< 1 Mosebog 29 >

1 Derpå fortsatte Jakob sin Vandring og drog til Østens Børns Land.
Yakobo anapitiriza ulendo wake kupita ku dziko la anthu a kummawa.
2 Da fik han Øje på en Brønd på Marken og tre Hjorde af Småkvæg, der var lejrede ved den. Ved den Brønd vandede man Hjordene; og over Hullet lå der en stor Sten,
Atafika kumeneko anaona chitsime ku busa ndipo panali magulu atatu a nkhosa zitagona pafupi ndi chitsimecho chifukwa nkhosazo zimamwetsedwa madzi ochokera mʼchitsimecho. Pamwamba pa chitsimecho panali mwala waukulu.
3 som man først væltede bort, når alle Hjordene var samlede, for siden, når Dyrene var vandet, at vælte den på Plads igen.
Amati nkhosa zonse zikasonkhana, abusawo ankagudubuza mwalawo, kuwuchotsa ndi kumwetsa madzi nkhosazo. Kenaka ankawubwezera mwalawo pamalo pake, pakamwa pa chitsimepo.
4 Jakob spurgte dem: "Hvor er I fra, Brødre?" De svarede: "Fra Karan!"
Yakobo anafunsa abusawo kuti, “Abale anga, mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Tachokera ku Harani.”
5 Da spurgte han dem: "Kender I Laban, Nakors Søn?" De svarede: "Ja, ham kender vi godt."
Iye anawafunsanso kuti, “Kodi Labani, mdzukulu wa Nahori mukumudziwa?” Iwo anayankha, “Inde tikumudziwa?”
6 Han spurgte da: "Går det ham vel? De svarede: "Ja, det går ham vel; se, hans Datter Rakel kommer netop med Hjorden derhenne!"
Ndipo Yakobo anawafunsanso, “Kodi ali bwino?” Iwo anati, “Inde ali bwino. Nayu Rakele mwana wake akubwera apoyu ndi nkhosa.”
7 Da sagde han: "Det er jo endnu højlys Dag og for tidligt at drive Kvæget sammen; vand Dyrene og før dem ud på Græsgangene!"
Iye anati, “Taonani, dzuwa likanalipo ndipo nthawi yosonkhanitsa nkhosa sinakwane. Bwanji osazimwetsa madzi nkhosazi.”
8 Men de svarede: "Det kan vi ikke, før alle Hyrderne er samlede; først når de vælter Stenen fra Brøndhullet, kan vi vande Dyrene."
Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”
9 Medens han således stod og talte med dem, var Rakel kommet derhen med sin Faders Hjord, som hun vogtede;
Ali chiyankhulire nawo, Rakele anafika ndi nkhosa za abambo ake popeza ndiye amene ankaweta nkhosazo.
10 og så snart Jakob så sin Morbroder Labans Datter Rakel og hans Hjord, gik han hen og væltede Stenen fra Brøndhullet og vandede sin Morbroder Labans Hjord.
Yakobo ataona Rakele mwana wa Labani, mlongo wa amayi ake, ali ndi nkhosa za Labani, anapita nawugudubuza mwala uja nazimwetsa madzi nkhosa za amalume akezo.
11 Så kyssede han Rakel og brast i Gråd;
Kenaka Yakobo anapsompsona Rakele nayamba kulira mokweza.
12 og han fortalte hende; at han var hendes Faders Frænde, en Søn af Rebekka: Da skyndte hun sig hjem til sin Fader og fortalte ham det"
Kenaka Yakobo anawuza Rakele kuti iye ndi mwana wa Rebeka, mlongo wa abambo a Rakele uja. Choncho Rakele anathamanga nakawuza abambo ake.
13 og så snart Laban hørte om sin Søstersøn Jakob, løb han ham i Møde, omfavnede og kyssede ham og førte ham hjem til sit Hus. Så fortalte Jakob ham alt, hvad der var sket;
Labani atamva za Yakobo, mwana wa mlongo wake, anafulumira kukakumana naye. Anamukupatira napsompsona, napita naye ku nyumba kwake. Yakobo anafotokozera Labani zonse zinachitika.
14 og Laban sagde: "Ja, du er mit Kød og Blod!" Han blev nu hos ham en Månedstid.
Ndipo, Labani anati kwa iye, “Iwe ndiwe ndithu fupa ndi mnofu wanga.” Yakobo anakhala ndi Labani mwezi umodzi.
15 Så sagde Laban til Jakob: "Skulde du tjene mig for intet fordi du er min Frænde? Sig mig. hvad du vil have i Løn!"
Tsono Labani anawuza Yakobo kuti, “Zoona iwe ndi ife ndi abale. Koma suyenera kundigwirira ntchito popanda malipiro. Ndiwuze kuti malipiro ako azikhala wotani?”
16 Nu havde Laban to Døtre; den ældste hed Lea, den yngste Rakel;
Tsono Labani anali ndi ana aakazi awiri; dzina la wamkulu linali Leya, ndipo dzina la wamngʼono linali Rakele.
17 Leas Øjne var matte, men Rakel havde en dejlig Skikkelse og så dejlig ud,
Leya anali ndi maonekedwe wofowoka koma Rakele anali wa maonekedwe wokongola kwambiri.
18 og Jakob elskede Rakel; derfor sagde han: "Jeg vil tjene dig syv År for din yngste Datter Rakel."
Yakobo anakonda Rakele ndipo anati, “Ndidzakugwirirani ntchito kwa zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha mwana wanu wamngʼono, Rakele.”
