< Første Kongebog 15 >
1 I Kong Jeroboams, Nebats Søns, attende Regeringsår blev Abija Konge over Juda.
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Nebati, Abiya anakhala mfumu ya Yuda,
2 Tre År herskede han i Jerusalem. Hans Moder hed Ma'aka og var en datter af Absalom.
ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zitatu. Amayi ake anali Maaka, mwana wa Abisalomu.
3 Han vandrede i alle de Synder, hans Fader havde begået før ham, og hans Hjerte var ikke helt med HERREN hans Gud som hans Fader Davids.
Abiya anachita zoyipa zonse zimene abambo ake anazichita. Sanali wangwiro pamaso pa Yehova Mulungu wake, monga linachitira kholo lake Davide.
4 Men for Davids Skyld lod HERREN hans Gud ham få en Lampe i Jerusalem, idet han ophøjede hans Sønner efter ham og lod Jerusalem bestå,
Komabe chifukwa cha Davide, Yehova Mulungu wake anamupatsa nyale mu Yerusalemu pomupatsa mwana wolowa mʼmalo mwake ndi kumukhazikitsa kukhala wamphamvu mu Yerusalemu;
5 fordi David havde gjort, hvad der var ret i HERRENs Øjne, og ikke, så længe han levede, var veget fra noget af, hvad han havde pålagt ham, undtagen over for Hetiten Urias.
pakuti Davide anachita zolungama pamaso pa Yehova ndipo sanalephere kusunga chilichonse chimene Yehova anamulamula masiku onse a moyo wake kupatula nkhani ija ya Uriya Mhiti.
6 (Rehabeam lå i Krig med Jeroboam, så længe han levede).
Panali nkhondo pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu masiku onse a moyo wa Abiya.
7 Hvad der ellers er at fortælle om Abija, alt, hvad han gjorde, står jo optegnet i Judas Kongers Krønike. Abija og Jeroboam lå i Krig med hinanden.
Tsono ntchito zina za Abiya, ndi zina zonse anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
8 Så lagde Abija sig til Hvile hos sine Fædre, og man jordede ham i Davidsbyen; og hans Søn Asa blev Konge i hans Sted.
Ndipo Abiya anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Asa, mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
9 I Kong Jeroboam af Israels tyvende Regeringsår blev Asa Konge over Juda,
Mʼchaka cha makumi awiri cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Asa anakhala mfumu ya Yuda,
10 og han herskede een og fyrretyve År i Jerusalem. Hans Moder hed Ma'aka og var en Datter af Absalom.
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 41. Agogo ake akazi anali Maaka mwana wa Abisalomu.
11 Asa gjorde, hvad der var ret i HERRENs Øjne, ligesom hans Fader David;
Asa anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
12 han jog Mandsskøgerne ud af Landet og fjernede alle Afgudsbillederne, som hans Fædre havde ladet lave.
Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zadama pochita chipembedzo chawo ndiponso anachotsa mafano onse amene makolo ake anawapanga.
13 Han fratog endog sin Moder Ma'aka Værdigheden som Herskerinde, fordi hun havde ladet lave et Skændselsbillede til Ære for Asjera; Asa lod hendes Skændselsbillede nedbryde og brænde i Kedrons Dal.
Iye anachotsanso gogo wake Maaka pa udindo wake wa amayi a mfumu, chifukwa choti anapanga fano lonyansa la Asera. Asa anagwetsa fanolo nakalitentha ku Chigwa cha Kidroni.
14 Vel forsvandt Offerhøjene ikke, men alligevel var Asas Hjerte helt med HERREN, så længe han levede.
Ngakhale sanachotse malo opembedzerapo mafano, mtima wa Asa unali wodzipereka kwathunthu kwa Yehova masiku onse a moyo wake.
15 Og han bragte sin Faders og sine egne Helliggaver ind i HERRENs Hus, Sølv, Guld og forskellige Kar.
Asa anabweretsa ku Nyumba ya Yehova zinthu zimene abambo ake anazipereka, ndiponso zinthu zimene iye mwini anazipereka: zagolide, siliva ndi ziwiya zotengera.
16 Asa og Kong Basja af Israel lå i Krig med hinanden, så længe de levede.
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
17 Kong Basja af Israel drog op imod Juda og befæstede Rama for at hindre, at nogen af Kong Asa af Judas Folk drog ud og ind.
Baasa mfumu ya Israeli anapita kukathira nkhondo dziko la Yuda, ndipo anamangira linga mzinda wa Rama kuletsa kuti wina aliyense asatuluke kapena kulowa mʼdziko la Asa, mfumu ya Yuda.
18 Da tog Asa alt det Sølv og Guld, der var tilbage i Skatkamrene i HERRENs Hus og i Kongens Palads, overgav det til sine Folk og sendte dem til Kong Benhadad af Aram, en Søn af Hezjons Søn Tabrimmon, som boede i Damaskus, idet han lod sige:
Tsono Asa anatenga siliva yense pamodzi ndi golide zimene zinatsala ku malo osungira chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso ku nyumba yake yaufumu. Anazipereka kwa atumiki ake, nawatuma kupita nazo kwa Beni-Hadadi mwana wa Tabirimoni, mwana wa Heziyoni, mfumu ya Aramu, amene ankakhala ku Damasiko ndipo anakamuwuza kuti,
19 "Der består en Pagt mellem mig og dig, mellem min Fader og din Fader; her sender jeg dig en Gave af Sølv og Guld; bryd derfor din Pagt med Kong Basja af Israel, så at han nødes til at drage bort fra mig!"
