< Jeremias 21 >

1 Det Ord, som kom til Jeremias fra Herren, da kong Zedekias sendte Pasjhur, Malkias Søn, og Præsten Zefanja, Maasejas Søn, til ham og lod sige:
Mfumu Zedekiya inatuma Pasuri mwana wa Malikiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa Yeremiya.
2 "Rådspørg HERREN for os, thi kong Nebukadrezar af Babel angriber os; måske vil HERREN handle med os efter alle sine Undergerninger, så Nebukadrezar drager bort fra os."
Iwo amati akanene kwa Yeremiya mawu akuti, “Tinenere kwa Yehova chifukwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni akutithira nkhondo. Mwina mwake Yehova nʼkutichitira zodabwitsa kuti Nebukadinezarayo achoke kwathu kuno.”
3 Jeremias svarede dem: "Sig til Zedekias:
Koma Yehova anawuza Yeremiya kuti ayankhe Pasuri ndi Zefaniya kuti, “Kamuwuzeni Zedekiya kuti,
4 Så siger HERREN, Israels Gud: Se, Våbnene i eders Hånd, med hvilke I uden for Muren kæmper mod Babels Konge og Kaldæerne, der belejrer eder, dem driver jeg tilbage og samler dem midt i denne By;
‘Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ndikulandeni zida zimene zili mʼmanja mwanu zimene mukugwiritsa ntchito polimbana ndi mfumu ya ku Babuloni ndi ankhondo ake amene akuzingani kunja kwa lingali. Ndipo ndidzasonkhanitsa zidazo mʼkati mwa mzindawu.
5 og jeg vil selv kæmpe mod eder med utdrakt Hånd og stærk Arm, i Vrede og Harme og stor Fortørnelse;
Ineyo mwini wakene ndi mkono wotambasula ndi dzanja lamphamvu, ndidzachita nanu nkhondo ndili wokwiya, wokalipa ndi waukali.
6 og jeg slår denne Bys Indbyggere, ja både Folk og Fæ, med voldsom Pest, så de dør.
Ndidzakantha amene amakhala mu mzinda muno, anthu pamodzi ndi zirombo, ndipo zidzafa ndi mliri woopsa.
7 Og siden, lyder det fra HERREN, giver jeg Kong Zedekias af Juda og hans Tjenere og Folket, der levnes i denne By af Pesten, Sværdet og Hungeren, i Kong Nebukadrezar af Babels og i deres Fjenders Hånd, og i deres Hånd, som står dem efter Livet; de skal hugge dem ned med Sværdet, og jeg vil ikke ynkes over dem eller vise Skånsel eller Barmhjertighed!"
Pambuyo pake, ndidzapereka Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi anthu a mu mzinda muno amene adzapulumuke pa nthawi ya mliri, lupanga ndi njala kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi kwa adani awo amene ankafuna kuwapha. Iye adzawapha ndi lupanga. Sadzawachitira chifundo kapena kuwamvera chisoni kapenanso kuwakomera mtima.’
8 Og sig til dette Folk: "Så siger HERREN: Se, jeg forelægger eder Livets Vej og Dødens Vej.
“Yehova anati ndiwawuzenso anthu amenewa kuti asankhe pakati pa moyo ndi imfa.
9 Den, som bliver i denne By, skal dø ved Sværd, Hunger og Pest: men den, som går ud og overgiver sig til Kaldæerne, der belejrer eder, skal leve og vinde sit Liv som Bytte,
Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzaphedwa ndi lupanga, njala kapena mliri. Koma aliyense amene apite kukadzipereka kwa Ababuloni amene akuzinganiwa adzakhala ndi moyo, adzapulumuka.
10 Thi jeg retter mit Åsyn mod denne By til Ulykke og ikke til Lykke, lyder det fra HERREN; i Babels Konges Hånd skal den gives, og han skal opbrænde den med Ild."
Ine ndatsimikiza kuchitira mzinda uno choyipa osati chabwino, akutero Yehova. Udzaperekedwa mʼdzanja la mfumu ya ku Babuloni, ndipo iyeyo adzawutentha ndi moto.
11 Og sig til Judas Konges Hus: Hør HERRENs Ord,
“Komanso, uwuze banja laufumu la Yuda kuti, ‘Imva mawu a Yehova;
12 Davids Hus! Så siger HERREN: Hold årle retfærdig Dom, fri den, som er plyndret, af Voldsmandens Hånd, at ikke min Vrede slår ud som Ild og brænder, så ingen kan slukke, for eders onde Gerningers Skyld.
inu a mʼbanja la Davide, Yehova akuti, “‘Weruzani mwachilungamo mmawa uliwonse; pulumutsani mʼdzanja la wozunza aliyense amene walandidwa katundu wake, kuopa kuti ukali wanga ungabuke ndi kuyaka ngati moto wosazimitsika chifukwa cha zoyipa zimene mwachita.
13 Se, jeg kommer over dig, du By i Dalen, du Slettens Klippe, lyder det fra HERREN, I, som siger: "Hvo falder over os, hvo trænger ind i vore Boliger?"
Ndidzalimbana nanu, inu amene mukukhala pamwamba pa chigwa, inu okhala ngati thanthwe lapachidikha, akutero Yehova. Inu amene mumanena kuti, ‘Ndani amene angabwere kudzalimbana nafe? Ndani amene angathe kulowa mʼmalinga mwathu?’
14 Efter eders Gerningers Frugt hjemsøger jeg jer, lyder det fra HERREN; jeg sætter Ild på dens Skov, den fortærer alt deromkring.
Ndidzakulangani molingana ndi ntchito zanu, akutero Yehova. Ndidzatentha nkhalango zanu; moto udzapsereza zonse zimene zakuzungulirani.’”

< Jeremias 21 >