< 1 Samuel 13 >

1 Saul var....År ved sin Tronbestigelse, og han herskede i....År over Israel.
Sauli analowa ufumu ali ndi zaka makumi atatu, ndipo analamulira Israeli kwa zaka 42.
2 Saul udvalgte sig 3000 Mand af Israel; af dem var 2000 hos Saul i Mikmas og i Bjergene ved Betel, 1000 hos Jonatan i Gibea i Benjamin; Resten af Krigerne lod han gå hver til sit.
Nthawi ina Sauli anasankha Aisraeli 3,000. Mwa iwowa, 2,000 anali ndi Sauliyo ku Mikimasi ndi ku dziko la mapiri ku Beteli, ndipo 1,000 anali ndi Yonatani ku Gibeya ku Benjamini. Anthu ena onse otsala anawabweza kwawo.
3 Da fældede Jonatan Filisternes Foged i Geba. Det kom nu Filisterne for Øre, at Hebræerne havde revet sig løs. Men Saul havde ladet støde i Hornet hele Landet over,
Yonatani anakantha mkulu wa ankhondo wa Afilisti ku Geba, ndipo Afilisti anamva kuti Aheberi awukira. Tsono Sauli anawuza amithenga kuti alize lipenga mʼdziko lonse la Israeli.
4 og hele Israel hørte, at Saul havde fældet Filisternes Foged, og at Israel havde vakt Filisternes Vrede. Og Folket stævnedes sammen i Gilgal til at følge Saul,
Choncho Aisraeli onse anamva kuti Sauli wakantha mkulu wa ankhondo Wachifilisiti ndi kuti Afilisti anayipidwa nawo Aisraeli. Ndiye anthu anayitanidwa kuti abwere kwa Sauli ku Giligala.
5 men Filisterne havde samlet sig til Kamp mod Israel, 3000 Stridsvogne, 6000 Ryttere og Fodfolk så talrigt som Sandet ved Havets Bred, og de drog op og lejrede sig i Mikmas lige over for Bet-Aven.
Tsono Afilisti anasonkhana kuti amenyane ndi Aisraeli. Iwo anali ndi magaleta 3,000, okwera pa akavalo 2,000 ndiponso asilikali kuchuluka kwake ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Iwo anapita ndi kukamanga misasa yawo ku Mikimasi, kummawa kwa Beti-Aveni.
6 Da Israels Mænd skønnede, hvilken Fare de var i thi Folket blev trængt, skjulte Folket sig i Huler, Jordhuller, Klipperevner, Gruber og Cisterner
Pamene Aisraeli anaona kuti anali pamavuto akulu, poti anali atapanikizidwa kwambiri, anabisala mʼmapanga, mʼmaenje, mʼmatanthwe, mʼmakwalala ndi mʼzitsime.
7 eller gik over Jordans Vadesteder til Gads og Gileads Land. Men Saul var endnu i Gilgal, og hele Folket fulgte ham med Frygt i Sind.
Ahebri ena anawoloka Yorodani mpaka kukafika ku dziko la Gadi ndi ku Giliyadi. Koma Sauli anakhalabe ku Giligala ndipo ankhondo onse amene anali naye anali njenjenje ndi mantha.
8 Han ventede syv Dage til den Tid, Samuel havde fastsat; men Samuel kom ikke til Gilgal. Da Folket så spredte sig og forlod Saul,
Saulo anadikirira masiku asanu ndi awiri, monga mwa nthawi imene ananena Samueli. Koma Samueli sanabwere ku Giligala, ndipo anthu anayamba kumuthawa Sauli uja.
9 sagde han: "Bring Brændofferet og Takofrene hen til mig!" Så ofrede han Brændofferet.
Kotero iye anati, “Bwera nayoni nsembe yopsereza ndi nsembe ya chiyanjano.” Ndipo Sauli anapereka nsembe yopsereza.
10 Men lige som han var færdig med at ofre Brændofferet, se, da kom Samuel, og Saul gik ham i Møde for at hilse på ham.
Atangomaliza kupereka nsembe, anangoona Samueli watulukira ndipo Sauli anapita kukamulonjera.
11 Da sagde Samuel: "Hvad har du gjort!" Saul svarede: "Jeg så, at Folket spredte sig og forlod mig, men du kom ikke til den fastsatte Tid, og Filisterne samlede sig ved Mikmas;
Samueli anafunsa kuti, “Nʼchiyani chimene wachita?” Sauli anayankha kuti, “Nditaona kuti anthu ayamba kundithawa, ndi kuti inu simunabwere pa nthawi munanena ija, ndiponso kuti Afilisti akusonkhana ku Mikimasi,
12 så tænkte jeg: Nu drager Filisterne ned til Gilgal imod mig, og jeg har endnu ikke vundet HERRENs Gunst; da tog jeg Mod til mig og bragte Brændofferet!"
ndinati, ‘Tsopano Afilisti abwera kudzandithira nkhondo ku Giligala kuno, chonsecho sindinapemphe Yehova kuti andikomere mtima.’ Motero ndinakakamizika kupereka nsembe yopsereza.”
