< 2 Mosebog 32 >

1 Men da Folket så, at Moses tøvede med at komme ned fra Bjerget, samlede det sig om Aron, og de sagde til ham: "Kom og lav os en Gud, som kan drage foran os, thi vi ved ikke, hvad der er blevet af denne Moses, der førte os ud af Ægypten!"
Anthu ataona kuti Mose akuchedwa kutsika mʼphiri, anasonkhana kwa Aaroni ndipo anati, “Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.”
2 Da sagde Aron til dem: "Riv de Guldringe af, som eders Hustruer, Sønner og Døtre har i Ørene, og bring mig dem!"
Aaroni anawayankha kuti, “Vulani ndolo zagolide zimene avala akazi anu, ana anu aamuna ndi aakazi ndipo muzibweretse kwa ine.”
3 Så rev hele Folket deres Guldørenringe af og bragte dem til Aron.
Kotero anthu onse anavula ndolo zagolide ndi kubwera nazo kwa Aaroni.
4 Og han modtog dem af deres Hånd, formede Guldet med en Mejsel og lavede en støbt Tyrekalv deraf. Da sagde de: "Her, Israel, er din Gud, som førte dig ud af Ægypten!"
Choncho Aaroni analandira golideyo ndipo anamuwumba ndi chikombole ndi kupanga fano la mwana wangʼombe. Kenaka anthu aja anati, “Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.”
5 Og da Aron så det, byggede han et Alter for den, og Aron lod kundgøre: "I Morgen er det Højtid for HERREN!"
Aaroni ataona izi, anamanga guwa lansembe patsogolo pa mwana wangʼombeyo ndipo analengeza kuti, “Mawa kudzakhala chikondwerero cha Yehova.”
6 Tidligt næste Morgen ofrede de så Brændofre og bragte Takofre og Folket satte sig til at spise og drikke, og derpå stod de op for at lege.
Kotero tsiku linalo anthu anadzuka mmamawa ndithu ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Atatha kupereka nsembezo, anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.
7 Da sagde HERREN til Moses: "Skynd dig og stig ned, thi dit Folk, som du førte ud af Ægypten, har handlet ilde;
Pamenepo Yehova anati kwa Mose, “Tsika msanga, chifukwa anthu ako amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto aja adziyipitsa kwambiri.
8 hastigt veg de bort fra den Vej jeg bød dem at vandre; de har lavet sig en støbt Tyrekalv og tilbedt den og ofret til den med de Ord: Her, Israel, er din Gud, som førte dig ud af Ægypten!"
Iwo apatuka mwamsanga kuleka kutsatira zimene ndinawalamula. Ndiye adzipangira fano la mwana wangʼombe. Aligwadira ndi kuliperekera nsembe nʼkumati, ‘Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.’”
9 Og HERREN sagde til Moses: "Jeg har iagttaget dette Folk og set, at det er et halsstarrigt Folk.
Yehova anati kwa Mose, “Ine ndikuwadziwa anthu amenewa. Iwowa ndi ankhutukumve.
10 Lad mig nu råde, at min Vrede kan blusse op imod dem så vil jeg tilintetgøre dem; men dig vil jeg gøre til et stort Folk!"
Chifukwa chake undileke kuti mkwiyo wanga uyake pa iwo ndi kuwawononga. Ndipo Ine ndidzakusandutsa kuti ukhale mtundu waukulu.”
11 Men Moses bønfaldt HERREN sin Gud og sagde: "Hvorfor HERRE skal din Vrede blusse op mod dit Folk, som du førte ud af Ægypten med vældig Kraft og stærk Hånd?
Koma Mose anapempha chifundo cha Mulungu wake ndipo anati, “Chonde Yehova, chifukwa chiyani mwakwiyira anthu awa amene munawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
12 Hvorfor skal Ægypterne kunne sige: I ond Hensigt førte han dem ud, for at slå dem ihjel ude mellem Bjergene og udrydde dem af Jorden? Lad din Vredes Glød høre op, og anger den Ulykke, du vilde gøre dit Folk!
