< 5 Mosebog 4 >
1 Og nu, Israel! Hør de Anordninger og Lovbud, som jeg vil lære eder at holde, for at I kan blive i Live og komme ind og tage det Land i Besiddelse, som HERREN, eders Fædres Gud, vil give eder.
Mverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuphunzitseni. Muwatsatire kuti mukhale ndi moyo ndi kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu akukupatsani.
2 I må hverken lægge noget til eller trække noget fra, hvad jeg byder eder, men I skal holde HERREN eders Guds Bud, som jeg pålægger eder.
Musawonjezere pa zimene ndikukulamulirani ndipo musachotserepo, koma muwasunge malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani.
3 I har med egne Øjne set, hvad HERREN gjorde i Anledning af Ba'al Peor: Hver eneste Mand, som fulgte Ba'al Peor, udryddede HERREN din Gud af din Midte.
Inu munaona ndi maso anu zimene Yehova anachita ku Baala-Peori. Yehova Mulungu wanu anawononga aliyense amene anatsata Baala wa ku Peori pakati panu.
4 Men I, som holdt fast ved HERREN eders Gud, er alle i Live den Dag i Dag.
Koma inu nonse amene munagwiritsitsa Yehova Mulungu wanu mukanali ndi moyo mpaka lero.
5 Se, jeg har lært eder Anordninger og Lovbud, således som HERREN min Gud har pålagt mig, for at I skal handle derefter i det Land, I skal ind og tage i Besiddelse;
Taonani, ndakuphunzitsani malangizo ndi malamulo monga Yehova Mulungu wanga anandilamulira kuti inuyo muwatsatire mʼdziko limene mukulowa ndi kulitengali.
6 hold dem og følg dem! Thi det skal være eders Visdom og eders Kløgt i de andre Folks Øjne. Når de hører om alle disse Anordninger, skal de sige: "Sandelig, det er et vist og klogt Folk, dette store Folk!"
Muwasunge mosamalitsa pakuti zimenezi zidzaonetsa nzeru zanu ndi kuzindikira kwanu kwa anthu a mitundu ina, amene adzamva za malangizo onsewa nati, “Ndithudi, mtundu waukulu uwu ndi wa anthu anzeru ndi ozindikira.”
7 Thi hvor er der vel et stort Folk, som har Guder, der kommer til det, således som HERREN vor Gud gør det, når vi kalder på ham;
Mtundu wina wa anthu ndi uti umene uli waukulu chomwechi, woti ukhoza kukhala ndi milungu yawo pafupi monga mmene alili Yehova Mulungu wathu ndi ife nthawi zonse pamene tipemphera kwa Iye?
8 og hvor er der vel et stort Folk, der har så retfærdige Anordninger og Lovbud som hele denne Lov, jeg forelægger eder i Dag?
Ndipo ndi mtundu uti mwa mitundu ya anthu umene ndi waukulu chotere kuti nʼkukhala ndi malangizo ndi malamulo olungama ngati malamulo amene ndikuyika pamaso panu lero?
9 Kun skal du vogte dig og omhyggeligt tage Vare på dig selv, at du ikke glemmer, hvad du med egne Øjne har set, og at det ikke viger fra dit Hjerte, så længe du lever; og du skal fortælle dine Sønner og dine Sønners Sønner derom.
Inu mungosamala ndi kudziyangʼanira kwambiri nokha kuti musayiwale zimene maso anu aona. Musalole kuti zichoke mʼmitima mwanu pa moyo wanu wonse. Zimenezi muziphunzitse kwa ana anu ndi zidzukulu zanu ngakhale mʼtsogolo.
10 Glem ikke den Dag, du stod for HERREN din Guds Åsyn ved Horeb, da HERREN sagde til mig: "Kald mig Folket sammen, for at jeg kan kundgøre dem mine Ord, så de kan lære at frygte mig, så længe de lever på Jorden, og lære deres Sønner det samme!"
Kumbukirani tsiku limene munayimirira pamaso pa Yehova Mulungu wanu ku Horebu, pamene anati kwa ine, “Sonkhanitsa anthu pamaso panga kuti amve mawu anga ndi kuti aphunzire kundilemekeza mʼmoyo wawo onse mʼdzikomo ndi kuti ana awo aziwaphunzitsa zimenezi.”
11 Da trådte I frem og stod ved Bjergets Fod, medens Bjerget brændte i lys Lue helt ind i Himmelen, hylet i Mørke, Skyer og Mulm;
Munabwera pafupi ndi kuyima pa tsinde pa phiri pamene phirilo limayaka moto umene umafika mpaka kumwamba. Panalinso mtambo wakuda ndi mdima wambiri.
