< Aabenbaringen 11 >

1 Og der blev givet mig et Rør ligesom en Maalestok, med de Ord: Staa op og maal Guds Tempel og Alteret og dem, som tilbede deri.
Ndinapatsidwa bango longa ndodo yoyezera ndipo ndinawuzidwa kuti, “Pita, kayeze Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, ndipo ukawerenge anthu opembedza mʼNyumbamo.
2 Men Forgaarden uden for Templet, lad den ude og maal den ikke, thi den er given til Folkeslagene; og de skulle nedtræde den hellige Stad i to og fyrretyve Maaneder.
Koma bwalo lakunja ulisiye, usaliyeze chifukwa linaperekedwa kwa a mitundu ina. Iwo adzawupondereza mzinda woyerawo kwa miyezi 42.
3 Og jeg vil give mine tvende Vidner, at de skulle profetere eet Tusinde, to Hundrede og tresindstyve Dage, klædte i Sække.
Ndipo ndidzapereka mphamvu kwa mboni zanga ziwiri, zitavala ziguduli, ndipo kwa masiku 1,260 zidzakhala zikulalikira.”
4 Disse ere de tvende Olietræer og de tvende Lysestager, som staa for Jordens Herre.
Mboni ziwirizo ndi mitengo iwiri ya olivi ndi zoyikapo nyale ziwiri zija zimene zili pamaso pa Ambuye wa dziko lapansi.
5 Og dersom nogen vil gøre dem Skade, udgaar der Ild af deres Mund og fortærer deres Fjender; og dersom nogen vil gøre dem Skade, bør han saaledes ihjelslaas.
Ngati wina atafuna kuzipweteka mbonizo, moto umatuluka mʼkamwa mwawo ndikuwononga adani awo.
6 Disse have Magt til at lukke Himmelen, saa at der ingen Regn skal falde i deres Profetis Dage; og de have Magt over Vandene til at forvandle dem til Blod og til at slaa Jorden med alskens Plage, saa ofte de ville.
Mbonizo zili ndi mphamvu yomanga mvula kuti isagwe pa nthawi imene akulalikirayo; ndipo zili ndi mphamvu yosanduliza madzi kukhala magazi ndi yokantha dziko lapansi ndi miliri ya mitundumitundu nthawi iliyonse imene zingafune.
7 Og naar de faa fuldendt deres Vidnesbyrd, skal Dyret, som stiger op af Afgrunden, føre Krig imod dem og overvinde dem og ihjelslaa dem. (Abyssos g12)
Tsono zikadzatsiriza umboni wawowo, chirombo chotuluka mʼChidzenje chakuya chija chidzachita nawo nkhondo nʼkuzigonjetsa mpaka kuzipha. (Abyssos g12)
8 Og deres Lig skal ligge paa Gaden i den store Stad, som i aandelig Forstand kaldes Sodoma og Ægypten, der, hvor ogsaa deres Herre blev korsfæstet.
Mitembo yawo idzakhala ili gone pabwalo la mu mzinda waukulu umene mozimbayitsa umatchedwa Sodomu ndi Igupto, kumenenso Ambuye wawo anapachikidwako.
9 Og Mennesker af alle Folk og Stammer og Tungemaal og Folkeslag skulle se paa deres Lig i tre og en halv Dag og ikke tilstede, at deres Lig lægges i Grav.
Kwa masiku atatu ndi theka, anthu ochokera ku mtundu uliwonse, fuko lililonse, chiyankhulo chilichonse ndi dziko lililonse, azidzayangʼanitsitsa mitembo yawoyo koma adzakana kuyikwirira.
10 Og de, som bo paa Jorden, glæde sig over dem og fryde sig; og de sende hverandre Gaver, fordi disse to Profeter vare til Plage for dem, som bo paa Jorden.
Anthu okhala pa dziko lapansi adzasangalala nazo zimenezi. Adzachita chikondwerero ndi kutumizirana mphatso, chifukwa aneneri awiri amenewa ankasautsa anthu okhala pa dziko lapansi.
