< Ezekiel 11 >
1 Så løftede Ånden mig og bragte mig til Herrens huses østport, den der vender mod Øst. Og se, ved Indgangen til Porten var der fem og tyve Mænd, og jeg så iblandt dem Jaazanja, Azzurs Søn, og Pelatja, Benajas Søn, Folkets Fyrster.
Pamenepo Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kubwera nane ku chipata cha kummawa cha Nyumba ya Yehova. Kumeneko pa khomo la chipata panali anthu 25, ndipo ndinaona pakati pawo atsogoleri awa: Yaazaniya mwana wa Azuri ndi Pelatiya mwana wa Benaya.
2 Og han sagde til mig: "Menneskesøn! Det er de Mænd, som pønser på Uret og lægger onde Råd op i denne By,
Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi anthu amene akukonza zoyipa ndi kupereka malangizo oyipa mu mzindamo.
3 idet de siger: "Er Husene ikke nys bygget? Byen er Gryden, vi Kødet!"
Iwo amawuza anthu kuti, ‘Nthawi sinafike yoti timange Nyumba? Mzindawu uli ngati mʼphika umene uli pa moto ndipo ife tili ngati nyama mu mʼphikamo.
4 Profeter derfor imod dem, profeter, Menneskesøn!
Choncho iwe mwana wa munthu, unenere mowadzudzula. Nenera ndithu.’”
5 Så faldt HERRENs Ånd på mig, og han sagde til mig: Sig: Så siger HERREN: Således taler I, Israels Hus; jeg kender godt, hvad der stiger op i eders Ånd.
Ndipo Mzimu wa Yehova unandigwera ndipo unandiwuza kuti, “Unene kuti zimene akunena Yehova ndi izi. Iye akuti. ‘Izi ndi zimene mukunena, Inu Aisraeli, koma Ine ndikudziwa zimene zili mu mtima mwanu.’
6 Mange har I dræbt i denne By; I har fyldt dens Gader med dræbte.
Mwapha anthu ambiri mu mzinda muno ndipo mwadzaza misewu yake ndi mitembo.
7 Derfor, så siger den Herre HERREN: De, som I dræbte og henslængte i dens Midte, de er Kødet, og Byen er Gryden; men eder vil jeg føre ud af den.
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti, ‘Mitembo imene mwayiponya mʼmisewuyo ndiyo nyama ndipo mzinda uno ndiwo mʼphika, koma Ine ndidzakuthamangitsanimo.
8 I frygter for Sværd, og Sværd vil jeg bringe over eder, lyder det fra den Herre HERREN.
Inu mumaopa lupanga, koma lupangalo ndi limene ndidzakubweretsereni, akutero Ambuye.
9 Jeg vil føre eder ud af den og give eder i fremmedes Hånd, og jeg vil holde Dom over eder.
Ine ndidzakuthamangitsani mu mzinda ndipo ndidzakuperekani mʼdzanja la alendo kuti akulangeni.
10 For Sværd skal I falde; ved Israels Grænse vil jeg dømme eder. Og I skal kende, at jeg er HERREN.
Mudzaphedwa ndi lupanga ndipo ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
11 Byen skal ikke være eder en Gryde, og I skal ikke være Kødet deri; ved Israels Grænse vil jeg dømme eder.
Mzinda uno sudzakhala ngati mʼphika wokutetezani ndipo simudzakhalanso ngati nyama ya mʼmenemo. Ndidzakulangani mpaka kumalire a Israeli.
12 Og I skal kende, at jeg er HERREN, hvis Vedtægter I ikke fulgte, og hvis Lovbud I ikke levede efter, hvorimod I levede efter eders Nabofolks Lovbud. -
Ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova. Inu simunatsatire malangizo anga kapena kusunga malamulo anga koma mwakhala mukutsata zochita za mitundu ina ya anthu imene yakuzungulirani.’”
13 Men medens jeg profeterede således, døde Pelatja, Benajas Søn. Da faldt jeg på mit Ansigt og råbte med høj Røst: "Ak, Herre, HERRE, vil du da helt udrydde Israels Rest?"
Tsono pamene ndinkanenera, Pelatiya mwana wa Benaya anafa. Pomwepo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba ndipo ndinafuwula ndi mawu aakulu kuti “Mayo, Ambuye Yehova! Kodi mudzawatheratu Aisraeli onse otsala?”