“Tiyeni tigwirizane inu ndi ine, monga panali mgwirizano pakati pa abambo anu ndi abambo anga. Onani, ndikukutumizirani mphatso za siliva ndi golide. Tsopano kathetseni mgwirizano wanu ndi Baasa mfumu ya Israeli kuti andisiye.”
20 Benhadad gik ind på Kong Asas Forslag og sendte sine Hærførere mod Israels Byer og indtog Ijjon, Dan, Abel-Bet-Ma'aka og hele Kinnerot tillige med hele Naftalis Land.
Choncho Beni-Hadadi anamvera zimene ananena mfumu Asa ndipo anatumiza olamulira magulu ake ankhondo ku mizinda ya Israeli. Ndipo iye anagonjetsa Iyoni, Dani, Abeli-Beti-Maaka ndi dera lonse la Kinereti kuphatikiza dziko lonse la Nafutali.
21 Da Basja hørte det, opgav han at befæste Rama og vendte tilbage til Tirza.
Baasa atamva zimenezi, anasiya kumangira linga Rama ndipo anakakhala ku Tiriza.
22 Men Kong Asa stævnede hver eneste Mand i hele Juda sammen, og de førte Stenene og Træværket bort, som Basja havde brugt ved Befæstningen af Rama; dermed befæstede Kong Asa så Geba i Benjamin og Mizpa.
Pamenepo Mfumu Asa analamula anthu onse a ku Yuda osasiya ndi mmodzi yemwe, ndipo anachotsa ku Rama miyala ndi matabwa amene Baasa ankamangira kumeneko. Zipangizo zimenezi Mfumu Asa inamangira linga la Geba ku Benjamini ndi la ku Mizipa.
23 Hvad der ellers er at fortælle om Asa, alle hans Heltegerninger, alt, hvad han gjorde, og de Byer, han befæstede, står jo optegnet i Judas Kongers Krønike. I øvrig led han i sin Alderdom af en Sygdom i Fødderne.
Tsono ntchito zina za Asa, za mphamvu zake ndi mizinda imene anayimanga ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? Koma pa nthawi ya ukalamba wake anadwala nthenda ya mapazi.
24 Så lagde han sig til Hvile hos sine Fædre og blev jordet hos sine Fædre i sin Fader Davids By; og hans Søn Josafat blev Konge i hans Sted.
Ndipo Asa anamwalira nayikidwa mʼmanda momwe anayikidwa makolo ake mu mzinda wa Davide kholo lake. Ndipo Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
25 Nadab, Jeroboams Søn, blev Konge over Israel i Kong Asa af Judas andet Regeringsår, og han herskede to År over Israel.
Nadabu, mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli mʼchaka chachiwiri cha Asa mfumu ya Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri.
26 Han gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne, og vandrede i sin Faders Spor og i de Synder, han havde forledt Israel til.
Nadabu anachita zoyipa pamaso pa Yehova, anayenda mʼnjira za abambo ake ndi mu uchimo womwe anachimwitsa nawo Israeli.
27 Da stiftede Basja, Ahijas Søn af Issakars Hus, en Sammensværgelse imod ham, og Basja huggede ham ned ved Gibbeton, der tilhørte Filisterne, medens Nadab og hele Israel belejrede Byen.
Baasa mwana wa Ahiya, wa banja la Isakara anakonzera Nadabuyo chiwembu, ndipo anamukantha ku Gibetoni, mzinda wa Afilisti, pamene Nadabu ndi anthu onse a ku Israeli anali atawuzungulira.
28 Basja dræbte ham i Kong Asa af Judas tredje Regeringsår og blev Konge i hans Sted;
Baasa anapha Nadabu mʼchaka chachitatu cha Asa, mfumu ya ku Yuda ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 nu da han var blevet Konge, lod han hele Jeroboams Hus nedhugge, idet han ikke skånede en eneste Sjæl af Jeroboams Slægt, men udryddede dem efter det Ord, HERREN havde talet ved sin Tjener Ahija fra Silo,
Iye atangoyamba kulamulira, anapha anthu onse a banja la Yeroboamu. Sanasiye ndi mmodzi yemwe wamoyo pa banjapo, koma anawononga anthu onse, molingana ndi mawu a Yehova amene anayankhula mwa mtumiki wake Ahiya wa ku Silo
30 for de Synders Skyld, Jeroboam havde begået og forledt Israel til, for den Krænkelse, han havde tilføjet HERREN, Israels Gud.
chifukwa cha machimo amene Yeroboamu anachita, ndiponso kuchimwitsa anthu a ku Israeli, naputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israeli.
31 Hvad der ellers er at fortælle om Nadab, alt, hvad han gjorde, står jo optegnet i Israels Kongers Krønike
Tsono ntchito za Nadabu ndi zina zonse zimene anazichita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
32 ( Asa og kong Ba'sja af Israel lå i Krig med hinanden, så længe de levede.)
Panali nkhondo pakati pa Asa ndi Baasa mfumu ya Israeli pa nthawi yonse ya ulamuliro wawo.
33 I Kong Asa af Judas tredje Regeringsår blev Basja, Ahijas Søn, Konge over hele Israel, og han herskede tre og tyve År i Tirza.
Chaka chachitatu cha Asa mfumu ya Yuda, Baasa mwana wa Ahiya anakhala mfumu ya Aisraeli onse ku Tiriza, ndipo analamulira zaka 24.
34 Han gjorde, hvad der var ondt i HERRENs Øjne, og vandrede i Jeroboams Spor og de Synder, han havde forledt Israel til.
Anachita zoyipa pamaso pa Yehova, nayenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchita tchimo lake limene linachimwitsa anthu a ku Israeli.