< 1 Mosebog 11 >
1 Hele Menneskeheden havde eet Tungemål og samme Sprog.
Nthawi imeneyo anthu onse a pa dziko lapansi ankayankhula chiyankhulo chimodzi ndipo mawu amene ankayankhula anali amodzi.
2 Da de nu drog østerpå, traf de på en Dal i Sinear, og der slog de sig ned.
Pamene anthu amapita chakummawa anapeza chigwa ku dziko la Sinara nakhazikikako.
3 Da sagde de til hverandre: "Kom, lad os stryge Teglsten og brænde dem godt!" De brugte nemlig Tegl som Sten og Jordbeg som Kalk.
Tsono anawuzana kuti, “Tiyeni tiwumbe njerwa ndi kuziwotcha bwinobwino.” Tsono mʼmalo mwa miyala anagwiritsa ntchito njerwa zowotcha, ndipo mʼmalo mwa matope anagwiritsa ntchito phula.
4 Derpå sagde de: "Kom, lad os bygge os en By og et Tårn, hvis Top når til Himmelen, og skabe os et Navn, for at vi ikke skal spredes ud over hele Jorden!"
Kenaka anati, “Tiyeni tidzimangire mzinda wokhala ndi nsanja yoti ikafike kumwamba kuti titchuke. Kupanda kutero tibalalikana pa dziko lonse lapansi.”
5 Men HERREN steg ned for at se Byen og Tårnet, som Menneskebørnene byggede,
Koma Yehova anatsika kudzaona mzindawo ndi nsanja imene anthu aja ankayimanga.
6 og han sagde: "Se, de er eet Folk og har alle eet Tungemål; og når de nu først er begyndt således, er intet, som de sætter sig for, umuligt for dem;
Yehova anati, “Anthuwa ndi amodzi, ndipo ali ndi chiyankhulo chimodzi. Izi akuchitazi nʼchiyambi chabe cha zomwe akufuna kukwaniritsa kuchita.
7 lad os derfor stige ned og forvirre deres Tungemål der, så de ikke forstår hverandres Tungemål!"
Tiyeni titsikireko tikasokoneze chiyankhulo chawo kuti asamamvetsetsane.”
8 Da spredte HERREN dem fra det Sted ud over hele Jorden, og de opgav at bygge Byen.
Choncho Yehova anabalalitsa anthu aja pa dziko lonse lapansi ndipo analeka kumanga mzindawo.
9 Derfor kaldte man den Babel, thi der forvirrede HERREN al Jordens Tungemål, og derfra spredte HERREN dem ud over hele Jorden.
Nʼchifukwa chake mzindawo unatchedwa Babeli, popeza Yehova anasokoneza chiyankhulo cha anthu onse. Powachotsa kumeneko, Yehova anawabalalitsira pa dziko lonse lapansi.
10 Dette er Sems Slægtebog. Da Sem var 100 År gammel, avlede han Arpaksjad, to År efter Vandfloden;
Nayi mibado yochokera kwa Semu. Patapita zaka ziwiri chitatha chigumula, Semu ali ndi zaka 100, anabereka Aripakisadi.
11 og efter at Sem havde avlet Arpaksjad, levede han 500 År og avlede Sønner og Døtre.
Atabereka Aripakisadi, Semu anakhala ndi moyo zaka 500 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
12 Da Atpaksjad havde levet 35 År, avlede han Sjela;
Pamene Aripakisadi anali ndi zaka 35, anabereka Sela.
13 og efter at Arpaksjad havde avlet Sjela, levede han 403 År og avlede Sønner og Døtre.
Atabereka Sela, Aripakisadi anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
14 Da Sjela havde levet 30 År, avlede han Eber;
Pamene Sela anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Eberi.
15 og efter at Sjela havde avlet Eber, levede han 403 År og avlede Sønner og Døtre.
Atabereka Eberi, Sela anakhala ndi moyo zaka zina 403 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
16 Da Eber havde levet 34 År, avlede han Peleg;
Pamene Eberi anali ndi zaka 34 anabereka Pelegi.
17 og efter at Eber havde avlet Peleg, levede han 430 År og avlede Sønner og Døtre.
Atabereka Pelegi, Eberi anakhala ndi moyo zaka zina 430 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
18 Da Peleg havde levet 30 År, avlede han Re'u;
Pamene Pelegi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Reu.
19 og efter at Peleg havde avlet Re'u, levede han 209 År og avlede Sønner og Døtre.
Atabereka Reu, Pelegi anakhala zaka zina 209 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
20 Da Re'u havde levet 32 År, avlede han Serug;
Pamene Reu anali ndi zaka 32, anabereka Serugi.
21 og efter at Re'u havde avlet Serug, levede han 207 År og avlede Sønner og Døtre.
Atabereka Serugi, Reu anakhala ndi moyo zaka zina 207 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
22 Da Serug havde levet 30 År, avlede han Nakor;
Pamene Serugi anali ndi zaka makumi atatu, anabereka Nahori.
23 og efter at Serug havde avlet Nakor, levede han 200 År og avlede Sønner og Døtre.
Atabereka Nahori, Serugi anakhala ndi moyo zaka zina 200 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
24 Da Nakor havde levet 29 År, avlede han Tara;
Pamene Nahori anali ndi zaka 29, anabereka Tera.
25 og efter at Nakor havde avlet Tara, levede han 119 År og avlede Sønner og Døtre.
Atabereka Tera, Nahori anakhala ndi moyo zaka zina 119 ndipo anali ndi ana ena aamuna ndi aakazi.
26 Da Tara havde levet 70 År, avlede han Abram, Nakor og Haran.
Pamene Tera anali ndi zaka 70, anabereka Abramu, Nahori ndi Harani.
27 Dette er Taras Slægtebog. Tara avlede Abram, Nako og Haran. Haran avlede Lot.
Nayi mibado yochokera mwa Tera. Tera anabereka Abramu, Nahori ndi Harani. Ndipo Harani anabereka Loti.
28 Haran døde i sin Fader Taras Levetid i sin Hjemstavn i Ur Kasdim.
Abambo ake a Tera akanali ndi moyo, Harani anamwalira ku Uri wa ku Akaldeya kumene anabadwira.
29 Abram og Nakor tog sig Hustruer; Abrams Hustru hed Saraj, Nakors Milka, en Datter af Haran, Milkas og Jiskas Fader.
Abramu ndi Nahori onse anakwatira. Dzina la mkazi wa Abramu linali Sarai, ndipo la mkazi wa Nahori linali Milika. Iyeyu ndi Isika abambo awo anali Harani.
30 Men Saraj var ufrugtbar og havde ingen Børn.
Sarai analibe ana chifukwa anali wosabereka.
31 Tara tog sin Søn Abram, sin Sønnesøn Lot, Harans Søn, og sin Sønnekone Saraj, hans Søn Abrams Hustru, og førte dem fra Ur Kasdim for at begive sig til Kana'ans Land; men da de kom til Karan, slog de sig ned der.
Tera anatenga mwana wake Abramu, mdzukulu wake Loti, ndi mpongozi wake Sarai, mkazi wa Abramu natuluka mzinda wa Uri wa ku Akaldeya kupita ku Kanaani. Pamene anafika ku Harani, anakhazikika kumeneko.
32 Taras Levetid var 205 År; og Tara døde i Karan.
Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.