< Aabenbaringen 5 >

1 ag jeg saa i hans højre Haand, som sad paa Tronen, en Bog, beskreven indeni og udenpaa, forseglet med syv Segl.
Kenaka ndinaona buku mʼdzanja la wokhala pa mpando waufumu uja. Bukulo linali lolembedwa mbali zonse ndipo linali lomatidwa ndi zomatira zisanu ndi ziwiri.
2 Og jeg saa en vældig Engel, som udraabte med høj Røst: Hvem er værdig til at aabne Bogen og bryde dens Segl?
Ndipo ndinaona mngelo wamphamvu akulengeza ndi mawu okweza kuti, “Ndani ali woyenera kumatula zomatira ndi kufutukula bukuli?”
3 Og ingen i Himmelen, ej heller paa Jorden, ej heller under Jorden, formaaede at aabne Bogen eller at se i den.
Koma panalibe ndi mmodzi yemwe kumwamba kapena pa dziko lapansi kapena kunsi kwa dziko lapansi woti afutukule bukulo kapena kuona zamʼkati mwake.
4 Og jeg græd saare, fordi ingen fandtes værdig til at aabne Bogen eller at se i den.
Ndinalira kwambiri chifukwa panalibe amene anapezeka woyenera kufutukula bukuli kapena kuona zamʼkati mwake.
5 Og en af de Ældste sagde til mig: Græd ikke! se, sejret har Løven af Judas Stamme, Davids Rodskud, saa han kan aabne Bogen og dens syv Segl.
Tsono mmodzi mwa akuluakulu aja anati kwa ine, “Usalire! Taona, Mkango wa fuko la Yuda, Muzu wa Davide, wapambana. Iye angathe kufutukula bukuli ndi kumatula zomatira zisanu ndi ziwirizo.”
6 Og jeg saa, midt imellem Tronen med de fire Væsener og de Ældste stod et Lam, ligesom slagtet: Det havde syv Horn og syv Øjne, hvilke ere de syv Guds Aander, som ere udsendte til hele Jorden.
Kenaka ndinaona Mwana Wankhosa akuoneka ngati wophedwa atayimirira pakatikati pa mpando waufumu uja ndi zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu aja. Mwana Wankhosayo anali ndi nyanga zisanu ndi ziwiri ndi maso asanu ndi awiri omwe ndi Mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu yomwe anayitumiza ku dziko lonse lapansi.
7 Og det kom og tog Bogen af hans højre Haand, som sad paa Tronen.
Iye anabwera natenga buku lija limene linali mʼdzanja lamanja la wokhala pa mpando waufumuyo.
8 Og da det tog Bogen, faldt de fire Væsener og de fire og tyve Ældste ned for Lammet, holdende hver sin Harpe og Guldskaaler fyldte med Røgelse, som er de helliges Bønner.
Ndipo atalitenga, zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu 24 aja anadzigwetsa pansi pamaso pa Mwana Wankhosa. Aliyense wa akuluakuluwo anali ndi zeze ndiponso mbale zagolide zodzaza ndi lubani. Lubaniyo ndi mapemphero a oyera mtima.
9 Og de sang en ny Sang og sagde: Du er værdig til at tage Bogen og aabne dens Segl, fordi du blev slagtet og med dit Blod købte til Gud Mennesker af alle Stammer og Tungemaal og Folk og Folkeslag,
Ndipo ankayimba nyimbo yatsopano yakuti, “Inu ndinu woyenera kulandira bukuli ndi kumatula zomatira zake, chifukwa munaphedwa, ndipo magazi anu munagulira Mulungu anthu a fuko lililonse, a chiyankhulo chilichonse, ndi mtundu uliwonse.
10 og du har gjort dem for vor Gud til et Kongerige og til Præster, og de skulle være Konger paa Jorden.
Inu munawasandutsa kukhala mtundu waufumu ndi ansembe otumikira Mulungu, ndipo adzalamulira dziko lapansi.”
11 Og jeg saa, og jeg hørte rundt om Tronen og Væsenerne og de Ældste en Røst af mange Engle, og deres Tal var Titusinder Gange Titusinder, og Tusinder Gange Tusinder,
Kenaka nditayangʼananso ndinamva mawu a angelo ambiri, miyandamiyanda kuchulukitsa ndi miyandamiyanda. Anazungulira mpando waufumu pamodzi ndi zamoyo zija ndi akuluakulu aja.
12 og de sagde med høj Røst: Værdigt er Lammet, det slagtede, til at faa Kraften og Rigdom og Visdom og Styrke og Ære og Pris og Velsignelse!
Ndipo angelowo anayimba ndi mawu ofuwula akuti, “Mwana Wankhosa amene anaphedwayu ndi woyenera kulandira ulamuliro, chuma, nzeru, mphamvu, ulemu, ulemerero ndi mayamiko.”
13 Og hver Skabning, som er i Himmelen og paa Jorden og under Jorden og paa Havet, ja, alt, hvad der er i dem, hørte jeg sige: Ham, som sidder paa Tronen, og Lammet tilhører Velsignelsen og Æren og Prisen og Magten i Evighedernes Evigheder! (aiōn g165)
Kenaka ndinamva mawu a cholengedwa chilichonse kumwamba, pa dziko lapansi, kunsi kwa dziko lapansi, pa nyanja ndi zonse zili mʼmenemo zikuyimba kuti, “Kwa wokhala pa mpando waufumu ndi kwa Mwana Wankhosa, kukhale mayamiko, ulemu, ulemerero ndi mphamvu (aiōn g165)
14 Og de fire Væsener sagde: Amen! Og de Ældste faldt ned og tilbade.
Zamoyo zinayi zija zinati: “Ameni,” ndipo akuluakulu aja anadzigwetsa pansi napembedza.

< Aabenbaringen 5 >