< Anden Krønikebog 20 >
1 Siden hændte det sig, at Moabiterne og ammoniterne sammen med Folk fra Maon drog i Krig mod Josafat.
Zitatha izi, Amowabu ndi Aamoni pamodzi ndi Ameuni ena anabwera kudzachita nkhondo ndi Yehosafati.
2 Og man kom og bragte Josafat den Efterretning: "En vældig Menneskemængde rykker frem imod dig fra Egnene binsides Havet), fra Edom, og de står allerede i Hazazon-Tamar (det er En-Gedi)!"
Anthu ena anabwera kudzamuwuza Yehosafati kuti, “Gulu lalikulu kwambiri lankhondo likubwera kudzachita nanu nkhondo lochokera ku Edomu, ku mbali ina ya Nyanja. Gululi lafika kale ku Hazazoni Tamara” (ndiye kuti Eni-Gedi).
3 Da grebes Josafat af Frygt, og han vendte sig til HERREN og søgte ham og lod en Faste udråbe i bele Juda.
Ndi mantha, Yehosafati anaganiza zofunsira kwa Yehova, ndipo analengeza kuti Ayuda onse asale zakudya.
4 Så samledes Judæerne for at søge Hjælp hos HERREN; også fra alle Judas Byer kom de for at søge HERREN.
Anthu a ku Yuda anabwera pamodzi kudzafuna thandizo kwa Yehova, ndipo anabweradi kuchokera ku mzinda uliwonse wa mu Yuda kudzafunafuna Yehova.
5 Men Josafat trådte frem i Judas og Jerusalems Forsamling i HERRENs Hus foran den nye Forgård
Yehosafati anayimirira pakati pa msonkhano wa Yuda ndi Yerusalemu, pa Nyumba ya Yehova patsogolo pa bwalo latsopano
6 og sagde: "HERRE, vore Fædres Gud! Er du ikke Gud i Himmelen, er det ikke dig, der hersker over alle Hedningerigerne? I din Hånd er Kraft og Styrke, og mod dig kan ingen holde Stand!
ndipo anati: “Inu Yehova, Mulungu wa makolo athu, kodi Inu sindinu Mulungu amene muli kumwamba? Inu mumalamulira maufumu onse a mitundu ya anthu. Mphamvu ndi nyonga zili mʼmanja mwanu, ndipo palibe amene angalimbane nanu.
7 Var det ikke dig, vor Gud, der drev dette Lands Indbyggere bort foran dit Folk Israel og gav din Ven Abrahams Efterkommere det for evigt?
Inu Mulungu wathu, kodi simunathamangitse nzika za dziko lino pamaso pa anthu anu Aisraeli ndipo munalipereka kwa zidzukulu za Abrahamu bwenzi lanu kwamuyaya?
8 Og de bosatte sig der og byggede dig der en Helligdom for dit Navn, idet de sagde:
Iwo akhala mʼdzikolo ndipo anamangira Dzina lanu malo opatulika, nʼkumati,
9 Hvis Ulykke rammer os, Sværd, Straffedom, Pest eller Hungersnød, vil vi træde frem foran dette Hus og for dit Åsyn, thi dit Navn bor i dette Hus, og råbe til dig om Hjælp i vor Nød, og du vil høre det og frelse os!
‘Ngati tsoka litigwera kaya ndi lupanga lachiweruzo, kapena mliri, kapenanso njala, ife tidzayima pamaso panu patsogolo pa Nyumba ya Mulungu ino imene imatchedwa ndi Dzina lanu ndipo tidzalirira kwa inu mʼmasautso athu, ndipo Inu mudzatimvera ndi kutipulumutsa.’
10 Se nu, hvorledes Ammoniterne og Moabiterne og de fra Se'irs Bjerge, hvem du ikke tillod Israeliterne at angribe, da de kom fra Ægypten, tværtimod holdt de sig tilbage fra dem og tilintetgjorde dem ikke,
“Koma tsopano pano pali anthu ochokera ku Amoni, Mowabu ndi Phiri la Seiri amene dziko lawo Inu simunawalole Aisraeli kuti alithire nkhondo pamene amabwera kuchokera ku Igupto. Kotero anatembenuka ndi kuwaleka ndipo sanawawononge.
11 se nu, hvorledes de gengælder os det med at komme for at drive os bort fra din Ejendom, som du gav os i Eje!
Taonani, mmene akutibwezera ife pobwera kudzatithamangitsa mʼdziko limene inu munatipatsa ngati cholowa chathu.
12 Vor Gud, vil du ikke holde Dom over dem? Thi vi er afmægtige over for denne vældige Menneskemængde, som kommer over os; vi ved ikke, hvad vi skal gøre, men vore Øjne er vendt til dig!"
Inu Mulungu wathu, kodi simuwaweruza? Pakuti ife tilibe mphamvu zolimbana ndi gulu lalikulu lankhondo limene likutithira nkhondoli. Ife sitikudziwa choti tichite, koma maso athu ali pa Inu.”