12 og da HERREN talede til eder ud fra Ilden, hørte I kun Ordene, men nogen Skikkelse så I ikke, kun en Røst fornam I.
Kenaka Yehova anayankhula nanu kuchokera mʼmotowo. Inu munamva mawu ake okha koma simunamuone pakuti panali mawu chabe.
13 Da kundgjorde han eder sin Pagt, som han bød eder at holde, de ti Ord, og han skrev dem på to Stentavler.
Iye anakuwuzani Malamulo Khumi omwe ndi pangano lake limene anakulamulirani kuti mutsatire. Ndipo anawalemba malamulowo pa mapale awiri a miyala.
14 Og mig bød HERREN dengang at lære eder Anordninger og Lovbud, som I skulde overholde idet Land, I nu skal over og tage i Besiddelse.
Ndipo Yehova anandilamula nthawi imene ija kuti ndikuphunzitseni malangizo ndi malamulo amene muyenera kutsata mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani.
15 Eftersom I ikke så nogen Skikkelse, dengang HERREN talede til eder på Horeb ud fra Ilden, så vogt eder nu omhyggeligt for
Tsiku limene Yehova anayankhula nanu ku Horebu mʼmoto uja, simunaone thupi lake. Choncho mudziyangʼanire nokha mosamalitsa,
16 at handle så ryggesløst, at I laver eder et Gudebillede, en Stenstøtte i en eller anden Skikkelse, enten det nu er et Afbillede af en Mand eller en Kvinde
kuti musasokonezeke ndi kudzipangira nokha fano kapena chifanizo cha mtundu uliwonse, kaya chokhala ngati mwamuna kapena ngati mkazi,
17 eller et Afbillede af et eller andet Dyr, der lever på Jorden, eller et Afbillede af en eller anden vinget Fugl, der flyver under Himmelen,
kaya chokhala ngati nyama iliyonse ya pa dziko lapansi kapena mbalame iliyonse yowuluka mlengalenga.
18 eller et Afbillede af et eller andet Kryb, der kryber på Jorden, eller et Afbillede af en eller anden Fisk i Vandet under Jorden;
Kapena cholengedwa chilichonse choyenda pa nthaka kapena nsomba ya mʼmadzi akuya.
19 og når du løfter dit Blik til Himmelen og ser Solen og Månen og Stjernerne, hele Himmelens Hær, så vogt dig for at lade dig forføre til at tilbede og dyrke dem. Thi HERREN din Gud har tildelt alle de andre Folk under hele Himmelen dem;
Ndipo pamene muyangʼana kumwamba muona dzuwa, mwezi ndi nyenyezi, zonse zakumwambazo musakopeke kuti muzigwadire ndi kumapembedza zinthu zimene Yehova wapereka kwa anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi.
20 men eder tog HERREN og førte ud af Smelteovnen, af Ægypten, for at I skulde være hans Ejendomsfolk, som I nu er.
Koma inuyo, Yehova anakutengani ndi kukutulutsani mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo, ku Igupto kuti mukhale anthu olandira chuma chake monga mmene mulili tsopano.
21 Men HERREN blev vred på mig for eders Skyld og svor, at jeg ikke skulde komme over Jordan ind i det herlige Land, som HERREN din Gud vil give dig i Eje,
Yehova anakwiya nane chifukwa cha inu, ndipo analumbira kwathunthu kuti sindidzawoloka Yorodani ndi kulowa mʼdziko labwinolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani inu ngati cholowa chanu.
22 thi jeg skal dø i Landet her; jeg skal ikke komme over Jordan, men I skal komme over og tage dette herlige Land i Besiddelse.
Ine ndifera mʼdziko lino, sindiwoloka Yorodani. Koma inu mwatsala pangʼono kuwoloka ndi kukatenga dziko labwinolo.
23 Så vogt eder for at glemme HERREN eders Guds Pagt, som han sluttede med eder, og for at lave eder noget Gudebillede i Skikkelse af noget som helst, HERREN din Gud har forbudt dig
Samalani, musayiwale pangano limene Yehova Mulungu wanu anapangana nanu ndipo musadzipangire nokha fano la chinthu chilichonse chimene Yehova Mulungu wanu waletsa.
24 Thi HERREN din Gud er en fortærende Ild, en nidkær Gud!
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi moto wonyeketsa ndipo ndi Mulungu wansanje.
