< Anden Krønikebog 12 >
1 Men da Rehabeams Kongedømme var grundfæstet og hans Magt styrket, forlod han tillige med hele Israel HERRENs Lov.
Rehobowamu atakhazikika monga mfumu nakhaladi wamphamvu, iyeyo pamodzi ndi Aisraeli onse anasiya malamulo a Yehova.
2 Da drog i Kong Rehabeams femte Regeringsår Ægypterkongen Sjisjak op imod Jerusalem, fordi de havde været troløse mod HERREN,
Chifukwa anakhala osakhulupirika pamaso pa Yehova, Sisaki mfumu ya dziko la Igupto inathira nkhondo Yerusalemu mʼchaka chachisanu cha mfumu Rehobowamu.
3 med 1200 Stridsvogne og 60.000 Ryttere, og der var ikke Tal på Krigerne, der drog med ham fra Ægypten, Libyere, Sukkijiter og Ætiopere;
Sisakiyo anabwera ndi magaleta 1,200 ndi anthu okwera akavalo 60,000 ndiponso asilikali osawerengeka ochokera ku Libiya, Suki ndi Kusi amene anabwera naye kuchokera ku Igupto.
4 og efter at have indtaget Fæstningerne i Juda drog han mod Jerusalem.
Iye analanda mizinda yotetezedwa ya Yuda ndipo anafika mpaka ku Yerusalemu.
5 Da kom Profeten Sjemaja til Rehabeam og Judas Øverster, som var tyet sammen i Jerusalem for Sjisjak, og sagde til dem: "Så siger HERREN: I har forladt mig, derfor har jeg også forladt eder og givet eder i Sjisjaks Hånd!"
Ndipo mneneri Semaya anabwera kwa Rehobowamu ndi kwa atsogoleri a Yuda amene anasonkhana mu Yerusalemu chifukwa cha Sisaki ndipo iye anawawuza kuti, “Yehova akuti, ‘Inu mwandisiya, choncho Inenso ndakusiyani ndi kukuperekani kwa Sisaki.’”
6 Da ydmygede Israels Øverster og Kongen sig og sagde: "HERREN er retfærdig!"
Atsogoleri a Israeli pamodzi ndi mfumu anadzichepetsa nati, “Yehova ndi wolungama.”
7 Og da HERREN så, at de havde ydmyget sig, kom HERRENs Ord til Sjemaja således: "De har ydmyget sig; derfor vil jeg ikke tilintetgøre dem, men frelse dem om ikke længe, og min Vrede skal ikke udgydes over Jerusalem ved Sjisjak;
Yehova ataona kuti adzichepetsa, anayankhula ndi Semaya kuti, “Pakuti adzichepetsa, Ine sindiwawononga koma posachedwapa ndiwapulumutsa. Sinditsanulira ukali wanga pa Yerusalemu kudzera mwa Sisaki.
8 men de skal komme til at stå under ham og lære at kende Forskellen mellem at tjene mig og at tjene Hedningemagterne!"
Komabe iwo adzakhala pansi pa ulamuliro wake, kuti aphunzire kudziwa kusiyanitsa pakati pa kutumikira Ine ndi kutumikira mafumu a mayiko ena.”
9 Så drog Sjisjak op mod Jerusalem og tog Skattene i HERRENs Hus og i Kongens Palads; alt tog han, også de Guldskjolde, Salomo havde ladet lave.
Sisaki mfumu ya dziko la Igupto atathira nkhondo Yerusalemu, iye anatenga chuma cha mʼNyumba ya Yehova ndi chuma cha mʼnyumba yaufumu. Iye anatenga zinthu zonse kuphatikizapo zishango zagolide zimene Solomoni anapanga.
10 Kong Rehabeam lod da i Stedet lave Kobberskjolde og gav dem i Forvaring hos Høvedsmændene for Livvagten, der holdt Vagt ved Indgangen til Kongens Palads;
Ndipo mfumu inapereka zishango zamkuwa kwa oyangʼanira mʼmalo mwake ndipo iwo anazipereka kwa oyangʼanira alonda amene amayangʼanira pa chipata cha nyumba yaufumu.
11 og hver Gang Kongen begav sig til HERRENs Hus, kom Livvagten og hentede dem, og bagefter bragte de dem tilbage til Vagtstuen.
Nthawi ina iliyonse imene mfumu ikupita ku Nyumba ya Yehova, alonda amapita nayo atanyamula zishango, ndipo kenaka amakazibwezera ku chipinda cha alonda.
12 Men da han havde ydmyget sig, vendfe HERRENs Vrede sig fra ham, så han ikke helt tilintetgjorde ham; også i Juda var Forholdene gode.
Pakuti mfumu Rehobowamu inadzichepetsa, mkwiyo wa Yehova unamuchokera, sanawonongedweretu. Kunena zoona, munali zinthu zina zabwino mu Yuda.
13 Således styrkede Kong Rehabeam sin Magt i Jerusalem og blev ved at herske; thi Rehabeam var een og fyrretyve År gammel, da han blev Konge, og han herskede sytten År i Jerusalem, den By, HERREN havde udvalgt af alle Israels Stammer for der at stedfæste sit Navn. Hans Moder var en ammonitisk Kvinde ved Navn Na'ama.
Mfumu Rehobowamu anayika maziko a ufumu wake mwamphamvu mu Yerusalemu ndipo anapitirira kukhala mfumu. Iye anali ndi zaka 41 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira zaka 17 mu Yerusalemu, mzinda wa Yehova umene anasankha pakati pa mafuko a Aisraeli mmene Yehova anakhazikikamo. Dzina la amayi ake linali Naama, amene anali Mwamoni.
14 Han gjorde, hvad der var ondt, thi hans Hjerte var ikke vendt til at søge HERREN.
Rehobowamu anachita zoyipa chifuwa mtima wake sunafunefune Yehova.
15 Rehabeams Historie fra først til sidst står jo optegnet i Profeten Sjemajas og Seeren tddos Krønike. Rehabeam og Jeroboam lå i Krig med hinanden hele Tiden.
Ntchito za Rehobowamu, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri la mneneri Semaya ndi mlosi Ido amene amalemba mbiri? Panali nkhondo yosatha pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
16 Så lagde Rehabeam sig til Hvile hos sine Fædre og blev jordet i Davidsbyen. Og hans Søn Abija blev Konge i hans Sted.
Rehobowamu anamwalira, ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Ndipo mwana wake Abiya analowa ufumu mʼmalo wake.