< Anden Kongebog 5 >
1 Na'aman, Kongen af Arams Hærfører, havde meget at sige hos sin Herre og var højt agtet; thi ved ham havde HERREN givet Aramæerne Sejr; men Manden var spedalsk.
Tsono Naamani anali mtsogoleri wa gulu lankhondo a mfumu ya ku Aramu. Iye anali munthu wodalirika pamaso pa mbuye wake ndipo anali wokondedwa kwambiri, chifukwa kudzera mwa iye Yehova anapambanitsa Aaramu. Anali msilikali wolimba mtima, koma anali ndi khate.
2 Nu havde Aramæerne engang på et Strejtog røvet en lille Pige i Israels Land; hun var kommet i Tjeneste hos Na'amans Hustru,
Tsono magulu a Aaramu anapita ku nkhondo ndipo anakagwira ukapolo mtsikana wamngʼono wa ku Israeli, ndipo ankatumikira mkazi wa Naamani.
3 og hun sagde til sin Frue: "Gid min Herre var hos Profeten i Samaria; han vilde sikkert skille ham af med hans Spedalskhed!"
Mtsikanayo anawuza mkazi wa Naamani kuti, “Mbuye wanga akanapita kukaonana ndi mneneri amene amakhala ku Samariya, akanachiritsidwa khate lawo.”
4 Så kom Na'aman og fortalte sin Herre, hvad Pigen fra Israels Land havde sagt.
Naamani anapita kwa mbuye wake kukamuwuza zomwe mtsikana wochokera ku Israeli ananena.
5 Da sagde Arams Konge: "Rejs derhen! Jeg skal sende etBrevmed til Israels Konge!" Så rejste han og tog ti Talenter Sølv, 6000 Sekel Guld og ti Sæt Festklæder med.
Mfumu ya ku Aramu inayankha kuti, “Iwe uyenera kupita. Ine ndilembera kalata mfumu ya ku Israeli.” Choncho Naamani ananyamuka kupita ku Samariya, atatenga ndalama za siliva 30,000, ndalama zagolide 6,000 ndiponso zovala khumi za pa chikondwerero.
6 Og han overbragte IsraelsKonge Brevet. Deri stod der: "Når dette Brev kommer dig i Hænde, skal du vide, at jeg sender min Tjener Na'aman til dig, for at du skal skille ham af med hans Spedalskhed!"
Kalata imene anapita nayo kwa mfumu ya ku Israeli inali ndi mawu awa: “Taonani, ndikutumiza Naamani mtumiki wanga pamodzi ndi kalatayi kwa inu kuti mumuchiritse khate lake.”
7 Da Israels Konge havde læst Brevet, sønderrev han sine klæder og sagde: "Er jeg Gud, så jeg råder over Liv og Død, siden han skriver til mig, at jeg skal skille en Mand afmed hans Spedalskhed Nej, I kan da se, at han søger Lejlighed til Strid med mig!"
Mfumu ya ku Israeli itangowerenga kalatayo, inangʼamba mkanjo wake ndipo inati, “Kodi ine ndine Mulungu? Kodi ndingathe kupha kapena kupereka moyo? Chifukwa chiyani munthu ameneyu wanditumizira munthu woti ndimuchiritse khate lake? Taonani, iyeyu akungofuna kuti apeze chifukwa choyambanirana nane!”
8 Men da den Guds Mand Elisa hørte, at Israels Konge havde sønderrevet sine klæder, sendte han det Bud til Kongen: "Hvorfor sønderriver du dine Klæder? Lad ham komme til mig, så skal han kende, at der er en Profet i Israel!"
Elisa munthu wa Mulungu atamva kuti mfumu ya ku Israeli yangʼamba mkanjo wake, anatumiza uthenga uwu: “Chifukwa chiyani mwangʼamba mkanjo wanu? Mutumizeni munthuyo kwa ine ndipo iyeyo adzadziwa kuti muli mneneri mu Israeli.”
9 Da kom Na'aman med Heste og Vogne og holdt uden for Døren til Elisas Hus.
Choncho Naamani anapita pamodzi ndi akavalo ake ndi magaleta nakayima pa khomo la nyumba ya Elisa.
10 Elisa sendte et Bud ud til ham og lod sige: "Gå hen og bad dig syv Gange i Jordan, så bliver dit Legeme atter friskt, og du bliver ren!"