25 Når du får Børn og Børnebørn, og I bliver gamle i Landet, og I da handler så ryggesløst, at I laver eder Gudebilleder i en eller anden Skikkelse og gør, hvad der er ondt i HERREN din Guds Øjne, så at I fortørner ham,
Mukadzakhala nthawi yayitali mʼdzikomo ndi kubereka ana ndi kukhala ndi zidzukulu ndipo mukadzasokonekera ndi kupanga fano la mtundu uliwonse, nʼkumachita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kumukwiyitsa,
26 så kalder jeg i Dag Himmelen og Jorden til Vidne imod eder på, at I hastigt skal blive udryddet af det Land, I skal over Jordan og tage i Besiddelse; I skal ikke få noget langt Liv der, men visselig gå til Grunde;
ine ndi kuti kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni lero zokutsutsani kuti mudzawonongedwa msanga ndipo mudzachotsedwa mʼdziko limene mutenge mukawoloka Yorodani. Simudzakhalitsa kumeneko koma mudzawonongedwa ndithu.
27 og HERREN vil splitte eder mellem Folkene, og kun nogle få af eder skal blive tilbage blandt de Folkeslag, HERREN driver eder hen iblandt.
Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu ena. Ochepa okha pakati panu ndi amene adzapulumuke pakati pa anthu a mitundu ina kumene Yehova adzakupirikitsireniko.
28 Der skal I komme til at dyrke Guder, der er Menneskehænders Værk, Træ og Sten, som hverken kan se eller høre, spise eller lugte!
Kumeneko mudzapembedza milungu ya mitengo ndi miyala yopangidwa ndi anthu, imene singaone kapena kumva kapena kudya kapena kununkhiza.
29 Der skal I så søge HERREN din Gud, og du skal finde ham, når du søger ham af hele dit Hjerte og hele din Sjæl.
Mukanali komweko, ngati mudzamufunafuna Yehova Mulungu wanu mudzamupeza koma ngati mutamufunafuna ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
30 I de kommende Dage, når du er i Nød, og alle disse Ting kommer over dig, skal du vende om til HERREN din Gud og adlyde hans Røst.
Mukadzakhala pa chipsinjo ndipo zonsezi zikadzakuchitikirani, ndi pamene pambuyo pake mudzabwerera kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera Iye.
31 Thi en barmhjertig Gud er HERREN din Gud; han slipper dig ikke og lader dig ikke gå til Grunde og glemmer ikke Pagten med dine Fædre, som han tilsvor dem.
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wachifundo, Iye sadzakutayani kapena kukuwonongani kapena kuyiwala pangano lake ndi makolo anu, limene analitsimikiza mwa lumbiro.
32 Thi gransk dog i de henfarne Tider, der gik forud for dig, lige fra den Tid af da Gud skabte Menneskene på Jorden, og fra den ene Ende af Himmelen til den anden, om der er sket noget så stort som dette, eller om dets Lige er hørt.
Tsopano tafunsani za masiku a mʼmbuyomu, zakale inu musanabadwe, kuyambira tsiku limene Mulungu analenga munthu pa dziko lapansi. Tafufuzani kuyambira kumapeto mpaka mapeto anzake a thambo. Kodi chinachitikako china chachikulu ngati ichi, kapena chinayamba chamvekako chokhala ngati ichi?
33 Har noget Folk hørt Guds Røst ud fra Ilden, således som du hørte det, og levet?
Kodi uliponso mtundu wina wa anthu umene unamva mawu a Mulungu akuyankhula kuchokera mʼmoto nʼkukhala ndi moyo monga mwachitira inumu?
34 Eller har nogen Gud søgt at komme og hente sig et Folk midt ud af et andet Folk ved Prøvelser, Tegn og Undere, ved Krig, med stærk Hånd og udstrakt Arm og store Rædsler, således som du med egne Øjne så HERREN eders Gud gøre med eder i Ægypten?
Kodi alipo mulungu amene anayeserapo kudzitengera mtundu wa anthu kuwachotsa mu mtundu unzake mwa mayesero, zizindikiro zozizwitsa, nkhondo, komanso mwa mphamvu zake zopanda malire, kapena mwa zochita zazikulu ndi zochititsa mantha, monga zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Igupto inu mukupenya?
35 Du fik det at se, for at du skulde vide, af HERREN og ingen anden er Gud.
Iye anakuonetsani zonsezi kuti inu muzindikire kuti Yehova ndiye Mulungu, palibenso wina wofanana naye.
36 Fra Himmelen lod han dig høre sin Røst for at undervise dig, og på Jorden lod han dig se sin store Ild, og hans Ord hørte du ud fra Ilden.
