< Anden Kongebog 8 >

1 Elisa talte til den Kvinde, hvis Søn han havde kaldt til Live, og sagde: "Drag bort med dit Hus og slå dig ned som fremmed et eller andet Sted, thi HERREN har kaldt Hungersnøden hid; og den vil komme over Landet og vare syv År!"
Ndipo Elisa anawuza mayi amene anamuukitsira mwana wake kuti, “Choka kuno pamodzi ndi banja lako ndipo ukakhale kulikonse ukufuna, chifukwa Yehova akubweretsa njala ya zaka zisanu ndi ziwiri mʼdziko muno.”
2 Da brød Kvinden op og gjorde, som den Guds Mand havde sagt, og drog med sit Hus hen og boede syv År som fremmed i Filisternes Land.
Mayiyo ananyamuka nachita zimene munthu wa Mulungu ananena. Iye pamodzi ndi banja lake anachoka nakakhala ku dziko la Afilisti zaka zisanu ndi ziwiri.
3 Men da der var gået syv År, vendte Kvinden tilbage fra Filisternes Land; Og hun gik hen og påkaldte Kongens Hjælp til at få sit Hus og sin Jord tilbage.
Zitatha zaka zisanu ndi ziwirizo anabwera kuchokera ku dziko la Afilisti ndipo anapita kwa mfumu kukafunsa za nyumba yake ndi munda wake.
4 Kongen talte just med den Guds Mands Tjener Gehazi og sagde: "Fortæl mig om alle de storeGerninger, Elisa harudført!"
Ndipo mfumu inkayankhula ndi Gehazi, mtumiki wa munthu wa Mulungu kuti, “Tandiwuza zinthu zikuluzikulu zimene Elisa wachita.”
5 Og netop som han fortalte Kongen, hvorledes han havde kaldt den døde til Live, kom Kvinden, hvis Søn han havde kaldt til Live, og påkaldt Kongens Hjælp til at få sit Hus og sin Jord tilbage. Da sagde Gehazi: "Herre Konge, der er den Kvinde, og der er hendes Søn. som Elisa kaldte til Live!"
Pamene Gehazi ankayiwuza mfumuyo momwe Elisa anaukitsira anthu akufa, mayi amene mwana wake Elisa anamuukitsa kwa akufayo analowa kudzafunsa mfumu za nyumba yake ndi munda wake. Gehazi anati, “Mbuye wanga mfumu, mayi wake ndi uyu ndipo mwana wakeyo ndi uyu amene Elisa anamuukitsa kwa akufa.”
6 Kongen spurgte så Kvinden ud, og hun forfalte. Derpå gav Kongen hende en Hofmand med og sagde: "Sørg for, at hun får al sin Ejendom tilbage og alt, hvad hendes Jord har båret, siden den Dag hun forlod Landet!"
Mfumu inafunsa mayiyo za nkhaniyi ndipo iye anayifotokozera mfumuyo. Ndipo mfumu inasankha munthu woti ayendetse nkhani yake ndipo inati, “Mubwezereni zonse zimene zinali zake, kuphatikizapo phindu lonse lochokera mʼmunda wake, kuyambira tsiku limene anachoka mpaka tsopano lino.”
7 Siden begav Elisa sig til Damaskus, hvor Kong Benbadad af Aram lå syg. Da Kongen fik at vide, at den Guds Mand var på Vej derhen,
Elisa anapita ku Damasiko, ndipo Beni-Hadadi mfumu ya ku Aramu ankadwala. Mfumuyo itawuzidwa kuti, “Munthu wa Mulungu wabwera kuno kuchokera kutali,”
8 sagde han til Hazael: "Tag en Gave med, gå den Guds Mand i Møde og rådspørg HERREN gennem ham, om jeg kommer mig af min Sygdom!"
inawuza Hazaeli kuti, “Tenga mphatso ndipo pita ukakumane ndi munthu wa Mulungu. Ukandifunsire kwa Yehova kudzera mwa iye kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
9 Da gik Hazael ham i Møde; han tog en Gave med af alskens Kostbarheder, som fandfes i Damaskus, fyrretyve Kamelladninger, og trådte frem for ham og sagde: "Din Søn Benhadad, Arams Konge sender mig til dig og lader spørge: Kommer jeg mig af min Sygdom?"
