< Esajas 41 >
1 Hør mig i Tavshed, I fjerne Strande, lad Folkene hente ny Kraft, komme hid og tage til Orde, lad os sammen gå frem for Retten!
“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
2 Hvo vakte i Østen ham, hvis Fod går fra Sejr til Sejr, hvo giver Folk i hans Vold og gør ham til Kongers Hersker? Han gør deres Sværd til Støv, deres Buer til flagrende Strå,
“Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
3 forfølger dem, går uskadt frem ad en Vej, hans Fod ej har trådt.
Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
4 Hvo gjorde og virkede det? Han, som længst kaldte Slægterne frem, jeg, HERREN, som er den første og end hos de sidste den samme.
Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
5 Fjerne Strande så det med Gru, den vide Jord følte Rædsel, de nærmede sig og kom.
Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
6 Den ene hjælper den anden og siger: "Broder, fat Mod!"
aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
7 Mesteren opmuntrer Guldsmeden, Glatteren ham, der hamrer; Lodningen tager han god og sømmer det fast, så det står.
Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
8 Men Israel, du min Tjener, Jakob, hvem jeg har udvalgt, - Ætling af Abraham, min Ven -
“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
9 hvem jeg tog fra Jordens Grænser og kaldte fra dens fjerneste Kroge, til hvem jeg sagde: "Du min Tjener, som jeg valgte og ikke vraged":
Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 Frygt ikke, thi jeg er med dig, vær ej rådvild, thi jeg er din Gud! Med min Retfærds højre styrker, ja hjælper, ja støtter jeg dig.
Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
11 Se, Skam og Skændsel får alle, som er dig fjendske, til intet bliver de, der trætter med dig, de forgår.
“Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Du søger, men finder ej dem, der kives med dig, til intet, til Luft bliver de, der strides med dig.
Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
13 Thi jeg, som er HERREN din Gud, jeg griber din Hånd, siger til dig: Frygt kun ikke, jeg er din Hjælper.
Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
14 Frygt ikke, Jakob, du Orm, Israel, du Kryb! Jeg hjælper dig, lyder det fra HERREN, din Genløser er Israels Hellige.
Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 Se, jeg gør dig til Tærskeslæde, en ny med mange Tænder; du skal tærske og knuste Bjerge, og Høje skal du gøre til Avner;
“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 du kaster dem, Vinden tager dem, Stormen hvirvler dem bort. Men du skal juble i HERREN, rose dig af Israels Hellige.
Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
17 Forgæves søger de arme og fattige Vand, deres Tunge brænder af Tørst; jeg, HERREN, vil bønhøre dem, dem svigter ej Israels Gud.
“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Fra nøgne Høje sender jeg Floder og Kilder midt i Dale; Ørkenen gør jeg til Vanddrag, det tørre Land til Væld.
Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19 I Ørkenen giver jeg Cedre, Akacier, Myrter, Oliven; i Ødemark sætter jeg Cypresser tillige med Elm og Gran,
Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20 at de må se og kende, mærke sig det og indse, at HERRENs Hånd har gjort det, Israels Hellige skabt det.
kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
21 Fremlæg eders Sag, siger HERREN, kom med Bevis! siger Jakobs Konge.
“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22 De træde nu frem og forkynde os, hvad der herefter skal ske. Sig frem, hvad I har forudsagt, at vi kan granske derover og se, hvad Udfald det fik; eller kundgør os, hvad der kommer!
Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23 Forkynd, hvad der siden vil ske, at vi kan se, I er Guder! Gør noget, godt eller ondt, så måler vi os med hinanden!
tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24 Se, I er intet, eders Gerning Luft, vederstyggelig, hvo eder vælger.
Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
25 Jeg vakte ham fra Norden, og han kom, jeg kaldte ham fra Solens Opgang. Han nedtramper Fyrster som Dynd, som en Pottemager ælter sit Ler.
“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26 Hvo forkyndte det før, så vi vidste det, forud, så vi sagde: "Han fik Ret!" Nej, ingen har forkyndt eller sagt det, ingen har hørt eders Ord.
Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
27 Først jeg har forkyndt det for Zion, sendt Jerusalem Glædesbud.
Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28 Jeg ser mig om der er ingen, ingen af dem ved Råd, så de svarer mig på mit Spørgsmål.
Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29 Se, alle er de intet, deres Værker Luft, deres Billeder Vind og Tomhed.
Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.