14 Så kom HERRENs Ord til mig således:
Yehova anayankhula nane kuti,
15 Menneskesøn! Dine Brødre, dine Medfanger og alt Israels Hus, alle de, om hvem Jerusalems Indbyggere siger: "De er langt borte fra HERREN, os er Landet givet i Eje!" -
“Anthu okhala ku Yerusalemu akuwanena abale ako, anthu a ku ukapolo, onse a banja la Israeli, kuti, ‘Anthu onse amene anatengedwa ukapolo ali kutali ndi Yehova. Dziko lanu Yehova anatipatsa kuti likhale lathulathu.’”
16 derfor skal du sige: Så siger den Herre HERREN: Ja, jeg har ført dem langt bort blandt Folkene og spredt dem i Landene, og kun i ringe Måde var jeg dem en Helligdom i de Lande, hvor de kom hen.
“Nʼchifukwa chake nena kwa anzako a ku ukapolo kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Ine ndinawatumiza kutali pakati pa anthu a mitundu ina. Ndinawabalalitsa ku mayiko ambiri. Komabe ndakhala ndikuwasunga ku mayiko kumene anapitako!’
17 Men derfor skal du sige: Så siger den Herre HERREN: Jeg vil samle eder sammen fra Folkeslagene og sanke eder op i Landene, hvor I er spredt, og give eder Israels Jord.
“Nʼchifukwa chake uwawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kuti, Ndidzawasonkhanitsa kuchokera kwa anthu a mitundu inayo ndi kuwasonkhanitsira pamodzi kuchokera ku mayiko kumene ndinawabalalitsirako. Pambuyo pake ndidzawapatsa dziko la Israeli.
18 Derhen skal de komme og fjerne alle dets væmmelige Guder og alle dets Vederstyggeligheder;
“Akadzalowa mʼdzikomo adzachotsa mafano awo onse oyipa ndi onyansa.
19 jeg giver dem et nyt Hjerte og indgiver dem en ny Ånd; jeg tager Stenhjertet ud af deres Legeme og giver dem et Kødhjerte,
Ndidzawapatsa mtima watsopano ndipo ndidzayika mzimu watsopano mwa iwo. Ndidzachotsa mtima wowuma ngati mwala mwa iwo, ndipo ndidzawapatsa mtima wofewa ngati mnofu.
20 for at de må følge mine Vedtægter og holde mine Lovbud og gøre efter dem. Så skal de være mit Folk, og jeg vil være deres Gud.
Motero adzatsata malamulo anga ndipo adzasunga mosamala malamulo anga. Adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
21 Men hines Hjerter holder sig til deres væmmelige Guder og deres Vederstyggeligheder; dem gengælder jeg deres Færd, lyder det fra den Herre HERREN.
Koma kunena za amene akupembedza mafano oyipa ndi onyansa, ndidzawalanga chifukwa cha zimene achita. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
22 Så løftede keruberne Vingerne og samtidig Hjulene; og Israels Guds Herlighed var oven over dem.
Tsono akerubi aja anatambasula mapiko awo kuyamba kuwuluka, mikombero ili mʼmbali mwawo. Ulemerero wa Mulungu wa Israeli unali pamwamba pawo.
23 Og HERRENs Herlighed steg op fra Byen og stillede sig på Bjerget østen for.
Ulemerero wa Yehova unakwera ndi kusiya mzindawo ndipo unakayima pa phiri cha kummawa kwake kwa mzindawo.
24 Derpå løftede Ånden mig og bragte mig ved Guds Ånd i Synet til de landflygtige i Kaldæa; og Synet, som jeg havde skuet, steg op og svandt bort.
Pambuyo pake Mzimu wa Mulungu unandinyamula ndi kukandifikitsa. Zimenezi zinkachitika mʼmasomphenya monga mmene Mzimu wa Mulungu unkandionetsera. Kenaka masomphenya amene ndinkawaonawo anayamba kuzimirira.
25 Så kundgjorde jeg de landflyggige alle de Ord, HERREN havde åbenbaret mig.
Ndipo ndinafotokozera akapolowo zonse zimene Yehova anandionetsa.