11 Og efter de tre og en halv Dags Forløb kom der Livs Aande fra Gud i dem; og de stode paa deres Fødder, og stor Frygt faldt paa dem, som saa dem.
Koma patapita masiku atatu ndi theka aja, mpweya wopatsa moyo wochoka kwa Mulungu unalowa mwa aneneriwo, ndipo anayimirira, ndipo amene anawaona anachita mantha aakulu.
12 Og de hørte en høj Røst fra Himmelen, som sagde til dem: Stiger her op! Og de stege op til Himmelen i Skyen, og deres Fjender derpaa.
Kenaka aneneri aja anamva mawu ofuwula ochokera kumwamba owawuza kuti, “Bwerani kuno.” Ndipo anapitadi kumwamba mu mtambo adani awo aja akuwaona.
13 Og i samme Stund skete der et stort Jordskælv, og Tiendedelen af Staden faldt, og syv Tusinde Personer bleve dræbte i Jordskælvet; og de andre bleve forfærdede og gave Himmelens Gud Ære.
Nthawi yomweyo panachitika chivomerezi choopsa mwakuti chigawo chimodzi cha magawo khumi a mzinda chinagwa. Anthu 7,000 anaphedwa ndi chivomerezicho, ndipo opulumukawo anachita mantha kwambiri nayamba kutamanda Mulungu wakumwamba.
14 Det andet Ve er til Ende; se, det tredje Ve kommer snart.
Tsoka lachiwiri lapita; koma tsoka lachitatu likubwera posachedwapa.
15 Og den syvende Engel basunede, og der hørtes høje Røster i Himmelen, som sagde: Herredømmet over Verden er blevet vor Herres og hans Salvedes, og han skal være Konge i Evighedernes Evigheder. (aiōn g165)
Mngelo wachisanu ndi chiwiri anawomba lipenga lake, ndipo kumwamba kunamveka mawu ofuwula amene anati, “Ufumu wa dziko lapansi uli mʼmanja mwa Ambuye athu ndi Khristu wake uja, ndipo adzalamulira mpaka muyaya.” (aiōn g165)
16 Og de fire og tyve Ældste, som sidde for Guds Aasyn paa deres Troner, faldt ned paa deres Ansigter og tilbade Gud og sagde:
Ndipo akuluakulu 24 aja okhala pa mipando yawo yaufumu pamaso pa Mulungu, anadzigwetsa chafufumimba napembedza Mulungu
17 Vi takke dig, Herre Gud, almægtige, du, som er, og som var, fordi du har taget din store Magt og tiltraadt dit Kongedømme,
Iwo anati, “Ife tikuyamika Inu Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse, amene mulipo ndipo munalipo, chifukwa mwaonetsa mphamvu yanu yayikulu, ndipo mwayamba kulamulira.
18 og Folkeslagene vrededes, og din Vrede kom og Tiden til, at de døde skulle dømmes, og til at give Lønnen til dine Tjenere, Profeterne, og de hellige og dem, som frygte dit Navn, de smaa og de store, og til at ødelægge dem, som lægge Jorden øde.
A mitundu ina anapsa mtima; koma yafika nthawi yoonetsa mkwiyo. Nthawi yakwana yoweruza anthu akufa, yopereka mphotho kwa atumiki anu, aneneri, anthu oyera mtima anu ndi amene amaopa dzina lanu, wamngʼono pamodzi ndi wamkulu yemwe. Yafika nthawi yowononga amene awononga dziko lapansi.”
19 Og Guds Tempel i Himmelen blev aabnet, og hans Pagts Ark kom til Syne i hans Tempel, og der kom Lyn og Røster og Tordener og Jordskælv og stærk Hagel.
Pamenepo anatsekula Nyumba ya Mulungu kumwamba ndipo mʼkati mwake munaoneka Bokosi la Chipangano. Kenaka kunachita mphenzi, phokoso, mabingu, chivomerezi ndipo kunachita mkuntho wamatalala akuluakulu.

< Aabenbaringen 11 >