< Anden Krønikebog 30 >

1 Derpå sendte Ezekias Bud til hele Israel og Juda og skrev desuden Breve til Efraim og Manasse om at komme til HERRENs Hus i Jerusalem for at fejre Påsken for HERREN, Israels Gud.
Hezekiya anatumiza uthenga mʼdziko lonse la Israeli ndi ku Yuda ndiponso analemba makalata ku Efereimu ndi Manase, oyitana anthu kuti abwere ku Nyumba ya Yehova ku Yerusalemu kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli.
2 Og Kongen, hans Øverster og hele Forsamlingen i Jerusalem rådslog om at fejre Påsken i den anden Måned;
Mfumu ndi akuluakulu ake pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu anagwirizana kuti akondwerere Paska pa mwezi wachiwiri.
3 thi de kunde ikke fejre den med det samme, da Præsterne ikke havde helliget sig i tilstrækkeligt Tal, og Folket ikke var samlet i Jerusalem.
Iwo sanathe kukondwerera pa nthawi yake chifukwa si ansembe ambiri amene anadziyeretsa ndiponso anthu anali asanasonkhane mu Yerusalemu.
4 Kongen og hele Forsamlingen fandt det rigtigt;
Chikonzerochi chinaoneka kuti chinali chabwino kwa mfumu pamodzi ndi anthu onse.
5 derfor vedtog de at lade et Opråb udgå i hele Israel fra Be'ersjeba til Dan om at komme og fejre Påsken i Jerusalem for HERREN, Israels Gud, thi man havde ikke fejret den så fuldtalligt som foreskrevet.
Iwo anagwirizana zoti alengeze mu Israeli monse kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani, kuyitana anthu kuti abwere ku Yerusalemu ndi kudzakondwerera Paska wa Yehova, Mulungu wa Israeli. Si ambiri amene ankachita chikondwererochi monga momwe kunalembedwera.
6 Så gik Ilbudene ud i hele Israel og Juda med Breve fra Kongens og hans Øversters Hånd og sagde efter Kongens Befaling: "Israeliter! Vend tilbage til HERREN, Abrahams, Isaks og Israels Gud, at han må vende sig til den Levnin: af eder, der er undsluppet Assyrerkongernes Hånd.
Molamulidwa ndi mfumu, amithenga anapita mu Israeli yense ndi Yuda ndi makalata ochokera kwa mfumu ndi kwa akuluakulu ake, olembedwa kuti, “Aisraeli bwererani kwa Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Israeli, kuti abwerere kwa inu amene mwatsala, amene mwapulumuka mʼdzanja la mafumu a ku Asiriya.
7 Vær ikke som eders Fædre og Brødre, der var troløse mod HERREN, deres Fædres Gud, hvorfor han gjorde dem til Rædsel, som I selv kan se.
Musakhale ngati makolo anu ndi abale anu, amene anali osakhulupirika kwa Yehova Mulungu wa makolo awo kotero kuti anawachititsa kuti akhale chinthu chochititsa mantha, monga mukuoneramu.
8 Vær nu ikke halsstarrige som eders Fædre, men ræk HERREN Hånden og kom til hans Helligdom, som han har helliget til evig Tid, og tjen HERREN eders Gud, at hans glødende Vrede må vende sig fra eder.
Musawumitse khosi monga anachitira makolo anu, Gonjerani Yehova. Bwerani ku malo opatulika, amene anawapatula kwamuyaya. Tumikirani Yehova Mulungu wanu kuti mkwiyo wake ukuchokereni.
9 Thi når I omvender eder til HERREN, skal eders Brødre og Sønner finde Barmhjertighed hos dem, der førte dem bort, og vende tilbage til dette Land. Thi HERREN eders Gud er nådig og barmhjertig og vil ikke vende sit Åsyn fra eder, når l omvender eder til ham!"
Ngati inu mubwerera kwa Yehova, pamenepo abale anu ndi ana anu adzachitiridwa chifundo ndi amene anawagwira ukapolo ndipo adzabwereranso ku dziko lino pakuti Yehova, Mulungu wanu ndi wokoma mtima ndi wachifundo. Iye sadzakufulatirani ngati inuyo mubwerera kwa Iye.”
10 Og Ilbudene gik fra By til By i Efraims og Manasses Land og lige til Zebulon, men man lo dem ud og hånede dem.
Amithenga aja anapita mzinda ndi mzinda wa ku Efereimu ndi Manase mpaka ku Zebuloni, koma anthu anawanyoza ndi kuwachita chipongwe.
11 Dog var der nogle i Aser, Manasse og Zebulon, der ydmygede sig og kom til Jerusalem;
Komabe anthu ena a ku Aseri, Manase ndi Zebuloni anadzichepetsa ndipo anapita ku Yerusalemu.
12 også i Juda virkede Guds Hånd, så at han gav dem et endrægtigt Hjerte til at udføre, hvad Kongen og Øversterne havde påbudt i Kraft af HERRENs Ord.
Dzanja la Mulungu linalinso pa anthu a ku Yuda, kuwapatsa mtima umodzi wochita zimene mfumu ndi akuluakulu ake analamula potsata mawu a Yehova.
13 Så samlede der sig i Jerusalem en Mængde Mennesker for at fejre de usyrede Brøds Højtid i den anden Måned, en vældig Forsamling.
Gulu lalikulu la anthu linasonkhana mu Yerusalemu kudzachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti pa mwezi wachiwiri.
14 De gav sig til at fjerne de Altre, der var i Jerusalem; ligeledes fjernede de alle Røgelsekarrene og kastede dem ned i Kedrons Dal.