Elisa anatumiza uthenga kwa iye woti, “Pita, kasambe kasanu ndi kawiri mu mtsinje wa Yorodani, thupi lako lidzachira ndi kukhalanso monga kale ndipo udzayeretsedwa.”
11 Men Na'aman blev vred og drog bort med de Ord: "Se, jeg havde tænkt, at han vilde komme ud til mig, stå og påkalde HERREN sin Guds Navn og svinge sin Hånd i Retning af Helligdommen og således gøre Ende på Spedalskheden!
Koma Naamani anachoka mokwiya ndipo anati, “Ine ndimaganiza kuti munthuyu atuluka ndipo ayimirira nayitana dzina la Yehova Mulungu wake, nayendetsa dzanja lake pamwamba pa nthendayi ndi kundichiritsa khate langa.
12 Er ikke Damaskus's Floder Abana og Parpar fuldt så gode som alle Israels Vande? Kunde jeg ikke blive ren ved at bade mig i dem?" Og han vendte sig og drog bort i Vrede.
Kodi Abana ndi Faripara, mitsinje ya ku Damasiko, siyoposa mitsinje ina yonse ya ku Israeli? Kodi sindikanasamba mʼmitsinje imeneyo ndi kuyeretsedwa?” Kotero anatembenuka nachoka ali wokwiya kwambiri.
13 Men hans Trælle kom og sagde til ham: "Dersom Profeten havde pålagt dig noget, som var vanskeligt vilde du så ikke have gjort det? Hvor meget mere da nu, da han sagde til dig: Bad dig, så bliver du ren!"
Antchito ake anamuyandikira namufunsa kuti, “Abambo anga, mneneri akanakulamulani chinthu chachikulu, kodi inu simukanachita? Nanga nʼzovuta motani zomwe mneneri wanena kuti ‘Kasambeni ndipo mudzayeretsedwa!’”
14 Så drog han ned og dykkede sig syv Gange i Jordan efter den Guds Mands Ord; og hans Legeme blev atter friskt som et Barns, og han blev ren.
Choncho Naamani anapita ku Yorodani nakadzimiza mʼmadzimo kasanu nʼkawiri, monga momwe munthu wa Mulungu anamuwuzira. Thupi lake linakhalanso monga kale ndipo linakhala losalala ngati la kamnyamata.
15 Så vendte han med hele sit Følge tilbage til den Guds Mand, og da han var kommet derhen, trådtehan frem forham og sagde: "Nu ved jeg, at der ingensteds på Jorden er nogen Gud uden i Israel! Så modtag nu en Takkegave af din Træl!"
Pamenepo Naamani ndi atumiki ake onse anabwerera kwa munthu wa Mulungu uja. Naamani anayima pamaso pa Elisa ndipo anati, “Tsopano ndikudziwa kuti kulibe Mulungu wina pa dziko lonse lapansi koma mu Israeli mokha. Chonde, tsopano landirani mphatso ya mtumiki wanu.”
16 Men han svarede: "Så sandt HERREN lever, for hvis Åsyn jeg står, jeg modtager ikke noget!" Og skønt han nødte ham, vægrede han sig ved at modtage noget.
Mneneri anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene ine ndimamutumikira, sindidzalandira zimenezi.” Ndipo ngakhale Naamani anamukakamiza, iye anakanabe.
17 Da sagde Na'aman: "Så lad da være! Men lad din Træl få så megel Jord, som et Par Muldyr kan bære, thi din Træl vil aldrig mere ofre Brændoffer eller Slagtoffer til nogen anden Gud end HERREN!
Naamani anati, “Ngati inu simulandira, chonde lolani mtumiki wanu kuti atengeko dothi lokwanira kunyamula abulu awiri, popeza mtumiki wanu sadzaperekanso nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa mulungu wina koma Yehova.
18 Men i een Ting vil HERREN nok bære over med din Træl: Når min Herre går ind i Rimmons Hus for at tilbede og støtfer sig til min Arm og jeg så sammen med ham kaster mig til Jorden i Rimmons Hus, da vil HERREN nok bære over ed din Træl i den Ting!"
Koma Yehova andikhululukire ine pa chinthu ichi: Pamene mbuye wanga alowa mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni ine ndimapita naye ndipo ndimakagwada naye limodzi. Pamene ndikugwada mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni, Yehova azikhululukira mtumiki wanu pa chinthu chimenechi.”
