< Aabenbaringen 3 >

1 Og skriv til Menighedens Engel i Sardes: Dette siger han, som har de syv Guds Aander og de syv Stjerner: Jeg kender dine Gerninger, at da har Ord for at leve og er dog død.
“Lembera mngelo wampingo wa ku Sarde kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene amasunga mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri. Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zako; umadziwika kuti ndiwe wamoyo koma ndiwe wakufa.
2 Bliv vaagen og styrk det øvrige, som ellers vilde dø; thi jeg har ikke fundet dine Gerninger fuldkommede for min Gud.
Dzuka! Limbitsa zimene zatsalira zomwe zatsala pangʼono kufa, pakuti ndaona kuti ntchito zako nʼzosakwanira pamaso pa Mulungu.
3 Kom derfor i Hu, hvorledes du modtog og hørte, og bevar det og omvend dig! Dersom du altsaa ikke vaager, skal jeg komme som en Tyv, og du skal ikke vide, i hvilken Time jeg kommer over dig.
Choncho, kumbukira zimene unalandira ndi kumva; uzisunge ndipo ulape. Koma ngati sudzuka, ndidzabwera ngati mbala ndipo sudzadziwa nthawi imene ndidzabwere kwanu.
4 Dog har du i Sardes nogle faa Personer, som ikke have besmittet deres Klæder; de skulle vandre med mig i hvide Klæder, thi de ere værdige dertil.
Komabe uli ndi anthu angapo mu Sarde amene sanadetse zovala zawo. Amenewa adzayenda ndi Ine atavala zoyera popeza ndi oyenera kutero.
5 Den, som sejrer, han skal saaledes iføres hvide Klæder, og jeg vil ikke udslette hans Navn af Livets Bog, og jeg vil bekende hans Navn for min Fader og for hans Engle.
Amene adzapambane adzavala zoyera ngati ena aja. Sindidzafafaniza dzina lake mʼbuku lamoyo, koma ndidzamuchitira umboni pamaso pa Atate anga ndi angelo ake.
6 Den, som har Øre, høre, hvad Aanden siger til Menighederne!
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.”
7 Og skriv til Menighedens Engel i Filadelfia: Dette siger den hellige, den sanddru, han, som har Davids Nøgle, han, som lukker op, saa ingen lukker i, og lukker i, saa ingen lukker op:
“Lembera mngelo wampingo wa ku Filadefiya kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi woyera ndi woonadi, amene ali ndi kiyi ya Davide. Iye akatsekula palibe amene angatseke; ndipo akatseka palibe amene angatsekule.
8 Jeg kender dine Gerninger. Se, jeg har givet dig, at der foran dig er en aabnet Dør, som ingen kan lukke; thi du har kun liden Kraft, og dog har du bevaret mit Ord og ikke fornægtet mit Navn.
Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa ntchito zako. Taona, ndakutsekulira pa khomo ndipo palibe wina amene angatseke. Ndikudziwa kuti uli ndi mphamvu zochepa komabe wasunga mawu anga ndipo sunandikane.
9 Se, jeg lader komme nogle af Satans Synagoge, som kalde sig selv Jøder og ikke ere det, men lyve. Se, jeg vil gøre, at de skulle komme og tilbede for dine Fødder og kende, at jeg har fattet Kærlighed til dig.
Amene ndi mpingo wa Satana, amene amadzitcha kuti ndi Ayuda pamene sali choncho, koma ndi onama, ndidzawabweretsa kwa inu ndi kuwagwetsa pansi pa mapazi anu kuti adzazindikire kuti ndimakukondani.
10 Efterdi du har bevaret mit Ord om Udholdenheden, vil ogsaa jeg bevare dig ud af Fristelsens Stund, som skal komme over hele Jorderige for at friste dem, som bo paa Jorden.
Popeza mwasunga mawu anga woti mupirire ndipo mwawugwira mtima, Inenso ndidzakupulumutsani nthawi ya mayesero imene idzabwera pa dziko lonse lapansi kuyesa onse okhala pa dziko lapansi.