Kodi mukufuna kuti Aigupto azinena kuti, ‘Munali ndi cholinga choyipa chofuna kuwaphera ku mapiri kuno ndi kuwawonongeratu pa dziko lapansi pamene munkawatulutsa ku Igupto kuja?’ Ayi, chonde mkwiyo wanu woyaka ngati motowu ubwezeni ndipo sinthani maganizo ofunira zoyipa anthu anu.
13 Kom Abraham, Isak og Israel i Hu, dine Tjenere, hvem du tilsvor ved dig selv: Jeg vil gøre eders Afkom talrigt som Himmelens Stjerner, og jeg vil give eders Afkom hele det Land, hvorom jeg har talet, og de skal eje det evindelig!"
Kumbukirani atumiki anu, Abrahamu, Isake, Israeli ndi zija munawalonjeza polumbira pa dzina lanu kuti, ‘Ine ndidzachulukitsa zidzukulu zanu ndipo zidzakhala zambiri ngati nyenyezi zakumwamba. Zidzukulu zanuzo ndidzazipatsa dziko lonseli limene ndinalonjeza. Dziko limeneli lidzakhala lawo nthawi zonse.’”
14 Da angrede HERREN den Ulykke han havde truet med at gøre sit Folk.
Choncho Yehova analeka ndipo sanawachitire choyipa anthu ake monga anaopsezera.
15 Derpå vendte Moses tilbage og steg ned fra Bjerget med Vidnesbyrdets to Tavler i Hånden, Tavler, der var beskrevet på begge Sider, både på Forsiden og Bagsiden var de beskrevet.
Mose anatembenuka ndi kutsika phiri miyala iwiri ya pangano ili mʼmanja mwake. Miyalayi inalembedwa mbali zonse, kutsogolo ndi kumbuyo komwe.
16 Og Tavlerne var Guds Værk, og Skriften var Guds Skrift, ridset ind i Tavlerne.
Miyalayi anayikonza ndi Mulungu. Malembawo analemba ndi Mulungu mozokota pa miyalapo.
17 Da hørte Josua Støjen af det larmende Folk, og han sagde til Moses: "Der høres Krigslarm i Lejren!"
Pamene Yoswa anamva phokoso la anthu anati kwa Mose, “Ku msasa kuli phokoso la nkhondo.”
18 Men han svarede: "Det er ikke sejrendes eller slagnes Skrig, det er Sang, jeg hører!"
Mose anayankha kuti, “Phokoso limeneli sindikulimva ngati phokoso la opambana nkhondo, kapena kulira kwa ongonjetsedwa pa nkhondo. Koma ndikulimva ngati phokoso la anthu amene akuyimba.”
19 Og da Moses nærmede sig Lejren og så Tyrekalven og Dansen, blussede hans Vrede op, og han kastede Tavlerne fra sig og sønderslog dem ved Bjergets Fod.
Mose atayandikira msasa ndi kuona mwana wangʼombe ndiponso kuvina, anakwiya kwambiri ndipo anaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwake, ndi kuyiphwanya pa tsinde la phiri.
20 Derpå tog han Tyrekalven, som de havde lavet, brændte den i Ilden og knuste den til Støv, strøde det på Vandet og lod Israeliterne drikke det.
Ndipo iye anatenga mwana wangʼombe amene anthu anapanga uja ndi kumuwotcha pa moto ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi. Kenaka anawaza fumbilo mʼmadzi ndi kuwamwetsa Aisraeli madziwo.
21 Og Moses sagde til Aron: "Hvad har dette Folk gjort dig, siden du har bragt så stor en Synd over det?"
Tsono Mose anafunsa Aaroni kuti, “Kodi anthu awa anakuchita chiyani kuti uwachimwitse koopsa chotere?”
22 Aron svarede: "Vredes ikke, Herre! Du ved selv, at Folket ligger i det onde,
Aaroni anayankha kuti, “Musakwiye mbuye wanga. Inu mukudziwa kuti anthu awa ndi ovuta.
23 og de sagde til mig: Lav os en Gud, som kan drage foran os, thi vi ved ikke, hvad der er blevet af denne Moses, der førte os ud af Ægypten!
Iwo anati kwa ine, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa ife mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.’