Choncho Hazaeli anapita kukakumana ndi Elisa, atasenzetsa ngamira 40 mphatso za zinthu zosiyanasiyana zabwino kwambiri za ku Damasiko. Iye analowa mʼnyumba ya Elisa ndi kuyima pamaso pake, ndipo anati, “Mwana wanu Beni-Hadadi wandituma kuti ndidzakufunseni kuti, ‘Kodi ndidzachira matenda angawa?’”
10 Elisa svarede: "Gå hen og sig ham: Du kommer dig!" Men HERREN har ladet mig skue, at han skal dø!"
Elisa anayankha kuti, “Pita ndipo ukamuwuze kuti, ‘Udzachira ndithu,’ koma Yehova wandionetsa kuti adzafabe.”
11 Og han stirrede stift frem for sig og var ude af sig selv af Rædsel. Så brast den Guds Mand i Gråd,
Elisa anamuyangʼana kwambiri Hazaeli mpaka anachita manyazi. Pamenepo munthu wa Mulungu anayamba kulira.
12 og Hazael sagde: "Hvorfor græder min Herre?" Han svarede: "Fordi jeg ved, hvilke Ulykkkr du skal bringe over Israeliterne! Deres Fæstninger skal du stikke i Brand, deres unge Mænd skal du hugge ned med Sværdet, deres spæde Børn skal du knuse, og på deres frugtsommelige Kvinder skal du rive Livet op!"
Hazaeli anafunsa kuti, “Mbuye wanga mukulira chifukwa chiyani?” Elisa anayankha kuti, “Chifukwa ndikudziwa choyipa chimene udzachitira Aisraeli. Udzatentha mizinda yawo ya chitetezo, udzapha anyamata awo ndi lupanga, udzaphwanyitsa pansi makanda awo ndiponso udzatumbula mimba za akazi awo oyembekezera.”
13 Da sagde Hazael: "Hvad er din Træl, den Hund, at han skal kunne gøre slige store Ting!" Elisa svarede: "HERREN har ladet mig skue dig som Konge over Aram!"
Ndipo Hazaeli anati, “Kodi kapolo wanune, amene ndine wonyozeka ngati galu, ndingathe bwanji kuchita chinthu chachikulu chotere?” Elisa anayankha kuti, “Yehova wandionetsa kuti iwe udzakhala mfumu ya ku Aramu.”
14 Derpå forlod han Elisa og kom til sin Herre; og han spurgte ham: "Hvad sagde Elisa til dig?" Han svarede: "Han sagde: Du kommer dig!"
Choncho Hazaeli anasiyana ndi Elisa ndi kubwerera kwa mbuye wake. Beni-Hadadi atafunsa kuti, “Elisa wakuwuza chiyani?” Hazaeli anayankha kuti, “Elisa wandiwuza kuti inu mudzachira ndithu.”
15 Men næste Dag tog han et Klæde, dyppede det i Vand og bredte det over Ansigtet på Kongen, og det blev hans Død. Og Hazael blev Konge i hans Sted.
Koma mmawa mwake Hazaeli anatenga nsalu yokhuthala ndi kuyiviyika mʼmadzi ndipo anaphimba nayo nkhope ya mfumu, kotero mfumuyo inafa. Hazaeli analowa ufumu mʼmalo mwake.
16 I Akabs Søns, Kong Joram af Israels, femte Regeringsår blev Joram, Josafats Søn, Konge over Juda.
Chaka chachisanu cha ufumu wa Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya ku Israeli, Yehosafati ali mfumu ya ku Yuda, Yehoramu mwana wake anakhala mfumu ya Ayuda.