11 Jeg kommer snart! Hold fast ved det, du har, for at ingen skal tage din Krone.
Ine ndikubwera msanga. Gwiritsitsa chimene uli nacho kuti wina angakulande chipewa chako chaufumu.
12 Den, som sejrer, ham vil jeg gøre til en Søjle i min Guds Tempel, og han skal ikke mere gaa ud derfra; og jeg vil skrive paa ham min Guds Navn og min Guds Stads Navn, det nye Jerusalem, der kommer ned fra Himmelen fra min Gud, og mit nye Navn.
Iye amene adzapambane ndidzamusandutsa mzati wa mʼNyumba ya Mulungu wanga. Sadzatulukamonso. Pa iye ndidzalemba dzina la Mulungu wanga ndi dzina la mzinda wa Mulungu wanga, Yerusalemu watsopano, umene ukubwera pansi kuchokera kumwamba kwa Mulungu wanga; ndipo pa iye ndidzalembanso dzina langa latsopano.
13 Den, som har Øre, høre, hvad Aanden siger til Menighederne!
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.’”
14 Og skriv til Menighedens Engel i Laodikea: Dette siger han, som er Amen, det troværdige og sanddru Vidne, Guds Skabnings Begyndelse:
“Lembera mngelo wampingo wa ku Laodikaya kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa Ameni, mboni yokhulupirika ndi yoona, gwero la zolengedwa zonse za Mulungu.
15 Jeg kender dine Gerninger, at du hverken er kold eller varm; gid du var kold eller varm!
Ine ndimadziwa ntchito zako, kuti sindiwe wozizira kapena wotentha. Ndikanakonda ukanakhala wozizira kapena wotentha!
16 Derfor, efterdi du er lunken og hverken varm eller kold, vil jeg udspy dig af min Mund;
Tsono popeza ndiwe wofunda chabe, sindiwe wotentha kapena wozizira, ndatsala pangʼono kuti ndikulavule mʼkamwa mwanga.
17 fordi du siger: Jeg er rig og har vundet Rigdom og fattes intet; og du ved ikke, at du er den elendige og jammerlige og fattige og blinde og nøgne.
Iwe umati: ‘Ndine wolemera, ndine wachuma ndipo sindisowa kanthu.’ Koma sudziwa kuti ndiwe wovutika, womvetsa chisoni, waumphawi, wosaona ndi wamaliseche.
18 Jeg raader dig, at du af mig køber Guld, lutret i Ilden, for at du kan blive rig, og hvide Klæder, for at du kan klæde dig dermed, og din Nøgenheds Skam ikke skal blottes, og Øjensalve til at salve dine Øjne med, for at du kan se.
Ndikukulangiza kuti ugule kwa Ine golide woyengedwa ndi moto kuti ukhale wolemera. Ugule zovala zoyera kuti uvale ndi kuphimba umaliseche wako wochititsa manyaziwo. Ndiponso ugule kwa Ine mankhwala a mʼmaso kuti uwone.
19 Alle dem, jeg elsker, dem revser og tugter jeg; vær derfor nidkær og omvend dig!
Amene ndimawakonda ndimawadzudzula ndi kuwalanga. Choncho chita changu ndipo lapa.
20 Se, jeg staar for Døren og banker; dersom nogen hører min Røst og aabner Døren, vil jeg gaa ind til ham og holde Nadvere med ham, og han med mig.
Taonani ndayima pa khomo ndikugogoda. Ngati wina amva mawu anga natsekula chitseko, Ine ndidzalowamo ndi kudya naye, Ine ndi iyeyo.
21 Den, som sejrer, ham vil jeg give at tage Sæde hos mig paa min Trone, ligesom jeg har sejret og har taget Sæde hos min Fader paa hans Trone.
Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wokhala nane pamodzi pa mpando wanga waufumu monga mmene Ine ndinapambana ndi kukhala pansi ndi Atate anga pa mpando wawo waufumu.
22 Den, som har Øre, høre, hvad Aanden siger til Menighederne!
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.”

< Aabenbaringen 3 >