13 Medens nu alle Judæerne stod for HERRENs Åsyn med deres Familier, Kvinder og Børn,
Anthu onse a Yuda, pamodzi ndi akazi awo ndi ana ndi makanda, anayima chilili pamaso pa Yehova.
14 kom HERRENs Ånd midt i Forsamlingen over Leviten Jahaziel, en Søn af Zekarja, en Søn af Benaja, en Søn af Je'iel, en Søn af Mattanja, af Asafs Sønner,
Ndipo Mzimu wa Yehova unabwera pa Yahazieli mwana wa Zekariya, mwana wa Benaya, mwana wa Yeiyeli, mwana wa Mataniya Mlevi, chidzukulu cha Asafu, atayimirira mu msonkhano.
15 og han sagde: "Lyt til, alle I Judæere, Jerusalems Indbyggere og Kong Josafat! Så siger HERREN til eder: Frygt ikke og forfærdes ikke for denne vældige Menneskemængde, thi Kampen er ikke eders, men Guds!
Iye anati, “Tamverani mfumu Yehosafati ndi onse amene amakhala mu Yuda ndi Yerusalemu! Zimene Yehova akunena kwa inu ndi izi: ‘Musaope kapena kutaya mtima chifukwa cha gulu lalikulu lankhondo ili. Pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.
16 Drag i Morgen ned imod dem; se, de er ved at stige op ad Vejen ved Hazziz, og l vil træffe dem ved Enden af Dalen østen for Jeruels Ørken.
Mawa mupite mukamenyane nawo. Adzakhala akubwera mokweza kudzera Njira ya Zizi, ndipo mukawapeza kumapeto kwa chigwa cha ku chipululu cha Yeruweli.
17 Det er ikke eder, der skal kæmpe her; stil eder op og bliv stående, så skal I se, hvorledes HERREN frelser eder, I Judæere og Jerusalems Indbyggere! Frygt ikke og forfærdes ikke, men drag i Morgen imod dem, og HERREN vil være med eder!"
Sikudzafunika kuti Inu mumenyane nawo pa nkhondo imeneyi. Inu mukhale pa malo anu; imani molimba ndipo onani chipulumutso chimene Yehova adzakupatsani, Inu Yuda ndi Yerusalemu. Musaope, musataye mtima. Pitani kuti mukakumane nawo mawa, ndipo Yehova adzakhala nanu.’”
18 Da bøjede Josafat sig med Ansigtet til Jorden, og alle Judæerne og Jerusalems Indbyggere faldt ned for HERREN og tilbad ham;
Yehosafati anaweramitsa nkhope yake ndi kugunda pansi, ndiponso anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anagwa pansi ndi kulambira Yehova.
19 men Leviterne af Keh'atiternes og Koraiternes Sønner stod op for at lovprise HERREN, Israels Gud, med vældig Røst.
Kenaka Alevi ena ochokera ku mabanja a Kohati ndi Kora anayimirira ndipo anatamanda Yehova Mulungu wa Israeli ndi mawu ofuwula kwambiri.
20 Tidligt næste Morgen drog de ud til Tekoas Ørken; og medens de drog ud, stod Josafat og sagde: "Hør mig, I Judæere og Jerusalems Indbyggere! Tro på HERREN eders Gud, og l skal blive boende, tro på hans Profeter, og Lykken skal følge eder!"
Mmamawa, ananyamuka kupita ku chipululu cha Tekowa. Akunyamuka, Yehosafati anayimirira ndipo anati, “Tandimverani ine anthu a Yuda ndi Yerusalemu! Khalani ndi chikhulupiriro mwa Yehova Mulungu wanu ndipo mudzatchinjirizidwa, khalani ndi chikhulupiriro mwa aneneri ake ndipo mudzapambana.”
21 Og efter at have rådført sig med Folket opstillede han Sangere til med Ordene "lov HERREN, thi hans Miskundhed varer evindelig!" at lovprise HERREN i helligt Skrud, medens de drog frem foran de væbnede.
Atafunsira kwa anthu, Yehosafati anasankha anthu oti ayimbire Yehova ndi kumutamanda chifukwa cha ulemerero wa chiyero chake pamene amapita ali patsogolo pa gulu la ankhondo, akunena kuti: “Yamikani Yehova pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
22 Og i samme Stund de begyndte med Jubelråb og Lovsang, lod HERREN et Baghold komme over Ammoniterne, Moabiterne og dem fra Se'irs Bjerge, der rykkede frem mod Juda, så de blev slået.
Atangoyamba kuyimba ndi kutamanda, Yehova anapereka mʼmanja mwawo anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu ndiponso a ku Phiri la Seiri amene amalimbana ndi Yuda, ndipo anagonjetsedwa.
23 Ammoniterne og Moabiterne angreb dem, der boede i Se'irs Bjerge, og lagde Band på dem og tilintetgjorde dem, og da de var færdige med dem fra Se'ir, gav de sig til at udrydde hverandre.
Anthu a ku Amoni ndi a ku Mowabu anawukira anthu ochokera ku Phiri la Seiri, ndipo anawawononga ndi kuwatheratu. Atatsiriza kuwapha anthu ochokera ku Seiri anamenyana wina ndi mnzake mpaka kuwonongana.
