< 1 Samuel 11 >
1 Siden efter drog Ammoniten Nahasj op og belejrede Jabesj i Gilead. Da sagde alle Mændene i Jabesj til Nahasj: "Slut Pagt med os, så vil vi underkaste os!"
Nahasi, Mwamoni anapita ndi kuzungulira mzinda wa Yabesi Giliyadi. Tsono anthu onse a ku Yabesi anapempha Nahasiyo kuti, “Muchite nafe pangano, ndipo tidzakutumikirani.”
2 Men Ammoniten Nahasj svarede: "Ja, på det Vilkår vil jeg slutte Pagt med eder, at jeg må stikke det højre Øje ud på enhver af eder til Forsmædelse for hele Israel!"
Koma Nahasi Mwamoni uja anayankha kuti, “Ndidzachita nanu pangano pokhapokha nditakolowola diso lakumanja la aliyense wa inu kuti ndichititse manyazi Aisraeli onse.”
3 Da sagde de Ældste i Jabesj til ham: "Giv os syv Dages Frist, så vi kan sende Bud rundt i hele Israels Land; hvis så ingen kommer os til Hjælp, vil vi overgive os til dig!"
Akuluakulu a mzinda wa Yabesi anati kwa iye, “Utipatse masiku asanu ndi awiri kuti titumize uthenga mu Israeli monse. Ngati sipapezeka wodzatipulumutsa, ndiye ife tidzadzipereka kwa iwe.”
4 Da Sendebudene kom til Sauls Gibea og forebragte Folket Sagen, brast hele Folket i Gråd.
Amithenga aja atafika kwawo kwa Sauli ku Gibeya ndi kufotokoza nkhaniyi kwa anthu onse, iwo analira motaya mtima.
5 Og se, Saul kom netop hjem med sine Okser fra Marken, og han spurgte: "Hvad er der i Vejen med Folket, siden det græder?" De fortalte ham da, hvad Mændene fra Jabesj havde sagt;
Pa nthawiyo nʼkuti Sauli akubwera kuchokera ku munda, ali pambuyo pa ngʼombe zake za ntchito ndipo anafunsa. “Nʼchiyani chawavuta anthuwa kuti azilira motere?” Ndipo anamufotokozera zomwe anthu a mu mzinda wa Yabesi ananena.
6 og da Saul hørte det, overvældede Guds Ånd ham, og hans Vrede blussede heftigt op.
Sauli atamva mawu awo, Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwa mphamvu ndipo anakwiya kwambiri.
7 Så tog han et Spand Okser og sønderhuggede dem, sendte Folk ud med Stykkerne i hele Israels Land og lod sige: "Hvis nogen ikke følger Saul og Samuel, skal der handles således med hans Okser!" Da faldt en HERRENs Rædsel over Folket, så de alle som een drog ud.
Tsono anatenga ngʼombe ziwiri za ntchito, nazidula nthulinthuli. Ndipo anatumiza amithenga ndi nthulizo dziko lonse la Israeli ndi mawu akuti, “Umo ndi mmene adzachite ndi ngʼombe ya aliyense amene satsata Sauli ndi Samueli.” Ndipo anthu anachita mantha aakulu motero kuti onse ananyamuka ndi mtima umodzi.
8 Og han mønstrede dem i Bezek, og der var 300000 Israeliter og 30000 Judæere.
Pamenepo Sauli anawasonkhanitsa ku Bezeki nawawerenga, ndipo Aisraeli analipo 300,000, Ayuda analipo 30,000.
9 Derpå sagde han til Sendebudene, som var kommet: "Således skal I sige til Mændene i Jabesj i Gilead: I Morgen, når Solen begynder at brænde, skal I få Hjælp!" Da Sendebudene kom og meddelte Mændene i Jabesj det, blev de glade.
Tsono Sauli anawuza amithenga ochokera ku Yabesi aja kuti, “Mukawawuze anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti mawa nthawi ya masana adzapulumutsidwa.” Pamene amithengawo anapita ndi kukafotokoza nkhani imeneyi kwa anthu a ku Yabesi, iwo anasangalala kwambiri.
10 Og Mændene i Jabesj sagde: "I Morgen vil vi overgive os til eder, så kan I gøre med os, hvad I finder for godt!"
Choncho anthu a ku Yabesi anawuza Nahasi kuti, “Mawa tidzadzipereka kwa inu ndipo inu mudzachite nafe chilichonse chokukomerani.”
11 Dagen efter delte Saul Hæren i tre Afdelinger, og de trængte ind i Lejren ved Morgenvagten og huggede ned blandt Ammoniterne, til det blev hedt; og de, som undslap, splittedes til alle Sider, så ikke to og to blev sammen.
Tsono mmawa mwake Sauli anagawa anthuwo mʼmagulu atatu. Mmamawa kusanache iwo analowa mʼmisasa ya Aamoni ndi kuwapha mpaka masana. Amene anapulumuka anabalalika, aliyense kwakekwake.
12 Da sagde Folket til Samuel: "Hvem var det, som sagde: Skal Saul være Konge over os? Bring os de Mænd, at vi kan slå dem ihjel!"
Kenaka anthu anafunsa Samueli kuti, “Kodi ndani aja ankanena kuti, ‘Kodi Sauli nʼkutilamulira ife?’ Bwera nawoni kuno kuti tidzawaphe.”
13 Men Saul sagde: "I Dag skal ingen slås ihjel; thi i Dag har HERREN givet Israel Sejr!"
Koma Sauli anati, “Palibe amene ati aphedwe lero, pakuti lero lino Yehova wagwira ntchito yopulumutsa Israeli.”
14 Da sagde Samuel til Folket: "Kom, lad os gå til Gilgal og gentage Kongevalget der!"
Ndipo Samueli anati kwa anthuwo, “Tiyeni tipite ku Giligala kuti tikatsimikizenso kuti Sauli ndi mfumu yathu.”
15 Så gik hele Folket til Gilgal og gjorde Saul til Konge for HERRENs Åsyn der i Gilgal, og de bragte Takofre der for Herrens Åsyn. Og Saul og alle Israels Mænd var højlig glade.
Choncho anthu onse anapita ku Giligala ndipo kumeneko Samueli anakalonga Sauli ufumu pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anthu anapereka nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova, ndipo Sauli ndi Aisraeli onse anachita chikondwerero chachikulu.