< 2 Mosebog 38 >

1 Derpå lavede han Brændofferalteret af Akacietræ, fem Alen langt og fem Alen bredt, firkantet, og tre Alen højt.
Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229.
2 Han lavede Horn til dets fire Hjørner, således at de var i eet dermed, overtrak det med Kobber
Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa.
3 og lavede alt Alterets Tilbehør, Karrene, Skovlene, Skålene, Gaflerne og Panderne; alt dets Tilbehør lavede han af Kobber.
Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
4 Derpå omgav han Alteret med et flettet Kobbergitter neden under dets Liste, således at det nåede op til Alterets halve Højde.
Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo.
5 Derefter støbte han fire Ringe til Kobbergitterets fire Hjørner til at stikke Bærestængerne i.
Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira.
6 Bærestængerne lavede han at Akacietræ og overtrak dem med Kobber.
Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa.
7 Og Stængerne stak han gennem Ringene på Alterets Sider, for at det kunde bæres med dem. Han lavede det hult af Brædder.
Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.
8 Derpå lavede han Vandkummen med Fodstykke af Kobber og brugte dertil Spejle, som tilhørte Kvinderne, der gjorde Tjeneste ved Indgangen til Åbenbaringsteltet.
Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
9 Derpå indrettede han Forgården: Til Sydsiden det hundrede Alen lange Forgårdsomhæng af tvundet Byssus
Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
10 med tyve Piller og tyve Fodstykker af Kobber og med Knager og Bånd af Sølv til Pillerne.
Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
11 Til Nordsiden hundrede Alen med tyve Piller og tyve Fodstykker af Kobber og med Knager og Bånd af Sølv til Pillerne.
Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
12 Til Vestsiden det halvtredsindstyve Alen lange Omhæng med ti Piller og ti Fodstykker og med Knager og Bånd af Sølv til Pillerne.
Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
13 Og til Forsiden mod Øst, der var halvtredsindstyve Alen bred,
Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23.
14 det femten Alen lange Omhæng med fire Piller og tre Fodstykker til den ene Side af Indgangen,
Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu,
15 og det femten Alen lange Omhæng med tre Piller og tre Fodstykker til den anden Side af Indgangen.
polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
16 Alle Omhæng rundt om Forgården var af tvundet Byssus,
Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino.
17 Fodstykkerne til Pillerne af Kobber, men deres Knager og Bånd af Sølv; alle Pillernes Hoveder var overtrukket med Sølv; og de havde Bånd af Sølv.
Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.
18 Forhænget til Forgårdens Indgang var af violet og rødt Purpurgarn i broget Vævning, karmoisinrødt Garn og tvundet Byssus, tyve Alen langt og fem Alen højt, svarende til Bredden på Forgårdens Omhæng.
Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229,
19 Dertil hørte fire Piller med fire Fodstykker af Kobber; Knagerne var af Sølv og Overtrækket på Hovederne og Båndene ligeledes af Sølv.
pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva.
20 Alle Pælene til Boligen og Forgården rundt om var af Kobber.
Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.
21 Her følger Regnskabet over Boligen, Vidnesbyrdets Bolig, som på Moses's Bud blev opgjort af Leviterne under Ledelse af Itamar, en Søn af Præsten Aron;
Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi:
22 Bezal'el, en Søn af Hurs Søn Uri, af Judas Stamme havde udført alt, hvad HERREN havde pålagt Moses,
Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose,
23 sammen med Oholiab, Ahisamaks Søn, af Dans Stamme, som udførte Udskæringsarbejdet, Kunstvævningen og den brogede Vævning af violet og rødt Purpur, Karmoisin og Byssus.
pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala.
24 Hvad angår Guldet, der anvendtes til Arbejdet, under hele Arbejdet på Helligdommen, så løb det som Gave viede Guld op til 29 Talenter og 730 Sekel efter hellig Vægt.
Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.
25 Det ved Menighedens Mønstring indkomne Sølv løb op til 100 Talenter og 1775 Sekel efter hellig Vægt
Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika.
26 en, Beka, det halve af en Sekel efter hellig Vægt, af enhver, der måtte lade sig mønstre, altså fra Tyveårsalderen og opefter, i alt 603 550 Mand:
Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550.
27 De 100 Talenter Sølv medgik til Støbningen af Helligdommens og Forhængets Fodstykker, 100 Talenter til 100 Fodstykker, en Talent til hvert Fodstykke.
Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi.
28 Men de 1775 Sekel anvendte han til Knager til Pillerne, til at overtrække deres Hoveder med og til Bånd på dem.
Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.
29 Det som Gave viede Kobber udgjorde 70 Talenter og 2400 Sekel.
Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425.
30 Deraf lavede han Fodstykkerne til Åbenbaringsteltets Indgang, Kobberalteret med dets Kobbergitter og alt Alterets Tilbehør,
Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse,
31 Fodstykkerne til Forgården rundt om og til Forgårdens Indgang og alle Teltpælene til Boligen og alle Teltpælene til Forgården hele Vejen rundt.
matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.

< 2 Mosebog 38 >