< Esajas 28 >

1 Ve Efraims berusedes stolte og dets herlige Smykkes visnende Blomster på Tindingen af de druknes fede Dal!
Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
2 Se, Herren har en vældig Kæmpe til Rede; som Skybrud af Hagl, som hærgende Storm, som Skybrud af mægtige skyllende Vande slår han til Jorden med Vælde.
Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
3 Med Fødderne trampes de ned, Efraims berusedes stolte Krans
Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
4 og dets herlige Smykkes visnende Blomster på Tindingen af den fede bal; det går den som en tidligmoden Figen før Frugthøst: Hvo der får Øje på den, plukker den, og knap er den i Hånden, før han har slugt den.
Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
5 På hin bag bliver Hærskarers HERRE en smuk Krans og en herlig Krone for sit Folks Rest
Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
6 og en Rettens Ånd for dem, som sidder til Doms, og Styrke for dem, der driver Krigen tilbage til Portene.
Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
7 Også disse raver af Vin, er svimle af Drik, Præst og Profet, de raver af Drik, fra Samling af Vin og svimle af Drik; de raver under Syner, vakler, når de dømmer.
Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
8 Thi alle Borde er fulde af Spy, Uhumskhed flyder på hver en Plet.
Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
9 "Hvem vil han belære, hvem tyder han Syner mon afvante Børn, nys tagne fra Brystet?
Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
10 Kun hakke og rakke, rakke og hakke, lidt i Vejen her og lidt i Vejen der!"
Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
11 Ja, med lallende Læber, med fremmed Mål vil han tale til dette Folk,
Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
12 han, som dog sagde til dem: "Her er der Hvile, lad den trætte hvile, her er der Ro!" men de vilde ej høre.
anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
13 Så bliver for dem da HERRENs Ord: "Hakke og rakke, rakke og bakke, lidt i Vejen her og lidt i Vejen der!" så de går hen og styrter bagover, sønderslås, fanges og hildes.
Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
14 Hør derfor HERRENs Ord, I spotske Mænd, I Nidvisens Mestre blandt dette Jerusalems Folk!
Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
15 Fordi I siger: "Vi slutted en Pagt med Døden, Dødsriget gjorde vi Aftale med; når den susende Svøbe går frem, da når den ej os, thi Løgn har vi gjort til vort Ly, vi har gemt os i Svig;" (Sheol h7585)
Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol h7585)
16 derfor, så siger den Herre HERREN: Se, jeg lægger i Zion en prøvet Sten, en urokkelig, kostelig Hjørnesten; tror man, baster man ikke.
Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
17 Og jeg gør Ret til Målesnor, Retfærd til Blylod; Hagl skal slå Løgnelyet ned, Vand skylle Gemmestedet bort.
Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
18 Eders Pagt med Døden skal brydes, Aftalen med Dødsriget glippe. Når den susende Svøbe går frem, skal den slå jer til Jorden, (Sheol h7585)
Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol h7585)
19 jer skal den ramme, hver Gang den går frem; thi Morgen efter Morgen går den frem, ved Dag og ved Nat, idel Angst skal det blive at få Syner tydet.
Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
20 Vil man strække sig, er Lejet for kort; vil man dække sig, er Tæppet for smalt.
Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
21 Thi som på Perazims Bjerg vil HERREN stå op, som i Gibeons Dal vil han vise sin Vrede for at gøre sin Gerning en underlig Gerning, og øve sit Værk et sælsomt Værk.
Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
22 Derfor hold inde med Spot, at ej eders Bånd skal snære; thi om hele Landets visse Undergang hørte jeg fra Herren, Hærskarers HERRE.
Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
23 Lyt til og hør min Røst, lån Øre og hør mit Ord!
Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
24 Bliver Plovmanden ved med at pløje til Sæd, med at bryde og harve sin Jord?
Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
25 Mon han ikke, når den er jævnet, sår Dild og udstrør Kommen, lægger Hvede, Hirse og Byg på det udsete Sted og Spelt i Kanten deraf?
Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
26 Hans Gud vejleder ham, lærer ham det rette.
Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
27 Thi med Tærskeslæde knuser man ikke Dild, lader ikke Vognhjul gå over Kommen; nej, Dilden tærskes med Stok og Kommen med Kæp.
Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
28 Mon Brødkorn knuses? Nej, det bliver ingen ved med at tærske; Vognhjul og Heste drives derover man knuser det ikke.
Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
29 Også dette kommer fra Hærskarers HERRE, underfuld i Råd og stor i Visdom.
Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.

< Esajas 28 >