19 Laban svarede: "Jeg giver hende hellere til dig end til en fremmed; bliv kun hos mig!"
Labani anati, “Kuli bwino kuti ndimupereke kwa iwe ameneyu kusiyana ndi munthu wina. Khala ndi ine kuno.”
20 Så tjente Jakob syv År for Rakel; og de syntes ham kun nogle få Dage, fordi han elskede hende.
Choncho Yakobo anagwira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele. Koma kwa iye zaka zonsezi zinakhala ngati masiku wochepa chifukwa anamukonda Rakele.
21 Derefter sagde Jakob til Laban: "Giv mig min Hustru, nu min Tjenestetid er ude, at jeg kan gå ind til hende!"
Kenaka Yakobo anati kwa Labani, “Nthawi yanga ndakwanitsa, ndipatseni mwana wanu kuti ndimukwatire.”
22 Så indbød Laban alle Mændene på Stedet til Gæstebud.
Pamenepo Labani anakonza phwando la ukwati, nayitana anthu onse a pamalopo.
23 Men da Aftenen kom, tog han sin, Datter Lea og bragte hende til ham, og han gik ind til hende.
Koma pokwana usiku, Labani anatenga mwana wake wamkazi Leya namupatsa Yakobo, ndipo Yakobo anagona naye.
24 Og Laban gav sin Datter Lea sin Trælkvinde Zilpa til Trælkvinde.
Ndipo Labani anapereka wantchito wake wamkazi Zilipa kwa Leya kuti akhale wantchito wake.
25 Da det nu om Morgenen viste sig at være Lea, sagde Jakob til Laban: "Hvad er det, du har gjort imod mig? Er det ikke for Rakel, jeg, har tjent hos dig? Hvorfor har, du bedraget mig?"
Pakucha mmawa, Yakobo anaona kuti anagona ndi Leya. Choncho Yakobo anafunsa Labani, “Nʼchiyani mwandichitirachi? Kodi ine sindinakugwirireni ntchito chifukwa cha Rakele? Bwanji mwandinyenga?”
26 Laban svarede: "Det er ikke Skik og Brug her til Lands at give den yngste bort før den ældste;
Labani anayankha, “Si mwambo wathu kuno kupereka wamngʼono ku banja, wamkulu asanakwatiwe.
27 men lad nu Bryllupsugen gå til Ende, så vil, jeg også give dig hende, imod at du bliver i min Tjeneste syv År til."
Yamba watsiriza sabata ya chikondwerero cha ukwati wa Leya; kenaka ndidzakupatsanso Rakele. Koma udzayenera kundigwirira ntchito zaka zisanu ndi ziwiri.”
28 Det gik Jakob ind på, og da Bryllupsugen var til Ende, gav Laban ham sin Datter Rakel til Hustru.
Yakobo anachitadi momwemo. Anamaliza sabata ya chikondwerero cha Leya, ndipo Labani anamupatsa Rakele kuti akhale mkazi wake.
29 Og Laban gav sin Datter Rakel sin Trælkvinde Bilha til Trælkvinde.
Labani anapereka wantchito wake wamkazi Biliha kwa Rakele kuti akhale wantchito wake.
30 Så gik Jakob også ind til Rakel, og han elskede Rakel højere end Lea. Derpå blev han i Labans Tjeneste syv År til.
Yakobo analowana ndi mkazi wake Rakele, ndipo Yakobo anakonda Rakele kuposa Leya. Ndipo anamugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri chifukwa cha Rakele.
31 Da HERREN så, at Lea blev tilsidesat, åbnede han hendes Moderliv, medens Rakel var ufrugtbar.
Pamene Mulungu anaona kuti Yakobo sankamukonda Leya kwambiri, Iye analola kuti Leya uja akhale ndi ana, ndi kuti Rakele akhale wosabala.
32 Så blev Lea frugtsommelig og fødte en Søn, som hun gav Navnet Ruben; thi hun sagde: "HERREN har set til min Ulykke; nu vil min Mand elske mig!"
Leya anakhala ndi pathupi ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha Rubeni pakuti anati, “Yehova waona kusauka kwanga. Zoonadi, mwamuna wanga adzandikonda tsopano.”
33 Siden blev hun frugtsommelig igen og fødte en Søn; og hun sagde: "HERREN hørte, at jeg var tilsidesat, så gav han mig også ham!" Derfor gav hun ham Navnet Simeon.
Anakhalanso ndi pathupi ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Yehova anamva kuti mwamuna wanga sakundikonda, choncho wandipatsanso mwana winayu.” Ndipo anamutcha dzina lake Simeoni.
34 Siden blev hun frugtsommelig igen og fødte en Søn; og hun sagde: "Nu må da endelig min Mand bolde sig til mig, da jeg har født ham tre Sønner." Derfor gav hun ham Navnet Levi.
Anatenganso pathupi kachitatu, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna anati, “Pano pokha tidzaphatikana kwambiri ndi mwamuna wanga, chifukwa ndamubalira ana aamuna atatu.” Kotero anamutcha dzina lake Levi.
35 Siden blev hun frugtsommelig igen og fødte en Søn; og hun sagde:"Nu vil jeg prise HERREN!" Derfor gav hun ham Navnet Juda. Så fik hun ikke flere Børn.
Anatenganso pathupi pena, ndipo pamene anabereka mwana wamwamuna, iye anati, “Nthawi ino ndidzalemekeza Yehova.” Choncho anamutcha Yuda. Kenaka analeka kubereka.

< 1 Mosebog 29 >