< Anden Kongebog 18 >

1 I Elas Søns, Kong Hosea af Israels, tredje Regeringsår blev Ezekias, Akaz's Søn, Konge over Juda.
Mʼchaka chachitatu cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Hezekiya mwana wa Ahazi mfumu ya Yuda analowa ufumu.
2 Han var fem og tyve År gammel, da han blev Konge, og han herskede ni og tyve År i Jerusalem. Hans Moder hed Abi og var en Datter af Zekarja.
Anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Abi, mwana wa Zekariya.
3 Han gjorde, hvad der var ret i HERRENs Øjne, ganske som hans Fader David.
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
4 Han skaffede Offerhøjene bort, sønderbrød Stenstøtterne, omhuggede Asjerastøtten og knuste Kobberslangen, som Moses havde lavet; thi indtil den Tid havde Israeliterne tændt Offerild for den, og man kaldte den Nehusjtan.
Anachotsa malo opembedzerako mafano, anaphwanya miyala yachipembedzo ndiponso anadula mafano a Asera. Iye anaphwanya njoka yamkuwa imene Mose anapanga, pakuti mpaka kufikira nthawi imeneyi Aisraeli amafukiza lubani kwa njoka imeneyi. (Imatchedwa Nehusitani).
5 Til HERREN, Israels Gud, satte han sin Lid, og hverken før eller siden fandtes hans Lige blandt alle Judas Konger.
Hezekiya anadalira Yehova Mulungu wa Israeli. Kotero panalibe wina wofanana naye pakati pa mafumu onse a Yuda, asanakhale mfumu kapena atakhala kale mfumu.
6 Han holdt fast ved HERREN og veg ikke fra ham, og han overholdt de Bud, HERREN havde givet Moses.
Iye anakangamira Yehova ndipo sanamusiye koma anasunga malamulo amene Yehova anapatsa Mose.
7 Og HERREN var med ham; i alt, hvad han tog sig for, havde han Lykken med sig. Han gjorde Oprør mod Assyrerkongen og vilde ikke stå under ham.
Ndipo Yehova anali naye ndipo kulikonse kumene anapita zinthu zinkamuyendera bwino. Iye anagalukira mfumu ya ku Asiriya ndipo sanayitumikirenso.
8 Han slog Filisterne lige til Gaza og dets Omegn, både Vagttårnene og de befæstede Byer.
Iye anakantha Afilisti kuyambira ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa. Anakafika mpaka ku Gaza ndi ku malire ake.
9 I Kong Ezekias's fjerde, Elas Søns, Kong Hosea af Israels, syvende Regeringsår, drog Assyrer kongen Salmanassar op mod Sa maria, belejrede
Mʼchaka chachinayi cha Mfumu Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chiwiri cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Salimenezeri, mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Samariya ndi kuwuzinga
10 og indtog det. Efter tre Års Forløb, i Ezekias's sjette, Kong Hosea af Israels niende Regeringsår, blev Samaria indtaget.
Asiriya analanda mzindawu patatha zaka zitatu. Choncho mzinda wa Samariya unalandidwa chaka chachisanu ndi chimodzi cha Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya mfumu ya Israeli.
11 Og Assyrerkongen førte Israel i Landflygtighed til Assyrien og lod dem bosætte sig i Hala, ved Habor, Gozans Flod, og i Mediens Byer,
Mfumu ya ku Asiriya inatenga Aisraeli kupita nawo ku ukapolo ku Asiriya ndipo anakawakhazika ku Hala, ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
12 til Straf for at de ikke havde adlydt HERREN deres Guds Røst, men overtrådt hans Pagt, alt hvad HERRENs Tjener Moses havde påbudt; de hørte ikke derpå og gjorde ikke derefter.
Izi zinachitika chifukwa sanamvere zonena za Yehova Mulungu wawo, koma anaphwanya pangano lake ndi zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anawalamula. Iwo sanamvere malamulowo kapena kuwagwiritsa ntchito.