Kuchokera kumwamba, Iye anafuna kuti inu mumve mawu ake ndi kuti mukhale osunga mwambo. Pa dziko lapansi anakuonetsani moto waukulu, ndipo inu munamva mawu ake kuchokera mʼmotomo.
37 Og fordi han elskede dine Fædre og udvalgte deres Afkom efter dem og selv førte dig ud af Ægypten ved sin store Vælde
Popeza anakonda makolo anu ndi kusankha adzukulu awo, a pambuyo pawo, anakutulutsani kuchoka ku Igupto ali pakati panu ndi mphamvu yake,
38 for at drive Folk bort foran dig, der er større og mægtigere end du selv, og lade dig komme ind i deres Land og give dig det i Eje, som det nu er sket,
kuti akupirikitsireni mayiko akuluakulu ndi amphamvu kuposa inu, ndi kukubweretsani inu ku dziko lawo kuti likhale lanu, monga liliri lero.
39 derfor skal du i Dag vide og lægge dig på Sinde, at HERREN og ingen anden er Gud oppe i Himmelen og nede på Jorden.
Vomerezani lero ndipo dziwani mu mtima mwanu kuti Yehova ndiye Mulungu kumwamba ndi pa dziko lapansi. Palibenso wina.
40 Og du skal holde hans Anordninger og Bud, som jeg pålægger dig i Dag, for at det kan gå dig og dine Børn efter dig vel, og for at du alle Dage kan leve længe i det Land, HERREN din Gud giver dig!
Sungani malangizo ake ndi malamulo ake amene ndikukupatsani lero lino, kuti zikuyendereni bwino inu ndi ana anu kutsogoloko, ndi kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kwa nthawi zonse.
41 På den Tid udskilte Moses tre Byer hinsides Jordan, på den østre Side,
Kenaka Mose anapatula mizinda itatu cha kummawa kwa Yorodani,
42 som Tilflugtsteder for Manddrabere, der uforsætligt slår et andet Menneske ihjel uden i Forvejen at have båret Nag til ham, for at de kan redde Livet ved at ty til en af disse Byer,
kumene aliyense amene wapha munthu akhoza kuthawirako ngati wopha munthuyo sanaphe mnzakeyo mwadala ndi maganizo oyipa. Iye akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi napulumutsa moyo wake.
43 nemlig Bezer i Ørkenen på Højsletten for Rubeniterne, Ramot i Gilead for Gaditerne og Golan i Basan for Manassiterne.
Mizindayo inali iyi: ku fuko la Rubeni, unali mzinda wa Bezeri ku mapiri a ku chipululu; ku fuko la Gadi, unali Ramoti ku Giliyadi; ndipo ku fuko la Manase, unali Golani ku Basani.
44 Dette er den Lov, Moses forelagde Israelitterne.
Awa ndi malamulo amene Mose anapereka kwa Aisraeli.
45 Dette er de Vidnesbyrd, Anordninger og Lovbud, Moses kundgjorde Israelitterne, da de drog bort fra Ægypten,
Izi ndi ndondomeko, malangizo ndi malamulo amene Mose anawapatsa iwo pamene anatuluka ku Igupto.
46 hinsides Jordan i Dalen lige for Bet Peor i det Land, der havde tilhørt Amoriterkongen Sihon, som boede i Hesjbon, og som Moses og Israelitterne havde slået, da de drog bort fra Ægypten.
Anali ku chigwa cha kufupi ndi Beti-Peori mbali ya kummawa kwa Yorodani, mʼdziko la Sihoni mfumu ya Aamori amene ankalamulira ku Hesiboni ndipo anagonjetsedwa ndi Mose ndi Aisraeli pamene ankachokera ku Igupto.
47 De havde erobret hans og Kong Og af Basans Land, de to Amoriterkonger hinsides Jordan, på den østre Side,
Iye anamulanda dziko lake ndi dziko la Ogi mfumu ya ku Basani. Awa anali mafumu awiri Aamori a kummawa kwa Yorodani.
48 fra Aroer ved Arnonflodens Bred til Sirjons Bjerg, det er Hermon,
Dziko ili linayambira ku Aroeri cha kumphepete kwa khwawa la Arinoni ku phiri la Siyoni (limeneli ndi phiri la Herimoni),
49 tillige med hele Arabalavningen hinsides Jordan, på den østre Side, lige til Arabahavet neden for Pisgas Skrænter.
ndi kuphatikizapo dziko lonse la Araba cha kummawa kwa Yorodani mpaka kukafika ku Nyanja ya Araba, kumunsi kwa Phiri la Pisiga.