17 Han var to og tredive År gammel, da han blev Konge, og han herskede otte År i Jerusalem.
Yehoramu analowa ufumu ali ndi zaka 32, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
18 Han vandrede i Israels Kongers Spor ligesom Akabs Hus, thi han havde en Datter af Akab til Hustru, og han gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne.
Iye anatsatira khalidwe la mafumu a ku Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, popeza iye anakwatira mwana wa Ahabu. Yehoramu anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
19 Dog vilde HERREN ikke tilintetgøre Juda for sin Tjener Davids Skyld efter det Løfte, han havde givet ham, at han altid skulde have en Lampe for hans Åsyn.
Komabe, chifukwa cha mtumiki wake Davide, Yehova sanafune kuwononga Yuda popeza Yehova analonjeza Davide kuti adzamupatsa nyale pamodzi ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
20 I hans Dage rev Edomiterne sig løs fra Judas Overherredømme og valgte sig en Konge.
Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira ulamuliro wa Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
21 Da drog Joram over til Za'ir med alle sine Stridsvogne. Og han stod op om Natten, og sammen med Vognstyrerne slog han sig igennem Edoms Rækker, der havde omringet ham, hvorpå Folket flygtede tilbage hver til sit.
Choncho Yehoramu anapita ku Zairi pamodzi ndi magaleta ake onse. Ndipo iye anakantha Aedomu amene anamuzungulira pamodzi ndi oyendetsa magaleta ake usiku. Koma ankhondo ake anathawa napita ku misasa yawo.
22 Således rev Edom sig løs fra Judas Overherredømme, og således er det den Dag i Dag. På samme Tid rev også Libna sig løs.
Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira Yuda. Nthawi yomweyo mzinda wa Libina unawukiranso.
23 Hvad der ellers er at fortælle om Joram, alt, hvad han udførte, står optegnet i Judas Kongers Krønike.
Ndipo ntchito zina za Yehoramu ndi zonse zomwe anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
24 Så lagde Joram sig til Hvile hos sine Fædre og blev jordet hos sine Fædre i Davidsbyen; og hans Søn Ahazja blev Konge i hans Sted.
Choncho Yehoramu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 I Akabs Søns, Kong Joram af Israels, tolvte Regeringsår blev Ahazja, Jorams Søn, Konge over Juda.
Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri cha Yoramu mwana wa Ahabu mfumu ya Israeli, Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
26 Ahazja var to og tyve År gammel, da han blev Konge, og han herskede eet År i Jerusalem. Hans Moder hed Atalja og var Datter af Kong Omri af Israel.
Ahaziya anali ndi zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Amayi ake anali Ataliya, chidzukulu cha Omiri mfumu ya Israeli.
27 Han vandrede i Akabs Hus's Spor og gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne, ligesom Akabs Hus, thi han var besvogret med Akabs Hus.
Iye anatsatira makhalidwe a banja la Ahabu ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga linachitira banja la Ahabu, pakuti anali mkamwini wa banja la Ahabu.
28 Sammen med Joram, Akabs Søn, drog han i Krig mod Kong Hazael af Aram ved Ramot i Gilead. Men Aramæerne sårede Joram.
Ahaziya anapita pamodzi ndi Yoramu mwana wa Ahabu kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yoramu.
29 Så vendte Kong Joram tilbage for i Jizre'el at søge Helbredelse for de Sår, Aramæerne havde tilføjet ham ved Ramot, da han kæmpede med Kong Hazael af Aram; og Jorams Søn, Kong Ahazja af Juda, drog ned for at se til Joram, Akabs Søn, i Jizre'el, fordi han lå syg.
Choncho mfumu Yoramu inabwerera ku Yezireeli kuti ikachire mabala ake amene Aaramu anamuvulaza ku Rama pa nkhondo yake ndi Hazaeli mfumu ya Aramu. Tsono Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya ku Yuda anapita ku Yezireeli kuti akamuone Yoramu mwana wa Ahabu, popeza nʼkuti akudwala.

< Anden Kongebog 8 >