13 I Kong Ezekias's fjortende Regeringsår drog Assyrerkongen Sankerib op mod alle Judas befæstede Byer og indtog dem.
Mʼchaka chakhumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, nayilanda.
14 Da sendte Kong Ezekias af Juda Bud til Assyrerkongen i Lakisj og lod sige: "Jeg har forbrudt mig; drag bort fra mig igen! Hvad du pålægger mig, vil jeg tage på mig!" Da pålagde Assyrerkongen Kong Ezekias af Juda at udrede 300 Talenter Sølv og 300 talenter Guld;
Choncho Hezekiya mfumu ya Yuda anatumiza uthenga kwa mfumu ya ku Asiriya ku Lakisi wonena kuti, “Ine ndalakwa. Chokani kuno ndipo ndidzakupatsani chilichonse chimene munene.” Mfumu ya ku Asiriya inalamula mfumu Hezekiya, mfumu ya Yuda, kuti azipereka makilogalamu a siliva okwana 3,000 ndi makilogalamu a golide 1,000.
15 og Ezekias udleverede alt det Sølv, der var i HERRENs Hus og i Skatkamrene i Kongens Palads.
Mfumu Hezekiya inapereka siliva yense amene anapezeka mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba zosungiramo chuma cha mfumu.
16 Ved den Lejlighed plyndrede Ezekias Dørene i HERRENs Helligdom og Pillerne for det Guld, han selv havde overtrukket dem med, og udleverede det til Assyrerkongen.
Nthawi imeneyi Hezekiya mfumu ya Yuda anakanganula golide amene anakuta zitseko ndi mphuthu za chipata cha Nyumba ya Yehova namupereka kwa mfumu ya ku Asiriya.
17 Assyrerkongen sendte så Tartan, Rabsaris og Rabsjake med en anselig Styrke fra Lakisj til Kong Ezekias i Jerusalem, og de drog op og kom til Jerusalem og gjorde Holdt ved Øvredammens Vandledning, ved Vejen til Blegepladsen.
Mfumu ya ku Asiriya inatuma Taritani, Rabusarisi ndi Rabusake pamodzi ndi gulu lalikulu la ankhondo, kwa Mfumu Hezekiya ku Yerusalemu kuchokera ku Lakisi. Iwo anafika ku Yerusalemu nakayima pafupi ndi ngalande ya madzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu waukulu wopita ku malo a Munda wa Mmisiri Wochapa.
18 Da de krævede at få Kongen i Tale, gik Paladsøversten Eljakim, Hilkijas Søn, Statsskriveren Sjebna og Kansleren Joa, Asafs Søn, ud til dem.
Iwo anayitana mfumu, ndipo Eliyakimu mwana wa Hilikiya woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa anthuwo.
19 Rabsjake sagde til dem: "Sig til Ezekias: Således siger Storkongen, Assyrerkongen: Hvad er det for en Fortrøstning, du hengiver dig til?
Ndipo Rabusake anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “‘Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, ‘Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?’
20 Du mener vel, at et blot og bart Ord er det samme som Plan og Styrke i Krig? Og til hvem sætter du egentlig din Lid, siden du gør Oprør imod mig?
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
21 Se nu, du sætter din Lid til Ægypten, denne brudte Rørkæp, som river Sår i Hånden på den, der støtter sig til den! Thi således går det alle dem, der sætter deres Lid til Farao, Ægyptens Konge.
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.’”
22 Men vil I sige til mig: Det er HERREN vor Gud, vi sætter vor Lid til! er det så ikke ham, hvis Offerhøje og Altre Ezekias skaffede bort, da han sagde til Juda og Jerusalem: Foran dette Alter, i Jerusalem skal I tilbede!
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, “Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu.” Kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, “Muzipembedza pa guwa lansembe ili mu Yerusalemu?”
