< Første Krønikebog 28 >
1 Derpå samlede David i Jerusalem alle Israels Øverster, Stammeøversterne, Skifternes Øverster, som var i Kongens Tjeneste, Tusind- og Hundredførerne, Overopsynsmændene over alle Kongens og hans Sønners Ejendele og Kvæg, ligeledes Hofmændene, Kærnetropperne og alle dygtige Krigere.
Davide anayitana akuluakulu onse a Israeli kuti asonkhane ku Yerusalemu: akuluakulu a mafuko, olamulira magulu a ntchito ya mfumu, olamulira ankhondo 1,000, ndi olamulira ankhondo 100, ndiponso akuluakulu onse osunga katundu ndi ziweto za mfumu ndi ana ake, pamodzinso ndi akuluakulu a ku nyumba yaufumu, anthu amphamvu ndi asilikali onse olimba mtima.
2 Kong David rejste sig op og sagde: "Hør mig, mine Brødre og mit Folk! Jeg havde i Sinde at bygge HERRENs Pagts Ark og vor Guds Fodskammel et Hus at hvile i og havde truffet forberedelser til at bygge.
Mfumu Davide inayimirira ndipo inati: “Tamverani abale anga ndi anthu anga. Ine ndinali ndi maganizo omanga nyumba monga malo okhalamo Bokosi la Chipangano la Yehova, malo oyikapo mapazi a Mulungu wathu, ndipo ndinakonza ndondomeko yomangira nyumbayo.”
3 Men Gud sagde til mig: Du skal ikke bygge mit Navn et Hus, thi du er en Krigens Mand og har udgydt Blod!
Koma Mulungu anati kwa ine, “Usandimangire nyumba chifukwa ndiwe munthu wankhondo ndipo wakhala ukukhetsa magazi.”
4 Af mit Fædrenehus udvalgte HERREN, Israels Gud, ene mig til Konge over Israel evindelig, thi han udvalgte Juda til Fyrste og af Juda mit Fædrenehus, og mellem min Faders Sønner fandt han Behag i mig, så han gjorde mig til Konge over hele Israel.
“Komabe Yehova Mulungu wa Israeli anasankha ine pakati pa onse a banja langa kukhala mfumu ya Israeli kwamuyaya. Iye anasankha Yuda kukhala mtsogoleri, ndipo pa banja la Yuda anasankha banja langa. Pakati pa ana aamuna a abambo anga, kunamukomera Iye kundikhazika mfumu ya Aisraeli onse.
5 Og af alle mine Sønner - HERREN har givet mig mange Sønner har han udvalgt min Søn Salomo til at sidde på HERRENs Kongetrone og herske over Israel.
Pa ana anga ambiri onse amene Yehova wandipatsa, Iye wasankha mwana wanga Solomoni kuti akhale pa mpando waufumu wa ufumu wa Yehova kuti alamulire Israeli.”
6 Og han sagde til mig: Din Søn Salomo er den, som skal bygge mit Hus og mine Forgårde, thi ham har jeg udvalgt til min Søn, og jeg vil være ham en Fader;
Yehova anati kwa ine, “Solomoni mwana wako ndiye amene adzamanga nyumba yanga ndi mabwalo anga, pakuti Ine ndamusankha kuti akhale mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake.
7 jeg vil grundfæste hans Kongedømme til evig Tid, hvis han holder fast ved mine Bud og Lovbud og gør efter dem således som nu.
Ine ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya ngati iye saleka kutsatira malamulo ndi malangizo anga, monga momwe zikuchitikira leromu.”
8 Og nu, for hele Israels, HERRENs Forsamlings, Øjne og i vor Guds Påhør siger jeg: Stræb at holde alle HERREN eders Guds Bud, at I må eje dette herlige Land og lade det gå i Arv til eders Efterkommere til evig Tid!
“Tsono lero ine ndikulamula inu pamaso pa Aisraeli onse ndi pa msonkhano wa Yehova, ndipo Mulungu wathu akumva: Mutsatire mosamala malamulo a Yehova Mulungu wathu, kuti dziko labwinoli likhale lanu ndi kuti mudzalipereke kwa zidzukulu zanu kukhala cholowa chawo kwamuyaya.”
9 Og du, min Søn Salomo! Kend din Faders Gud og tjen ham med et helt Hjerte og en villig Sjæl, thi HERREN ransager alle Hjerter og kender alt, hvad der rører sig i deres Tanker. Hvis du søger ham, vil han lade sig fmde af dig, men forlader du ham, vil han forkaste dig for evigt.
“Ndipo iwe mwana wanga Solomoni, umvere Mulungu wa abambo ako, umutumikire ndi mtima wodzipereka kwathunthu ndi mtima wako wonse, pakuti Yehova amasanthula mtima wa aliyense, ndipo amadziwa maganizo aliwonse a munthu. Ngati ufunafuna Yehova, Iye adzapezeka; koma ngati umutaya, Iye adzakukana kwamuyaya.
10 Så se da til, thi HERREN har udvalgt dig til at bygge et Hus til Helligdom! Gå til Værket med Frimodighed!"
Tsopano ganizira bwino, pakuti Yehova wakusankha iwe kuti umange Nyumba ya Mulungu monga malo ake opatulika. Khala wamphamvu ndipo ugwire ntchito.”