13 Samuel sagde til Saul: "Tåbeligt har du handlet. Hvis du havde holdt den Befaling, HERREN din Gud gav dig, vilde HERREN nu have grundfæstet dit Kongedømme over Israel til evig Tid;
Samueli anati, “Mwachita zopusa. Simunatsate zimene Yehova Mulungu wanu anakulamulani kuti muchite. Mukanazitsata, Yehova akanawukhazikitsa ufumu wanu mu Israeli mpaka kalekale.
14 men nu skal dit Kongedømme ikke bestå. HERREN har udsøgt sig en Mand efter sit Hjerte, og ham har HERREN kaldet til Fyrste over sit Folk, fordi du ikke holdt, hvad HERREN bød dig!"
Koma tsopano ufumu wanu sudzakhalitsa. Yehova wapeza munthu wapamtima pake ndipo wamusankha kukhala mtsogoleri wa anthu ake chifukwa inu simunasunge malamulo a Yehova.”
15 Derpå brød Samuel op og gik bort fra Gilgal; men den tilbageblevne Del af Folket drog op i Følge med Saul for at støde til Krigerne, og de kom fra Gilgal til Gibea i Benjamin. Da mønstrede Saul de Folk, han havde hos sig, omtrent 600 Mand;
Kenaka Samueli anachoka ku Giligala ndi kupita ku Gibeyati ku dziko la Benjamini. Saulo anawerenga anthu amene anali naye ndipo analipo 600.
16 og Saul og hans Søn Jonatan og de Folk, de havde hos sig, lå i Geba i Benjamin, medens Filisterne lå lejret i Mikmas.
Sauli ndi mwana wake Yonatani pamodzi ndi asilikali amene anali naye aja amakhala ku Geba ku dziko la Benjamini. Koma Afilisti anamanga misasa yawo ku Mikimasi.
17 Fra Filisternes Lejr drog så en Skare ud i tre Afdelinger for at plyndre; den ene Afdeling drog i Retning af Ofra til Sjualegnen,
Ankhondo a Afilisti anatuluka mʼmisasa yawo mʼmagulu atatu. Gulu lina linapita ku Ofiri ku dziko la Suwala.
18 den anden i Retning af Bet Horon og den tredje i Retning af den Høj, som rager op over Zeboimdalen, ad Ørkenen til.
Gulu lina linalunjika ku Beti-Horoni, ndipo gulu lachitatu linalunjika ku malire oyangʼanana ndi chigwa cha Zeboimu cha ku chipululu.
19 Men der fandtes ingen Smede i hele Israels Land; thi Filisterne havde tænkt, at Hebræerne ellers kunde lave sig Sværd og Spyd;
Nthawi imeneyo nʼkuti mulibe osula zitsulo mʼdziko lonse la Israeli, pakuti Afilisti anati, “Tisawalole Aheberi kudzipangira okha malupanga kapena mikondo!”
20 derfor måtte hele Israel drage ned til Filisterne for at få hvæsset deres Plovjern, Hakker, Økser eller Pigkæppe;
Kotero Aisraeli onse amapita kwa Afilisti kukanoletsa mapulawo, makasu, nkhwangwa ndi zikwakwa zawo.
21 det kostede en Pim at få slebet Plovjem og Hakker og en Tredjedel Sekel for Økser og for at indsætte Pig.
Mtengo wonolera mapulawo ndi makasu unali zigawo ziwiri za sekeli, mtengo wonolera zisonga ndi nkhwangwa unali gawo limodzi la Sekeli.
22 Således fandtes der, den Dag Slaget stod ved Mikmas, hverken Sværd eller Spyd hos nogen af Krigerne, som var hos Saul og Jonatan; kun Saul og hans Søn Jonatan havde Våben.
Motero tsiku la nkhondolo panalibe lupanga kapena mkondo mʼdzanja la aliyense amene anatsatira Saulo ndi Yonatani. Koma Saulo ndi Yonatani, iwo okha ndiwo anali ndi zida.
23 Filisternes Forpost rykkede frem til Mikmaspasset.
Tsono gulu lina lankhondo la Chifilisti linapita kukalonda mpata wa Mikimasi.

< 1 Samuel 13 >