< 5 Mosebog 18 >
1 Levitpræsterne, hele Levis Stamme, skal ikke have arvelod og Del sammen med det øvrige Israel, men leve af HERRENs Ildofre og af det, der tilfalder ham.
Ansembe Achilevi amene ndi fuko lonse la Alevi, asapatsidwe malo kapena cholowa pakati pa Aisraeli. Iwowa azidzadya zoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe, popeza zimenezo ndiye cholowa chawo.
2 Han må ikke eje nogen Arvelod blandt sine Brødre; HERREN er hans Arvelod, som han lovede ham.
Iwowa sadzakhala ndi cholowa pakati pa abale awo pakuti Yehova ndiye cholowa chawo monga anawalonjezera.
3 Og dette skal være den Ret, Præsterne har Krav på hos Folket, hos dem, der slagter Ofre, være sig Okser eller Småkvæg: Han skal give Præsten Boven, Kæberne og Kaljunet.
Anthu amene abwera kudzapereka nsembe ya ngʼombe kapena nkhosa, azipereka kwa wansembe gawo lake motere: mwendo wakutsogolo, nyama yamʼmasaya ndi zamʼkati.
4 Det første af dit Korn, din Most og din Olie og den første Uld af dine Får skal du give ham.
Muziwapatsa zamasika zoyamba za tirigu wanu, vinyo watsopano ndi mafuta, ndi ubweya woyamba pometa nkhosa zanu,
5 Thi ham har HERREN din Gud udvalgt blandt alle dine Stammer, så at han og hans Sønner altid skal gøre Præstetjeneste i HERRENs Navn.
pakuti Yehova Mulungu wanu wawasankha iwowa ndi ana awo pakati pa mafuko anu onse kuti aziyimirira ndi kutumikira mʼdzina la Yehova nthawi zonse.
6 Når en Levit inden dine Porte et steds i Israel, hvor han har haft sit Ophold, kommer til det Sted, HERREN udvælger det står ham frit for at komme, hvis han vil
Ngati Mlevi asuntha achoka ku mzinda wake ndi kupita kumalo kwina kumene Yehova wasankha mu Israeli momwemo ndi mtima wake wonse,
7 må han gøre Præstetjeneste i HERREN sin Guds Navn, lige så vel som alle hans Brødre, de andre Leviter, der står for HERRENs Åsyn der.
kumeneko akhoza kukatumikirako mʼdzina la Yehova Mulungu wake monga Alevi anzake onse amene akutumikira pamaso pa Yehova.
8 De skal nyde samme Ret, fraregnet hvad enhver er kommet til ved Salg af sin Fædrenearv.
Iye ayenera kulandira zogawana zawo mofanana ndi anzakewo ngakhale kuti iye anagulitsa kale cholowa cha pa banja pawo.
9 Når du kommer ind i det Land, HERREN din Gud vil give dig, må du ikke lære at efterligne disse Folks Vederstyggeligheder.
Mukafika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musakaphunzire makhalidwe onyansa a anthu a mʼdzikolo.
10 Der må ingen findes hos dig, som lader sin Søn eller datter gå igennem. Ilden, ingen, som driver Spådomskunst, tager Varsler, er Sandsiger eller øver Trolddom,
Pasapezeke pakati panu munthu wootcha pa moto mwana wake wamwamuna kapena wamkazi ngati nsembe. Asapezekenso pakati panu munthu wowombeza kapena wochita mawula, wolosera, wochita za ufiti,
11 ingen, som foretager Besværgelse eller gør Spørgsmål til Genfærd og Sandsigerånder og henvender sig til de døde;
wolodza, kapena woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ndi kumafunsira nzeru kwa anthu akufawo.
12 thi enhver, der gør sligt, er HERREN vederstyggelig, og for disse Vederstyggeligheders Skyld er det, at HERREN din Gud driver dem bort foran dig.
Aliyense wochita zinthu zotere ndi wonyansa pamaso pa Yehova, ndipo chifukwa cha zonyansa zimenezi Yehova adzakupirikitsirani mitundu ya anthu imeneyi.
13 Ustraffelig skal du være for HERREN din Gud.
Muzikhala angwiro pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
14 Thi disse Folk, som du skal drive bort, hører på dem, der tager Varsler og driver Spådomskunst; men sligt har HERREN din Gud ikke tilladt dig.
Mitundu ya anthu imene mudzayipirikitseyo imamvera anyanga kapena owombeza mawula. Koma inu Yehova Mulungu wanu sanakuvomerezeni kutero.
15 HERREN din Gud vil lade en Profet som mig fremstå af din Midte, af dine Brødre; ham skal I høre på.
Yehova Mulungu wanu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine. Muyenera kumumvera ameneyo.
16 Således udbad du dig det jo af HERREN din Gud ved Horeb, den Dag I var forsamlede, da du sagde: "Lad mig ikke mere høre HERREN min Guds Røst og se denne vældige Ild, at jeg ikke skal dø!"
Pakuti izi ndi zimene munapempha kwa Yehova Mulungu wanu ku Horebu pa tsiku la msonkhano lija pamene munati, “Ife tisamvenso mawu a Yehova Mulungu wathu kapena kuona moto woopsawu, kuopa kuti tingafe.”
17 Da sagde HERREN til mig: "De har talt rettelig!
Yehova anati kwa ine, “Zimene akunenazi ndi zabwino.
18 Jeg vil lade en Profet som dig fremstå for dem af deres Brødre og lægge mine Ord i hans Mund, og han skal sige dem alt, hvad jeg byder ham!
Ndidzawawutsira mneneri ngati iwe pakati pa abale awo ndipo ndidzayika mawu anga mʼkamwa mwake ndipo adzawawuza chilichonse chimene ndidzamulamula.
19 Og enhver, der ikke vil høre mine Ord, som han taler i mit Navn, ham vil jeg kræve til Regnskab.
Ine mwini ndidzaweruza aliyense amene sadzamvera mawu anga amene mneneriyo adzayankhula mʼdzina langa.
20 Men den Profet, der formaster sig til at tale noget i mit Navn, som jeg ikke har pålagt ham at tale, eller taler i en anden Guds Navn, den Profet skal dø!"
Koma mneneri wonena zinthu mʼdzina langa ndisanamulamulire kutero, kapena mneneri wonenera mʼdzina la milungu ina, ayenera kuphedwa.”
21 Og hvis du tænker ved dig selv: "Hvorledes skal vi kende det Ord, HERREN ikke har talt?"
Mwina mukhoza kumadzifunsa kuti, “Kodi tingadziwe bwanji kuti uthengawu sanayankhule ndi Yehova?”
22 så vid: Hvad en Profet taler i HERRENs Navn, uden at det sker og indtræffer, det er noget, HERREN ikke har talt. I Formastelighed har Profeten udtalt det, og du skal ikke være bange for ham!
Ngati zimene mneneriyo wanenera mʼdzina la Yehova sizinachitike kapena kukwaniritsidwa, ndiye kuti umenewo si uthenga umene Yehova wayankhula. Mneneri ameneyo amangoyankhula za mʼmutu mwake ndiye musadzidzimuke naye.