24 Da så Judæerne kom op på Varden, hvorfra man ser ud over Ørkenen, og vendte Blikket mod Menneskemængden, se, da lå deres døde Kroppe på Jorden, ingen var undsluppet.
Anthu a ku Yuda atafika pa malo oyangʼanana ndi chipululu ndi kuona kumene kunali gulu lalikulu lankhondo, iwo anangoona mitembo yokhayokha itagona pansi ndipo palibe amene anathawa.
25 Så kom Josafat og hans Folk hen for at udplyndre dem, og de fandt en Mængde Kvæg, Gods, Klæder og kostbare Ting. De røvede så meget, at de ikke kunde slæbe det bort, og brugte tre Dage til at plyndre; så meget var der.
Choncho Yehosafati ndi anthu ake anapita kukafunkha, ndipo pakati pawo anapeza katundu wambiri ndi zovala ndiponso zinthu zina zamtengowapatali kuposa zomwe akanatha kunyamula. Kunali katundu wambiri kotero kuti zinawatengera masiku atatu kuti amutenge.
26 Den fjerde Dag samledes de i Berakadalen, thi der lovpriste de HERREN, og derfor kaldte man Stedet Berakadalen, som det hedder den Dag i Dag.
Tsiku lachinayi anasonkhana ku chigwa cha Beraka kumene anatamanda Yehova. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Beraka mpaka lero.
27 Derpå vendte alle Folkene fra Juda og Jerusalem med Josafat i Spidsen om og drog tilbage til Jerusalem med Glæde, thi HERREN havde bragt dem Glæde over deres Fjender;
Tsono motsogozedwa ndi Yehosafati, anthu onse a Yuda ndi Yerusalemu anabwerera ku Yerusalemu mokondwera pakuti Yehova anawagonjetsera adani awo.
28 og med Harper, Citre og Trompeter kom de lil Jerusalem, til HERRENs Hus.
Iwo analowa mu Yerusalemu ndipo anapita ku Nyumba ya Mulungu akuyimba azeze, apangwe ndi malipenga.
29 Men en Guds Rædsel kom over alle Lande og Riger, da de hørte, at HERREN havde kæmpet mod Israels Fjender.
Kuopsa kwa Mulungu kunali pa maufumu onse a mayiko amene anamva mmene Yehova anamenyera adani a Aisraeli.
30 Således fik Josafats Rige Fred, og hans Gud skaffede ham Ro til alle Sider.
Ndipo ufumu wa Yehosafati unali pa mtendere pakuti Mulungu wake anamupatsa mpumulo ku mbali zonse.
31 Josafat var fem og tredive År gammel, da han blev Konge over Juda, og han herskede fem og tyve År i Jerusalem. Hans Moder hed Azuba og var Datter af Sjilhi.
Choncho Yehosafati analamulira Yuda. Iye anali wa zaka 35 pamene anakhala mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 25. Dzina la amayi ake linali Azuba mwana wa Sili.
32 Han vandrede i sin Fader Asas Spor og veg ikke derfra, idet han gjorde, hvad der var ret i HERRENs Øjne.
Iye ankayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanapatuke pa zimenezi pakuti anachita zolungama pamaso pa Yehova.
33 Kun blev Offerhøjene ikke fjernet, og Folket vendte endnu ikke Hjertet til deres Fædres Gud.
Komabe malo opembedzerapo mafano sanachotsedwe ndipo anthu sanaperekebe mitima yawo kwa Mulungu wa makolo awo.
34 Hvad der ellers er at fortælle om Josafaf fra først til sidst, står jo optegnet i Jehus, Hananis Søns, Krønike, som er optaget i Bogen om Israels Konger.
Zochitika zina zokhudza ufumu wa Yehosafati, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la Yehu mwana wa Hanani, zomwe zikupezeka mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
35 Senere slog Kong Josafat af Juda sig sammen med Kong Ahazja af Israel, der var ugudelig i al sin Færd;
Zitapita izi, Yehosafati mfumu ya Yuda inachita mgwirizano ndi Ahaziya mfumu ya Israeli, amene anachita zoyipa kwambiri.
36 han slog sig sammen med ham om at bygge Skibe, der skulde sejle til Tarsis. De byggede Skibe i Ezjongeber.
Iye anagwirizana ndi Ahaziya kuti apange sitima zapamadzi zochitira malonda. Atazipanga zimenezi ku Ezioni-Geberi,
37 Men Eliezer, Dodavahus Søn, fra Maresja profeterede mod Josafat og sagde: "Fordi du har slået dig sammen med Ahazja, vil HERREN gøre dit Værk til intet!" Og Skibene gik under og nåede ikke Tarsis.
Eliezara mwana wa Dodavahu wa ku Maresa ananenera motsutsana ndi Yehosafati ndipo anati, “Chifukwa chakuti wachita mgwirizano ndi Ahaziya, Yehova adzawononga zimene mwapangazo!” Sitima za pamadzizo zinawonongeka ndipo sizinapite nʼkomwe kumene zimakachita malonda.