne og alt Folket ham og sagde: "Du skal dø!
Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
9 Hvor tør du profetere i HERRENs Navn og sige: Det skal gå dette Hus som Silo, og denne By skal ødelægges, så ingen bor der!" Og alt Folket stimlede sammen om Jeremias i HERRENs Hus.
Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
10 Da Judas Fyrster hørte det, gik de fra Kongens Palads op til HERRENs Hus og tog Sæde ved Indgangen til HERRENs nye Port.
Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
11 Så sagde Præsterne og Profeterne til Fyrsterne og alt Folket: "Denne Mand har gjort halsløs Gerning, thi han har profeteret mod denne By, som I selv hørte."
Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
12 Men Jeremias sagde til Fyrsterne og alt Folket: "HERREN sendte mig for at profetere mod dette Hus og denne By alle de Ord, I hørte.
Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
13 Bedrer dog eders Veje og eders Gerninger og hør på HERREN eders Guds Røst, at HERREN må angre det onde, han har talet imod eder.
Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
14 Men se, jeg er i eders Hånd; gør med mig, hvad der er godt og billigt i eders Øjne!
Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
15 Dog skal I vide, at hvis I dræber mig, så bringer I uskyldigt Blod over eder og denne By og dens Indbyggere; thi sandelig sendte HERREN mig for at tale alle disse ord til eder."
Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
16 Da sagde Fyrsterne og alt Folket til Præsterne og Profeterne: "Denne Mand har ikke gjort halsløs Gerning, men talt til os i HERREN vor Guds Navn."
Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
17 Og nogle af Landets Ældste trådte frem og sagde til hele Folkets Forsamling:
Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
18 "Mika fra Moresjet profeterede på Kong Ezekias af Judas Tid og sagde til alt Judas Folk: Så siger Hærskarers HERRE: Zion skal pløjes som en Mark, Jerusalem blive til Grushobe, Tempelbjerget til Krathøj.
“Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
19 Mon Kong Ezekias af Juda og hele Juda dræbte ham? Frygtede de ikke HERREN og bad ham om Nåde, så HERREN angrede det onde, han havde truet dem med? Vi er ved at bringe stor Ulykke over vore Sjæle."
Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
20 Der var også en anden Mand, som profeterede i HERRENs Navn, Urija, Sjemajas Søn, fra Kirjat Jearim; og han profeterede mod denne By og dette Land med de samme Ord som Jeremias.
(Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
21 Da Kong Jojakim og alle hans Krigsfolk og alle Fyrsterne hørte hans Ord, stod han ham efter Livet; og da Urija hørte det, blev han bange og flygtede og kom til Ægypten.
Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
22 Men Kong Jojakim sendte Folk til Ægypten; han sendte Elnatan, Akbors Søn, og nogle andre til Ægypten,
Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
23 og de bragte Urija hjem fra Ægypten og førte ham til Kong Jojakim, som lod ham hugge ned med Sværdet og hans Lig kaste hen, hvor Småfolk havde deres Grave.
Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
24 Men Ahikam, Sjafans Søn, holdt Hånden over Jeremias, så han ikke blev overgivet i Folkets Hånd og dræbt.
Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.