19 Han svarede: "Far i Fred!" Men da han var kommet et Stykke hen ad Vejen,
Elisa anati, “Pita mu mtendere.” Choncho anachoka nayenda pangʼono.
20 sagde Gehazi, den Guds Mand Elisas Tjener, ved sig selv: "Der har min Herre ladet denne Aramæer Na'aman slippe og ikke modtaget af ham, hvad han havde med; så sandt HERREN lever, jeg vil løbe efter ham for at få noget af ham!"
Koma Gehazi, mtumiki wa Elisa munthu wa Mulungu, anaganiza mu mtima mwake kuti, “Taonani, mbuye wanga wamulekerera Naamani Mwaramuyu, posalandira zomwe anabweretsa. Pali Yehova wamoyo, ine ndimuthamangira ndipo ndikatengako zinthu kwa iye.”
21 Så satte Gehazi efter Na'aman. og da Na'aman så ham komme løbende efter sig, sprang han af Vognen, gik ham i Møde og spurgte: "Står det godt til?"
Choncho Gehazi anamuthamangira Naamani uja. Naamani ataona Gehazi akumuthamangira, anatsika mʼgaleta lake ndi kukakumana naye. Iye anafunsa Gehazi kuti, “Kodi nʼkwabwino?”
22 Han svarede: "Ja, det står godt til! Min Herre sender mig med det Bud: Der kom lige nu to unge Mænd, som hører til Profetsønnerne, til mig fra Efraims Bjerge: giv dem en Talent Sølv og to Sæt Festklæder!"
Gehazi anayankha kuti, “Inde nʼkwabwino. Mbuye wanga wandituma kuti ndidzakuwuzeni kuti, ‘Anyamata awiri mwa ana a aneneri angondipeza kumene kuchokera ku dziko la mapiri la Efereimu. Chonde apatseniko ndalama za siliva 3,000 ndi zovala ziwiri za pa phwando.’”
23 Da sagde Na'aman: "Tag dog mod to Talenter Sølv!" Og han nødte ham. Så bandt han to Talenter ind i to Punge og tog to Sæt Festklæder og gav to af sine Trælle dem, for at de skulde bære dem foran ham.
Naamani anati, “Kuli bwino utenge ndalama zasiliva 6,000.” Iye anakakamiza Gehazi kuti alandire, ndipo kenaka anamanga matumba awiri a ndalama zasiliva pamodzi ndi zovala zinayi za pa mphwando. Naamani anazipereka kwa antchito ake awiri ndipo anazinyamula nayenda patsogolo pa Gehazi.
24 Men da de kom til Højen, tog han Pengene fra dem, gemte dem i Huset og lod Mændene gå.
Gehazi atafika ku phiri, anawalanda antchito aja zinthu zija nazibisa mʼnyumbamo. Iye anawawuza anthu aja kuti abwerere ndipo anapita.
25 Så gik han ind til sin Herre og trådte hen til ham. Da spurgte Elisa: "Hvor har du været, Gehazi?" Han svarede: "Din Træl har ingen Steder været!"
Kenaka analowa mʼnyumbamo nakayima pamaso pa mbuye wake Elisa. Elisa anafunsa kuti, “Kodi Gehazi unali kuti?” Iye anayankha kuti, “Mtumiki wanu sanapite kwina kulikonse.”
26 Så sagde han til ham: "Gik jeg ikke i Ånden hos dig, da en stod af sin Vogn og gik tilbage for at møde dig? Nu har du fået Penge, og du kan få Klæder, Olivenlunde og Vingårde, Småkvæg og Hornkvæg, Trælle og Trælkvinder,
Koma Elisa anati kwa Gehazi, “Kodi mzimu wanga sunali nawe pamene munthu uja anatsika mʼgaleta lake ndi kukumana nawe? Kodi ino ndi nthawi yolandira ndalama, kapena kulandira zovala, mitengo ya olivi, minda ya mpesa, nkhosa, ngʼombe kapena antchito aamuna kapena antchito aakazi?
27 men Na'amans Spedalskhed skal hænge ved dig og dit Afkom til evig Tid!" Og Gehazi gik fra ham, hvid som Sne af Spedalskhed.
Khate la Naamani lidzakumatirira iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.” Ndipo Gehazi anachoka pamaso pa Elisa ali ndi khate lotuwa ngati phulusa.