Anachotsa mu Yerusalemu maguwa ofukizira lubani ndipo anakawaponya mʼchigwa cha Kidroni.
15 Derpå slagtede de Påskelammet på den fjortende Dag i den anden Måned. Præsterne og Leviterne skammede sig og helligede sig og bragte Brændofre til HERRENs Hus;
Iwo anapha mwana wankhosa wa Paska pa tsiku la 14 la mwezi wachiwiri. Ansembe ndi Alevi anachita manyazi ndipo anadziyeretsa ndi kubweretsa nsembe zopsereza ku Nyumba ya Yehova.
16 og de stillede sig på deres Plads, som deres Pligt var efter den Guds Mand Moses's Lov; Præsterne sprængte Blodet, som de modtog af Leviterne.
Ndipo anakhala mʼmalo awo a nthawi zonse potsatira zolembedwa mʼmalamulo a Mose munthu wa Mulungu. Ansembe anawaza magazi amene anawapatsa Alevi.
17 Thi mange i Forsamlingen havde ikke helliget sig; derfor slagtede Leviterne Påskelammene for alle dem, der ikke var rene, for således at hellige HERREN dem.
Popeza ambiri mʼgululo anali asanadziyeretse, Alevi anapha ana ankhosa a Paska a iwo amene, mwa mwambo, anali osayeretsedwa ndipo sakanatha kupereka ana ankhosa awo kwa Yehova.
18 Thi de flesfe af Folket, især mange fra Efraim, Manasse, Issakar og Zebulon, havde ikke renset sig, men spiste Påskelammet anderledes end foreskrevet. Men Ezekias giki Forbøn for dem og sagde: "HERREN, den gode, tilgive
Ngakhale kuti ambiri mwa anthu ochokera ku Efereimu, Manase, Isakara ndi Zebuloni sanadziyeretse okha, komabe anadya Paska motsutsana ndi zimene zinalembedwa. Koma Hezekiya anawapempherera, kunena kuti, “Yehova wabwino, khululukirani aliyense
19 enhver, som har vendt sit Hjerte til at søge Gud HERREN, hans Fædres Gud, selv om han ikke er ren, som Helligdommen kræver det!"
amene wayika mtima wake kufunafuna Yehova, Mulungu wa makolo ake, ngakhale ali wosayeretsedwa molingana ndi malamulo a malo opatulika.”
20 Og HERREN bønhørte Ezekias og lod Folket uskadt.
Ndipo Yehova anamvera Hezekiya ndipo anachiritsa anthuwo.
21 Så fejrede de Israeliter, der var til Stede i Jerusalem, de usyrede Brøds Højtid med stor Glæde i syv Dage; og Leviterne og Præsterne sang af alle Kræfter dagligt Lovsange for HERREN.
Aisraeli amene anali mu Yerusalemu anachita chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti kwa masiku asanu ndi awiri akusangalala kwambiri, pamene Alevi ndi ansembe amayimbira Yehova tsiku lililonse, akuyimbira zida zamatamando za Yehova.
22 Og Ezekias talte venlige Ord til alle de Leviter, der havde udvist særlig Dygtighed i HERRENs Tjeneste; og de fejrede Højtiden til Ende de syv Dage, idet de ofrede Takofre og lovpriste HERREN, deres Pædres Gud.
Hezekiya anayankhula molimbikitsa Alevi onse amene anaonetsa kumvetsa bwino za kutumikira Yehova. Kwa masiku asanu ndi awiri anadya gawo lawo ndi kupereka nsembe zachiyanjano ndi kutamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo.
23 Men derefter vedtog hele Forsamlingen at holde Højtid syv Dage til, og det gjorde de så med Glæde,
Ndipo msonkhano wonse unagwirizana zopitiriza chikondwerero kwa masiku ena asanu ndi awiri. Kotero kwa masiku ena asanu ndi awiri anachita chikondwererocho mosangalala.
24 thi Kong Ezekias af Juda gav Forsamlingen en Ydelse af 1.000 Tyre og 7.000 Stykker Småkvæg, og Øversterne gav Forsamlingen 1.000 Tyre og 10.000 Stykker Småkvæg; og en Mængde Præster helligede sig.
Hezekiya mfumu ya Yuda anapereka ngʼombe zamphongo 1,000 ndi nkhosa ndi mbuzi 7,000 ku msonkhanoko ndipo akuluakulu ake anapereka ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa ndi mbuzi 10,000. Ansembe ambiri anadziyeretsa.
25 Da frydede hele Judas Forsamling sig, ligeledes Præsterne og Leviterne og hele den Forsamling, der var kommet fra Israel, og de fremmede, der var kommet fra Israels Land eller boede i Juda;
Gulu lonse la ku Yuda linasangalala, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ndi onse amene anasonkhana ochokera ku Israeli, kuphatikizanso alendo amene anachokera ku Israeli ndi amene amakhala ku Yuda.
26 og der var stor Glæde i Jerusalem, thi siden Davids Søns, Kong Salomo af Israels, Dage var sligt ikke sket i Jerusalem;
Munali chikondwerero chachikulu mu Yerusalemu, pakuti kuyambira masiku a Solomoni mwana wa Davide mfumu ya Israeli sizinachitikepo zotere mu Yerusalemu.
27 og Præsterne og Leviterne stod op og velsignede Folket, og deres Røst hørtes, og deres Bøn nåede Himmelen, hans hellige Bolig.
Ansembe ndi Alevi anayimirira kudalitsa anthu, ndipo Mulungu anawamvera pakuti pemphero lawo linafika kumwamba, malo ake oyera.

< Anden Krønikebog 30 >