< Esajas 12 >

1 På hin Dag skal du sige: Jeg takker dig, HERRE, thi du vrededes på mig; men din Vrede svandt, og du trøstede mig.
Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati: “Ndikukuyamikani, Inu Yehova; chifukwa ngakhale munandipsera mtima, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mwanditonthoza.
2 Se, Gud er min Frelse, jeg er trøstig og uden Frygt; thi HERREN er min Styrke og min Lovsang, og han blev mig til Frelse.
Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga; ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha. Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.”
3 I skal øse Vand med Glæde af Frelsens Kilder
Mudzakondwera popeza Yehova ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4 og sige på hin Dag: Tak HERREN, påkald hans Navn, gør hans Gerninger kendt blandt Folkene, kundgør, at hans Navn er højt!
Tsiku limenelo mudzati: “Yamikani Yehova, tamandani dzina lake; mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5 Lovsyng HERREN, thi stort har han øvet, lad det blive kendt på den vide Jord!
Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu; zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6 Bryd ud i Fryderåb, Zions Beboere, thi stor i eders Midte er Israels Hellige!
Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni; pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”

< Esajas 12 >