11 Derpå gav David sin Søn Salomo Planen til Forhallen, Templets Bygninger, Forrådskamrene, Rummene på Taget, de indre Kamre og Hallen til Sonedækket
Kotero Davide anapatsa Solomoni mwana wake mapulani a khonde la Nyumba ya Mulungu, nyumba zake, mosungiramo katundu, zipinda zake zamʼmwamba, zipinda zamʼkati ndi malo a nsembe zopepesera machimo.
12 og Planen til alt, hvad der stod for hans Tanke med Hensyn til HERRENs Hus's Forgårde og alle Kamrene rundt om, Guds Hus's Skatkamre og Skatkamrene til Helliggaverne,
Iye anapatsa Solomoni mapulani a zonse zimene ankaziganizira za bwalo la Nyumba ya Yehova ndi zipinda zonse zozungulira, zipinda zosungiramo chuma cha Nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Yehova.
13 fremdeles Anvisninger om Præsternes og Leviternes Skifter og alt Arbejdet ved Tjenesten i HERRENs Hus og alting, som hørte til Tjenesten i HERRENs Hus,
Davide anamulangiza za magulu a ansembe ndi Alevi ndi ntchito yonse yotumikira mʼNyumba ya Yehova, komanso za zinthu zonse zogwirira ntchito potumikira.
14 om Guldet, den Vægt, der skulde til hver enkelt Ting, som hørte til Tjenesten, og om alle Sølvtingene, den Vægt, der skulde til hver enkelt Ting, som hørte til Tjenesten,
Iye anakonzeratu za kulemera kwa golide wopangira zida zonse zagolide zogwirira ntchito zosiyanasiyana, ndiponso kulemera kwa siliva wopangira zida zonse zasiliva zogwirira ntchito zosiyanasiyana:
15 fremdeles om Vægten på Guldlysestagerne og deres Guldlamper, Vægten på hver enkelt Lysestage og dens Lamper, og på Sølvlysestagerne, Vægten på hver enkelt Lysestage og dens Lamper, svarende til hver enkelt Lysestages Brug ved Tjenesten,
kulemera kwa golide wopangira choyikapo nyale chagolide ndi nyale zake; ndiponso kulemera kwa siliva wa choyikapo nyale chilichonse ndi nyale zake, molingana ndi kagwiritsidwe ka choyikapo nyale chilichonse;
16 fremdeles om Vægten på Guldet til Skuebrødsbordene, til hvert enkelt Skuebrødsbord, og på Sølvet til Sølvbordene
kulemera kwa golide wa tebulo iliyonse yoyikapo buledi wopatulika; kulemera kwa siliva wopangira matebulo asiliva;
17 og om Gaflerne, Skålene og Krukkerne af purt Guld og om Guldbægrene, Vægten på hvert enkelt Bæger, og Sølvbægrene, Vægten på hvert enkelt Bæger,
muyeso wa golide woyengeka bwino wopangira mafoloko, mbale ndi zotungira; muyeso wa golide wa beseni lililonse la siliva;
18 øg om Vægten på Røgofferalteret af purt Guld og om Tegningen til Vognen, til Guldkeruberoe, som udbredte Vingerne skærmende over HERRENs Pagts Ark.
ndiponso muyeso wa golide wabwino wopangira guwa la zofukiza. Davide anamupatsanso ndondomeko ya mapangidwe a galeta, akerubi agolide atatambasula mapiko awo kuphimba Bokosi la Chipangano la Yehova.
19 "HERREN har sat mig ind i alt dette ved et Skrift, jeg har fra hans egen Hånd, i alle de Arbejder, Planen omfatter."
Davide anati, “Zonsezi ndalemba kuchokera kwa Yehova, ndipo Iye wachita kuti ndimvetsetse zonse za mapulaniwa.”
20 Derpå sagde David til sin Søn Salomo: "Gå til Værket og vær frimodig og stærk, frygt ikke og tab ikke Modet, thi Gud HERREN, min Gud, vil være med dig! Han vil ikke slippe dig og ikke forlade dig, før alt Arbejdet med HERRENs Hus er fuldført.
Davide anatinso kwa mwana wake Solomoni, “Khala wamphamvu ndi wolimba mtima ndipo uchite ntchitoyi. Usachite mantha kapena kutaya mtima pakuti Yehova Mulungu wanga ali nawe. Iye sadzakukhumudwitsa kapena kukusiya mpaka ntchito yonse ya Nyumba ya Mulungu itatha.
21 Se, Præsternes og Leviternes Skifter er rede til alt Arbejdet ved Guds Hus; og til alt, hvad der skal udføres, har du Folk hos dig, der alle er villige og forstår sig på Arbejder af enhver Art, og Øversterne og hele Folket er rede til alt, hvad du kræver."
Magulu a ansembe ndi Alevi ndi okonzeka kugwira ntchito ya Nyumba ya Mulungu, ndipo munthu waluso aliyense wodzipereka adzakuthandiza pa ntchito yonse. Akuluakulu ndi anthu onse adzamvera chilichonse chomwe udzalamula.”