23 Og nu, indgå et Væddemål med min Herre, Assyrerkongen: Jeg giver dig to Gange tusind Heste, hvis du kan stille Ryttere til dem!
“‘Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
24 Hvorledes vil du afslå et Angreb af en eneste Statholder, en af min Herres ringeste Tjenere? Og du sætter din Lid til Ægypten, til Vogne og Heste?
Ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo?
25 Mon det desuden er uden HERRENs Vilje, at jeg er draget op mod dette Sted for at ødelægge det? Det var HERREN selv, der sagde til mig: Drag op mod dette Land og ødelæg det!"
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga malo ano popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.’”
26 Men Eljakim, Hilkijas Søn, Sjebna og Joa sagde til Rabsjake: "Tal dog Aramaisk til dine Trælle, det forstår vi godt; tal ikke Judæisk til os, medens Folkene på Muren hører på det!"
Pamenepo Eliyakimu mwana wa Hilikiya, Sebina ndi Yowa anawuza Rabusakeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
27 Men Habsjake svarede dem: "Er det til din Herre og dig, min Herre har sendt mig med disse Ord? Er det ikke til de Mænd, der sidder på Muren hos eder og æder deres eget Skarn og drikker deres eget Vand!"
Koma Rabusake anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
28 Og Rabsjake trådte hen og råbte med høj Røst på Judæisk: "Hør Storkongens, Assyrerkongens, Ord!
Tsono Rabusake anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
29 Således siger Kongen: Lad ikke Ezekias vildlede eder, thi han er ikke i Stand til at frelse eder af min Hånd!
Zimene mfumu ikunena ndi izi: ‘Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni mʼdzanja langa.
30 Og lad ikke Ezekias forlede eder til at sætte eders Lid til HERREN, når han siger: HERREN skal sikkert frelse os, og denne By skal ikke overgives i Assyrerkongens Hånd!
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
31 Hør ikke på Ezekias; thi således - siger Assyrerkongen: Vil I slutte Fred med mig og overgive eder til mig, så skal enhver af eder spise af sin Vinstok og sit Figentræ og drikke af sin Brønd,
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
32 indtil jeg kommer og tager eder med til et Land, der ligner eders, et Land med Korn og Most, et Land med Brød og Vingårde, et Land med Oliventræer og Honning; så skal I leve og ikke dø. Hør derfor ikke på Ezekias, når han vil forføre eder og siger: HERREN vil frelse os!
mpaka nditabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanuli, dziko la tirigu ndi vinyo watsopano, dziko la chakudya ndi minda ya mipesa, dziko la mitengo ya olivi ndi uchi. Sankhani moyo osati imfa! “Musamvere zonena Hezekiya, pakuti iye akukusocheretsani ponena kuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’
33 Mon nogen af Folkeslagenes Guder har kunnet frelse sit Land af Assyrerkongens Hånd?
Kodi mulungu wa anthu a mtundu wina uliwonse wapulumutsapo dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
34 Hvor er Hamats og Arpads Guder, hvor er Sefarvajims, Henas og Ivvas Guder? Hvor er Landet Samarias Guder? Mon de frelste Samaria af min Hånd?
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu, Hena ndi Ivani? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
35 Hvor er der blandt alle Landes Guder nogen, der har frelst sit Land af min Hånd? Mon da HERREN skulde kunne frelse Jerusalem?"
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja langa? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
36 Men de tav og svarede ham ikke et Ord, thi Kongens Bud lød på, at de ikke måtte svare ham.
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
37 Derpå gik Paladsøversten Eljakim, Hilkijas Søn, Statsskriveren Sjebna og Kansleren Joa, Asafs Søn, med sønderrevne Klæder til Ezekias og meddelte ham, hvad Rabsjake havde sagt.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu, mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza Hezekiya zonse zimene anayankhula Rabusake uja.

< Anden Kongebog 18 >