24 Da sagde jeg til dem: De, der har Guldsmykker, skal rive dem af! De bragte mig da Guldet, og jeg kastede det i Ilden, og så kom denne Tyrekalv ud deraf!"
Choncho ine ndinawawuza kuti, ‘Aliyense amene ali ndi zokometsera zagolide azivule.’ Choncho iwo anandipatsa golide, ndipo ndinamuponya pa moto ndi kupanga fano la mwana wangʼombeyu.”
25 Da Moses nu så, at Folket var tøjlesløst til Skadefryd for deres Fjender, fordi Aron havde givet det fri Tøjler,
Mose anaona kuti anthuwo anali osokonezekadi chifukwa Aaroni anawalekerera mpaka kusanduka anthu osekedwa pakati pa adani awo.
26 stillede han sig ved Indgangen til Lejren og sagde: "Hvem der er for HERREN, han komme hid til mig!" Da samlede alle Leviterne sig om ham,
Choncho iye anayima pa chipata cholowera mu msasa ndipo anati, “Aliyense amene ali mbali ya Yehova abwere kwa ine.” Ndipo Alevi onse anapita mbali yake.
27 og han sagde til dem: "Så siger HERREN, Israels Gud: Bind alle Sværd om Lænd og gå frem og tilbage fra den ene Indgang i Lejren til den anden og slå ned både Broder, Ven og Frænde!"
Ndipo iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena, ‘Pitani ku misasa konse, mulowe ku zipata zonse ndipo aliyense akaphe mʼbale wake, kapena mnzake kapena mnansi wake.’”
28 Og Leviterne gjorde, som Moses havde sagt, og på den Dag faldt der af Folket henved 3000 Mand.
Alevi anachita zomwe Mose analamula, ndipo tsiku limenelo panafa anthu pafupifupi 3,000.
29 Og Moses sagde: "Fra i Dag af skal I være Præster for HERREN, thi ingen skånede Søn eller Broder, derfor skal Velsignelse komme over eder i Dag."
Kenaka Mose anati, “Lero mwadzipatula nokha kukhala ansembe otumikira Yehova. Mwachita izi popeza aliyense wa inu wapha mwana wake kapena mʼbale wake. Tsono lero Yehova wakudalitsani.”
30 Næste Dag sagde Moses til Folket: "I har begået en stor Synd; men nu vil jeg stige op til HERREN, måske kan jeg skaffe Soning for eders Synd!"
Mmawa mwake Mose anati kwa anthu onse, “Inu mwachita tchimo lalikulu. Koma tsopano ine ndipita ku phiri kwa Yehova mwina ndikatha kukupepeserani chifukwa cha tchimo lanu.”
31 Derpå gik Moses atter til HERREN og sagde: "Ak, dette Folk har begået en stor Synd, de har lavet sig en Gud af Guld.
Kotero Mose anabwereranso kwa Yehova ndipo anati, “Aa! Anthu awa achita tchimo lalikulu! Iwo adzipangira milungu yagolide.
32 Om du dog vilde tilgive dem deres Synd! Hvis ikke, så udslet mig af den Bog, du fører!"
Koma tsopano, chonde akhululukireni tchimo lawo. Ngati simutero, ndiye mundifute ine mʼbuku limene mwalemba.”
33 HERREN svarede Moses: "Den, som har syndet imod mig, ham vil jeg udslette af min Bog!
Yehova anamuyankha Mose kuti, “Ndidzafuta mʼbuku aliyense amene wandichimwira.
34 Men gå nu og før Folket hen, hvor jeg har befalet dig at føre det hen; se, min Engel skal drage foran dig! Men til sin Tid vil jeg straffe dem for deres Synd!"
Tsopano pita ukawatsogolere anthu kumalo kumene ine ndinanena, ndipo mngelo wanga adzakutsogolerani. Komabe, nthawi yanga ikadzafika kuti ndiwalange, ndidzawalanga chifukwa cha tchimo lawo.”
35 Og HERREN slog Folket, fordi de havde lavet Tyrekalven, den, Aron lavede.
Ndipo Yehova anawakantha anthuwo ndi mliri chifukwa anawumiriza Aaroni kuti awapangire fano la mwana wangʼombe.

< 2 Mosebog 32 >